Masalimo 132 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 132:1-18

Salimo 132

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Inu Yehova, kumbukirani Davide

ndi mavuto onse anapirira.

2Iye analumbira kwa Yehova

ndi kulonjeza kwa Wamphamvu wa Yakobo kuti,

3“Sindidzalowa mʼnyumba mwanga

kapena kugona pa bedi langa:

4sindidzalola kuti maso anga agone,

kapena zikope zanga ziwodzere,

5mpaka nditamupezera malo Yehova,

malo okhala a Wamphamvu wa Yakobo.”

6Zoonadi, tinamva za Bokosi la Chipangano ku Efurata,

tinalipeza mʼminda ya ku Yaara:

7“Tiyeni tipite ku malo ake okhalamo;

tiyeni tikamulambire pa mapazi ake.

8‘Dzukani Yehova, ndipo bwerani ku malo anu opumulira,

Inuyo ndi Bokosi la Chipangano limene limafanizira mphamvu zanu.

9Ansembe anu avekedwe chilungamo;

anthu anu oyera mtima ayimbe nyimbo mwachimwemwe.’ ”

10Chifukwa cha Davide mtumiki wanu,

musakane wodzozedwa wanu.

11Yehova analumbira kwa Davide,

lumbiro lotsimikizika kuti Iye sadzasintha:

“Mmodzi wa ana ako

ndidzamuyika pa mpando waufumu;

12ngati ana ako azisunga pangano langa

ndi malamulo amene ndiwaphunzitsa,

pamenepo ana awo adzakhala pa mpando

wako waufumu kwamuyaya ndi muyaya.”

13Pakuti Yehova wasankha Ziyoni,

Iye wakhumba kuti akhale malo ake okhalamo:

14“Awa ndi malo anga opumapo ku nthawi za nthawi;

ndidzakhala pano pa mpando waufumu, pakuti ndakhumba zimenezi.

15Ndidzadalitsa mzindawu ndi zinthu zambiri;

anthu ake osauka ndidzawakhutitsa ndi chakudya.

16Ndidzaveka ansembe ake chipulumutso,

ndipo anthu ake oyera mtima adzayimba nthawi zonse nyimbo zachimwemwe.

17“Pano ndidzachulukitsa mphamvu za Davide

ndi kuyikapo nyale ya wodzozedwa wanga.

18Ndidzaveka adani ake manyazi,

koma chipewa chaufumu pamutu pake chidzakhala chowala.”

New International Version

Psalms 132:1-18

Psalm 132

A song of ascents.

1Lord, remember David

and all his self-denial.

2He swore an oath to the Lord,

he made a vow to the Mighty One of Jacob:

3“I will not enter my house

or go to my bed,

4I will allow no sleep to my eyes

or slumber to my eyelids,

5till I find a place for the Lord,

a dwelling for the Mighty One of Jacob.”

6We heard it in Ephrathah,

we came upon it in the fields of Jaar:132:6 Or heard of it in Ephrathah, / we found it in the fields of Jearim. (See 1 Chron. 13:5,6) (And no quotation marks around verses 7-9)

7“Let us go to his dwelling place,

let us worship at his footstool, saying,

8‘Arise, Lord, and come to your resting place,

you and the ark of your might.

9May your priests be clothed with your righteousness;

may your faithful people sing for joy.’ ”

10For the sake of your servant David,

do not reject your anointed one.

11The Lord swore an oath to David,

a sure oath he will not revoke:

“One of your own descendants

I will place on your throne.

12If your sons keep my covenant

and the statutes I teach them,

then their sons will sit

on your throne for ever and ever.”

13For the Lord has chosen Zion,

he has desired it for his dwelling, saying,

14“This is my resting place for ever and ever;

here I will sit enthroned, for I have desired it.

15I will bless her with abundant provisions;

her poor I will satisfy with food.

16I will clothe her priests with salvation,

and her faithful people will ever sing for joy.

17“Here I will make a horn132:17 Horn here symbolizes strong one, that is, king. grow for David

and set up a lamp for my anointed one.

18I will clothe his enemies with shame,

but his head will be adorned with a radiant crown.”