Masalimo 131 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 131:1-3

Salimo 131

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Davide.

1Inu Yehova, mtima wanga siwodzikuza,

maso anga siwonyada;

sinditengeteka mtima

ndi zinthu zapamwamba ndi zodabwitsa.

2Koma moyo wanga ndawutontholetsa

ndi kuwukhalitsa chete ngati mwana amene amayi ake amuletsa kuyamwa,

moyo wanga mʼkati mwanga uli ngati mwana amene amuletsa kuyamwa.

3Yembekeza Yehova, iwe Israeli,

kuyambira tsopano mpaka muyaya.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Salmo 131:1-3

Salmo 131

Cántico de los peregrinos. De David.

1Señor, mi corazón no es orgulloso,

ni son altivos mis ojos;

no busco grandezas desmedidas,

ni proezas que excedan a mis fuerzas.

2Todo lo contrario:

he calmado y aquietado mis ansias.

Soy como un niño recién amamantado en el regazo de su madre.

¡Mi alma es como un niño recién amamantado!

3Israel, pon tu esperanza en el Señor

desde ahora y para siempre.