Masalimo 13 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 13:1-6

Salimo 13

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Mpaka liti Yehova? Kodi mudzandiyiwala mpaka kalekale?

Mpaka liti mudzandibisira nkhope yanu?

2Ndidzalimbana ndi maganizo anga

ndi kukhala ndi chisoni mu mtima mwanga tsiku lililonse mpaka liti?

Mpaka liti adani anga adzandipambana?

3Ndiyangʼaneni ndi kundiyankha, Inu Yehova Mulungu wanga.

Walitsani maso anga kuti ndingafe;

4mdani wanga adzati, “Ndamugonjetsa,”

ndipo adani anga adzakondwera pamene ine ndagwa.

5Koma ndikudalira chikondi chanu chosasinthika;

mtima wanga umakondwera ndi chipulumutso chanu.

6Ine ndidzayimbira Yehova

pakuti wandichitira zokoma.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Salmo 13:1-6

Salmo 13

Al director musical. Salmo de David.

1¿Hasta cuándo, Señor, me seguirás olvidando?

¿Hasta cuándo me esconderás tu rostro?

2¿Hasta cuándo he de estar angustiado

y he de sufrir cada día en mi corazón?

¿Hasta cuándo el enemigo me seguirá dominando?

3Señor y Dios mío,

mírame y respóndeme;

ilumina mis ojos.

Así no caeré en el sueño de la muerte;

4así no dirá mi enemigo: «Lo he vencido»;

así mi adversario no se alegrará de mi caída.

5Pero yo confío en tu gran amor;

mi corazón se alegra en tu salvación.

6Canto salmos al Señor.

¡El Señor ha sido bueno conmigo!