Masalimo 129 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 129:1-8

Salimo 129

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1“Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,”

anene tsono Israeli;

2“Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,

koma sanandipambane.

3Anthu otipula analima pa msana panga

ndipo anapangapo mizere yayitali:

4Koma Yehova ndi wolungama;

Iye wandimasula ku zingwe za anthu oyipa.”

5Onse amene amadana ndi Ziyoni

abwezedwe pambuyo mwamanyazi.

6Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba,

umene umafota usanakule;

7sungadzaze manja a owumweta

kapena manja a omanga mitolo.

8Odutsa pafupi asanene kuti,

“Dalitso la Yehova lili pa inu;

tikukudalitsani mʼdzina la Yehova.”