Masalimo 128 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 128:1-6

Salimo 128

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Odala ndi onse amene amaopa Yehova,

amene amayenda mʼnjira zake.

2Udzadya chipatso cha ntchito yako;

madalitso ndi chuma zidzakhala zako.

3Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka

mʼkati mwa nyumba yako;

ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi

kuzungulira tebulo lako.

4Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa

amene amaopa Yehova.

5Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni

masiku onse a moyo wako;

uwone zokoma za Yerusalemu,

6ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako.

Mtendere ukhale ndi Israeli.

New International Version

Psalms 128:1-6

Psalm 128

A song of ascents.

1Blessed are all who fear the Lord,

who walk in obedience to him.

2You will eat the fruit of your labor;

blessings and prosperity will be yours.

3Your wife will be like a fruitful vine

within your house;

your children will be like olive shoots

around your table.

4Yes, this will be the blessing

for the man who fears the Lord.

5May the Lord bless you from Zion;

may you see the prosperity of Jerusalem

all the days of your life.

6May you live to see your children’s children—

peace be on Israel.