Masalimo 126 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 126:1-6

Salimo 126

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni,

tinali ngati amene akulota.

2Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka;

malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe.

Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti,

“Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”

3Yehova watichitira zinthu zazikulu,

ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.

4Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova,

monga mitsinje ya ku Negevi.

5Iwo amene amafesa akulira,

adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.

6Iye amene amayendayenda nalira,

atanyamula mbewu yokafesa,

adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe,

atanyamula mitolo yake.

Nueva Versión Internacional

Salmo 126:1-6

Salmo 126

Cántico de los peregrinos.

1Cuando el Señor hizo volver a Sión a los cautivos,

nos parecía estar soñando.

2Entonces nuestra boca se llenó de risas;

nuestra lengua, de canciones jubilosas.

Hasta los otros pueblos decían:

«El Señor ha hecho grandes cosas por ellos».

3Sí, el Señor ha hecho grandes cosas por nosotros

y eso nos llena de alegría.

4Ahora, Señor, haz volver a nuestros cautivos

como haces volver los canales de los ríos en el Néguev.

5Los que con lágrimas siembran,

con regocijo cosechan.

6El que llorando esparce la semilla,

cantando recoge sus gavillas.