Masalimo 126 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 126:1-6

Salimo 126

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni,

tinali ngati amene akulota.

2Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka;

malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe.

Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti,

“Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”

3Yehova watichitira zinthu zazikulu,

ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.

4Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova,

monga mitsinje ya ku Negevi.

5Iwo amene amafesa akulira,

adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.

6Iye amene amayendayenda nalira,

atanyamula mbewu yokafesa,

adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe,

atanyamula mitolo yake.

Het Boek

Psalmen 126:1-6

1Een bedevaartslied.

Als de Here de ballingen laat terugkomen in Jeruzalem,

zal het net zijn of wij dromen.

2Dan breken wij uit in gejuich

en iedereen lacht van blijdschap.

Dan zullen zelfs de ongelovige volken rondom ons zeggen

dat de Here wonderen bij ons doet.

3De Here heeft inderdaad grote wonderen onder ons gedaan.

Wat waren wij blij!

4Here, wilt U een ommekeer geven in onze situatie?

5Wie met verdriet in het hart huilend hun akkers inzaaien,

ervaren tegen de oogsttijd vaak grote vreugde.

6Ook al huilt iemand terwijl hij op pad is om te zaaien,

zeker is dat hij blij lachend de rijke schoven zal wegdragen.