Masalimo 125 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 125:1-5

Salimo 125

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Amene amadalira Yehova ali ngati phiri la Ziyoni,

limene silingagwedezeke koma ndi lokhala mpaka muyaya.

2Monga mapiri azungulira Yerusalemu,

momwemonso Yehova azungulira anthu ake

kuyambira tsopano mpaka muyaya.

3Ndodo yaufumu ya anthu oyipa sidzakhala

pa dziko limene lapatsidwa kwa anthu olungama,

kuti anthu olungamawo

angachite nawonso zoyipa.

4Yehova chitirani zabwino amene ndi abwino,

amene ndi olungama mtima

5Koma amene amatembenukira ku njira zokhotakhota,

Yehova adzawachotsa pamodzi ndi anthu ochita zoyipa.

Mtendere ukhale pa Israeli.

New Serbian Translation

Псалми 125:1-5

Псалам 125

Песма поклоничка.

1Они што се у Господа уздају,

јесу као гора Сион – постојана,

довека се помакнути не да!

2Попут гора што Јерусалим окружују,

тако је и Господ око свог народа,

све од сада па за вечност целу.

3Уистину, неће жезло злочинаца владати

над земљом што припада праведнима;

да праведни руке своје не би

неправди пружали.

4О, Господе, добро чини добрима

и онима честитога срца!

5А оне што на своје криве стазе скрећу,

Господ ће одагнати са злотворима.

Мир Израиљу!