Masalimo 125 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 125:1-5

Salimo 125

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Amene amadalira Yehova ali ngati phiri la Ziyoni,

limene silingagwedezeke koma ndi lokhala mpaka muyaya.

2Monga mapiri azungulira Yerusalemu,

momwemonso Yehova azungulira anthu ake

kuyambira tsopano mpaka muyaya.

3Ndodo yaufumu ya anthu oyipa sidzakhala

pa dziko limene lapatsidwa kwa anthu olungama,

kuti anthu olungamawo

angachite nawonso zoyipa.

4Yehova chitirani zabwino amene ndi abwino,

amene ndi olungama mtima

5Koma amene amatembenukira ku njira zokhotakhota,

Yehova adzawachotsa pamodzi ndi anthu ochita zoyipa.

Mtendere ukhale pa Israeli.

New International Version

Psalms 125:1-5

Psalm 125

A song of ascents.

1Those who trust in the Lord are like Mount Zion,

which cannot be shaken but endures forever.

2As the mountains surround Jerusalem,

so the Lord surrounds his people

both now and forevermore.

3The scepter of the wicked will not remain

over the land allotted to the righteous,

for then the righteous might use

their hands to do evil.

4Lord, do good to those who are good,

to those who are upright in heart.

5But those who turn to crooked ways

the Lord will banish with the evildoers.

Peace be on Israel.