Masalimo 123 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 123:1-4

Salimo 123

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Ndikweza maso anga kwa Inu,

kwa Inu amene mumakhala kumwamba.

2Taonani, monga momwe maso a akapolo amayangʼana mʼdzanja la mbuye wawo,

monga momwenso maso a mdzakazi amayangʼana mʼdzanja la dona wake,

choncho maso athu ali kwa Yehova Mulungu wathu,

mpaka atichitire chifundo.

3Mutichitire chifundo, Inu Yehova mutichitire chifundo,

pakuti tapirira chitonzo chachikulu.

4Ife tapirira mnyozo wambiri kuchokera kwa anthu odzikuza,

chitonzo chachikulu kuchokera kwa anthu onyada.