Masalimo 122 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 122:1-9

Salimo 122

Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Ndinakondwera atandiwuza kuti,

“Tiyeni ku nyumba ya Yehova.”

2Mapazi athu akuyima mʼzipata

zako, Iwe Yerusalemu.

3Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda

umene uli wothithikana pamodzi.

4Kumeneko ndiye kumene kumapita mafuko,

mafuko a Yehova,

umboni wa kwa Israeli,

kuti atamande dzina la Yehova.

5Kumeneko anayikako mipando yaufumu yachiweruzo,

mipando yaufumu ya nyumba ya Davide.

6Pemphererani mtendere wa Yerusalemu:

“Iwo amene amakukonda iwe zinthu ziwayendere bwino.

7Mukhale mtendere mʼkati mwa makoma ako,

ndipo mʼnyumba zako zaufumu mukhale chitetezo.”

8Chifukwa cha abale anga ndi abwenzi anga

ndidzati, “Mtendere ukhale mʼkati mwako.”

9Chifukwa cha Nyumba ya Yehova Mulungu wathu,

ndidzakufunira zabwino.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 122:1-9

第 122 篇

為耶路撒冷禱告

大衛上聖殿朝聖之詩。

1人們對我說:

「讓我們去耶和華的殿吧!」

我感到歡喜。

2耶路撒冷啊,

我們踏進你的城門了。

3耶路撒冷是一座整齊堅固的城。

4以色列各支派,耶和華的子民,

都遵照祂賜的法度去那裡稱謝祂。

5那裡有審判的王座,

就是大衛家的王座。

6要為耶路撒冷的和平禱告,

願愛這城的人亨通。

7耶路撒冷啊!

願你城內有平安,

你的宮裡有安寧,

8為了我的親人和朋友,

我要祈求平安臨到你。

9為了我們的上帝耶和華的殿,

我要為你求福祉。