Masalimo 122 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 122:1-9

Salimo 122

Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Ndinakondwera atandiwuza kuti,

“Tiyeni ku nyumba ya Yehova.”

2Mapazi athu akuyima mʼzipata

zako, Iwe Yerusalemu.

3Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda

umene uli wothithikana pamodzi.

4Kumeneko ndiye kumene kumapita mafuko,

mafuko a Yehova,

umboni wa kwa Israeli,

kuti atamande dzina la Yehova.

5Kumeneko anayikako mipando yaufumu yachiweruzo,

mipando yaufumu ya nyumba ya Davide.

6Pemphererani mtendere wa Yerusalemu:

“Iwo amene amakukonda iwe zinthu ziwayendere bwino.

7Mukhale mtendere mʼkati mwa makoma ako,

ndipo mʼnyumba zako zaufumu mukhale chitetezo.”

8Chifukwa cha abale anga ndi abwenzi anga

ndidzati, “Mtendere ukhale mʼkati mwako.”

9Chifukwa cha Nyumba ya Yehova Mulungu wathu,

ndidzakufunira zabwino.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Забур 122:1-4

Песнь 122

Песнь восхождения.

1К Тебе поднимаю глаза свои,

Обитающий на небесах!

2Как глаза слуг смотрят на руку своего господина

и глаза служанки – на руку своей госпожи,

так наши глаза обращены на Вечного,

до тех пор, пока Он не смилуется над нами.

3Помилуй нас, Вечный, помилуй нас,

потому что мы долго терпели презрение.

4Долго мы терпели оскорбление от надменных

и презрение от гордых.