Masalimo 122 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 122:1-9

Salimo 122

Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Ndinakondwera atandiwuza kuti,

“Tiyeni ku nyumba ya Yehova.”

2Mapazi athu akuyima mʼzipata

zako, Iwe Yerusalemu.

3Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda

umene uli wothithikana pamodzi.

4Kumeneko ndiye kumene kumapita mafuko,

mafuko a Yehova,

umboni wa kwa Israeli,

kuti atamande dzina la Yehova.

5Kumeneko anayikako mipando yaufumu yachiweruzo,

mipando yaufumu ya nyumba ya Davide.

6Pemphererani mtendere wa Yerusalemu:

“Iwo amene amakukonda iwe zinthu ziwayendere bwino.

7Mukhale mtendere mʼkati mwa makoma ako,

ndipo mʼnyumba zako zaufumu mukhale chitetezo.”

8Chifukwa cha abale anga ndi abwenzi anga

ndidzati, “Mtendere ukhale mʼkati mwako.”

9Chifukwa cha Nyumba ya Yehova Mulungu wathu,

ndidzakufunira zabwino.

Bibelen på hverdagsdansk

Salmernes Bog 122:1-9

Lovprisning af og bøn for Jerusalem

1En valfartssang af David.

Jeg blev så glad, da jeg hørte,

at vi skulle drage til Herrens hus.

2Nu står vi så endelig her,

i porten ind til Jerusalem.

3Jerusalem er en fantastisk by,

tæt pakket med huse og mennesker.122,3 Teksten er uklar.

4Her mødes Israels stammer, Herrens eget folk,

for at takke Herren ifølge Toraens forskrifter.

5Her står Davids trone,

herfra regerer hans kongeslægt.

6Bed om fred i Jerusalem.

Må det gå godt for dem, der elsker byen.

7Må der være fred inden for murene

og tryghed i tårnene.

8For slægt og venners skyld

ønsker jeg fred over Jerusalem.

9For Herrens helligdoms skyld

beder jeg om tryghed for byen.