Masalimo 120 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 120:1-7

Salimo 120

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga,

ndipo Iye amandiyankha.

2Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza,

ndi kwa anthu achinyengo.

3Kodi adzakuchitani chiyani,

ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?

4Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo,

ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.

5Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki,

kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!

6Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati

pa iwo amene amadana ndi mtendere.

7Ine ndine munthu wamtendere;

koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.

New Russian Translation

Псалтирь 120:1-8

Псалом 120

1Песнь восхождения.

Обращаю взгляд свой к горам,

откуда придет мне помощь?

2Помощь мне придет от Господа,

сотворившего небо и землю.

3Он не позволит ноге твоей пошатнуться,

хранящий тебя не задремлет;

4истинно, хранящий Израиль

не задремлет и не уснет.

5Господь – страж твой;

Господь – тень твоя по правую руку твою.

6Солнце не поразит тебя днем,

ни луна – ночью.

7Господь сохранит тебя от всякого зла;

Он сохранит твою душу.

8Господь будет хранить тебя,

когда ты будешь уходить и когда будешь приходить,

отныне и вовеки.