Salimo 12
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe seminiti. Salimo la Davide.
1Thandizeni Yehova pakuti palibe munthu wokhulupirika;
okhulupirika akusowa pakati pa anthu.
2Aliyense amanamiza mʼbale wake;
ndi pakamwa pawo pabodza amayankhula zachinyengo.
3Inu Yehova tsekani milomo yonse yachinyengo
ndi pakamwa paliponse podzikuza.
4Pakamwa pamene pamati, “Ife tidzapambana ndi kuyankhula kwathu;
pakamwapa ndi pathupathu, tsono mbuye wathu ndani?”
5“Chifukwa cha kuponderezedwa kwa anthu opanda mphamvu
ndi kubuwula kwa anthu osowa,
Ine ndidzauka tsopano,” akutero Yehova,
“Ndidzawateteza kwa owazunza.”
6Ndipo mawu a Yehova ndi angwiro
monga siliva oyengedwa mʼngʼanjo yadothi,
oyengedwa kasanu nʼkawiri.
7Inu Yehova mudzatitchinjiriza ndipo
mudzatiteteza kwa anthu otere kwamuyaya.
8Oyipa amangoyendayenda ponseponse
anthu akamayamikira zochita zawo.
Псалом 12
1Дирижеру хора. Псалом Давида.
2Как долго, Господи? Неужели забыл Ты меня навеки?
Как долго Ты будешь скрывать от меня Свое лицо?
3Как долго мне муку в душе носить12:3 Так в одном из древних переводов; в нормативном еврейском тексте: «хранить советы в моей душе».
и целыми днями крушить болью сердце?
Как долго моему врагу надо мной кичиться?
4Посмотри на меня и ответь, Господи, Боже мой.
Глаза мои просветли,
чтобы мне не уснуть смертным сном,
5чтобы враг не сказал: «Я его превозмог» –
и когда я паду, не радовались бы недруги мои.
6Я уповаю на Твою милость,
мое сердце возрадуется спасению Твоему.
Господу буду петь,
потому что Он ко мне благ.