Masalimo 12 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 12:1-8

Salimo 12

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe seminiti. Salimo la Davide.

1Thandizeni Yehova pakuti palibe munthu wokhulupirika;

okhulupirika akusowa pakati pa anthu.

2Aliyense amanamiza mʼbale wake;

ndi pakamwa pawo pabodza amayankhula zachinyengo.

3Inu Yehova tsekani milomo yonse yachinyengo

ndi pakamwa paliponse podzikuza.

4Pakamwa pamene pamati, “Ife tidzapambana ndi kuyankhula kwathu;

pakamwapa ndi pathupathu, tsono mbuye wathu ndani?”

5“Chifukwa cha kuponderezedwa kwa anthu opanda mphamvu

ndi kubuwula kwa anthu osowa,

Ine ndidzauka tsopano,” akutero Yehova,

“Ndidzawateteza kwa owazunza.”

6Ndipo mawu a Yehova ndi angwiro

monga siliva oyengedwa mʼngʼanjo yadothi,

oyengedwa kasanu nʼkawiri.

7Inu Yehova mudzatitchinjiriza ndipo

mudzatiteteza kwa anthu otere kwamuyaya.

8Oyipa amangoyendayenda ponseponse

anthu akamayamikira zochita zawo.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 12:1-8

第 12 篇

祈求上帝幫助

大衛的詩,交給樂長。

1耶和華啊,求你救我們!

因為世上的敬虔人不見了,

忠信的人在人間消失了。

2人人謊話連篇,

花言巧語,口是心非。

3願你剷除一切花言巧語和狂妄自誇的人。

4他們說:「我們必靠舌頭制勝,

嘴唇是我們自己的,

誰管得著我們?」

5耶和華說:「我要保護受欺壓的困苦人和哀歎的貧窮人,

使他們如願以償。」

6耶和華的應許純全,

就像在爐中煉過七次的銀子。

7耶和華啊,你必保護我們,

永遠不容惡人侵害我們。

8眾人若抑善揚惡,

惡人必橫行無忌。