Salimo 119
Alefu
1Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa,
amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
2Odala ndi amene amasunga malamulo ake,
amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
3Sachita cholakwa chilichonse;
amayenda mʼnjira zake.
4Inu mwapereka malangizo
ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
5Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika
pa kumvera zophunzitsa zanu!
6Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi,
poganizira malamulo anu onse.
7Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama,
pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
8Ndidzamvera zophunzitsa zanu;
musanditaye kwathunthu.
Beti
9Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake?
Akawasamala potsata mawu anu.
10Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse;
musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
11Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga
kuti ndisakuchimwireni.
12Mutamandike Inu Yehova;
phunzitseni malamulo anu.
13Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse
amene amachokera pakamwa panu.
14Ndimakondwera potsatira malamulo anu
monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
15Ndimalingalira malangizo anu
ndipo ndimaganizira njira zanu.
16Ndimakondwera ndi malamulo anu;
sindidzayiwala konse mawu anu.
Gimeli
17Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo;
kuti tsono ndisunge mawu anu.
18Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona
zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
19Ine ndine mlendo pa dziko lapansi;
musandibisire malamulo anu.
20Moyo wanga wafowoka polakalaka
malamulo anu nthawi zonse.
21Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa,
amene achoka pa malamulo anu.
22Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo
pakuti ndimasunga malamulo anu.
23Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza,
mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
24Malamulo anu amandikondweretsa;
ndiwo amene amandilangiza.
Daleti
25Moyo wanga wakangamira fumbi;
tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
26Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha;
phunzitseni malamulo anu.
27Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu;
pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
28Moyo wanga wafowoka ndi chisoni;
limbikitseni monga mwa mawu anu.
29Mundichotse mʼnjira zachinyengo;
mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
30Ndasankha njira ya choonadi;
ndayika malamulo anu pa mtima panga.
31Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova;
musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
32Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu,
pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
He
33Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu;
ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
34Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu
ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
35Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu,
pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
36Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu,
osati chuma.
37Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe;
sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
38Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu,
kuti Inu muopedwe.
39Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa,
pakuti malamulo anu ndi abwino.
40Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu!
Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
Wawi
41Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova,
chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
42ndipo ndidzayankha amene amandinyoza,
popeza ndimadalira mawu anu.
43Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga,
pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
44Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse,
ku nthawi za nthawi.
45Ndidzayendayenda mwaufulu,
chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
46Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu
ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
47popeza ndimakondwera ndi malamulo anu
chifukwa ndimawakonda.
48Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda,
ndipo ndimalingalira malangizo anu.
Zayini
49Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu,
popeza mwandipatsa chiyembekezo.
50Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi:
lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
51Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa,
koma sindichoka pa malamulo anu.
52Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale,
ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
53Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa
amene ataya malamulo anu.
54Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga
kulikonse kumene ndigonako.
55Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova,
ndipo ndidzasunga malamulo anu.
56Ichi ndicho ndakhala ndikuchita:
ndimasunga malangizo anu.
Heti
57Yehova, Inu ndiye gawo langa;
ndalonjeza kumvera mawu anu.
58Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse;
mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
59Ndinalingalira za njira zanga
ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
60Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza
kumvera malamulo anu.
61Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe,
sindidzayiwala lamulo lanu.
62Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu
chifukwa cha malamulo anu olungama.
63Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani,
kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
64Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika,
phunzitseni malamulo anu.
Teti
65Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu
molingana ndi mawu anu.
66Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino,
pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
67Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera,
koma tsopano ndimamvera mawu anu.
68Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino;
phunzitseni malamulo anu.
69Ngakhale odzikuza andipaka mabodza,
ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
70Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa,
koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
71Ndi bwino kuti ndinasautsidwa
kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
72Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri
kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
Yodi
73Manja anu anandilenga ndi kundiwumba;
patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
74Iwo amene amakuopani akondwere akandiona,
chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
75Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama
ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
76Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa,
molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
77Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo,
popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
78Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa;
koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
79Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine,
iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
80Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu
kuti ndisachititsidwe manyazi.
Kafu
81Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu,
koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
82Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu;
Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
83Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi
sindiyiwala zophunzitsa zanu.
84Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti?
Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
85Anthu osalabadira za Mulungu,
odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
86Malamulo anu onse ndi odalirika;
thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
87Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi
koma sindinataye malangizo anu.
88Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika,
ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Lamedi
89Mawu anu Yehova ndi amuyaya;
akhazikika kumwambako.
90Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse;
Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
91Malamulo anu alipobe mpaka lero lino,
pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
92Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa,
ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
93Ine sindidzayiwala konse malangizo anu,
pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
94Ndine wanu, ndipulumutseni;
pakuti ndasamala malangizo anu.
95Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge,
koma ndidzalingalira umboni wanu.
96Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire,
koma malamulo anu alibe malire konse.
Memu
97Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu!
Ndimalingaliramo tsiku lonse.
98Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga,
popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
99Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse
popeza ndimalingalira umboni wanu.
100Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba,
popeza ndimamvera malangizo anu.
101Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa
kuti ndithe kumvera mawu anu.
102Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu,
pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
103Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa,
otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
104Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu;
kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Nuni
105Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga
ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
106Ndalumbira ndipo ndatsimikiza,
kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
107Ndazunzika kwambiri;
Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
108Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga,
ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
109Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi,
sindidzayiwala malamulo anu.
110Anthu oyipa anditchera msampha,
koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
111Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya;
Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
112Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu
mpaka kumapeto kwenikweni.
Samekhi
113Ndimadana ndi anthu apawiripawiri,
koma ndimakonda malamulo anu.
114Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa;
chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
115Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa,
kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
116Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo;
musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
117Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa;
nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
118Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu,
pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
119Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala;
nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
120Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu;
ndimachita mantha ndi malamulo anu.
Ayini
121Ndachita zolungama ndi zabwino;
musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
122Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino,
musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
123Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu,
kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
124Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika,
ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
125Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa,
kuti ndimvetsetse umboni wanu.
126Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu;
malamulo anu akuswedwa.
127Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu
kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
128ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka,
ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Pe
129Maumboni anu ndi odabwitsa
nʼchifukwa chake ndimawamvera.
130Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika;
ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
131Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu,
kufunafuna malamulo anu.
132Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo,
monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
133Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu;
musalole kuti tchimo lizindilamulira.
134Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza,
kuti ndithe kumvera malangizo anu.
135Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu
ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
136Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga,
chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Tsade
137Yehova ndinu wolungama,
ndipo malamulo anu ndi abwino.
138Maumboni amene munatipatsa ndi olungama;
ndi odalirika ndithu.
139Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga
chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
140Mawu anu ndi woyera kwambiri
nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
141Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka,
sindiyiwala malangizo anu.
142Chilungamo chanu nʼchamuyaya,
ndipo malamulo anu nʼchoona.
143Mavuto ndi masautso zandigwera,
koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
144Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse;
patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
Kofu
145Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova,
ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
146Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni
ndipo ndidzasunga umboni wanu.
147Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo;
chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
148Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku,
kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
149Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika;
Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
150Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira,
koma ali kutali ndi malamulo anu.
151Koma Inu Yehova muli pafupi,
malamulo anu onse ndi woona.
152Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu
kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
Reshi
153Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse,
pakuti sindinayiwale malamulo anu.
154Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola;
sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
155Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa,
pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
156Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu;
sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
157Adani amene akundizunza ndi ambiri,
koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
158Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro,
popeza samvera mawu anu.
159Onani momwe ndimakondera malangizo anu;
sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
160Mawu anu onse ndi owona;
malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
Sini ndi Shini
161Olamulira amandizunza popanda chifukwa,
koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
162Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu,
ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
163Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho,
koma ndimakonda malamulo anu.
164Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku
pakuti malamulo anu ndi olungama.
165Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu,
ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
166Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova,
ndipo ndimatsatira malamulo anu.
167Ndimamvera umboni wanu
pakuti ndimawukonda kwambiri.
168Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu,
pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
Tawu
169Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova;
patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
170Kupempha kwanga kufike pamaso panu;
pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
171Matamando asefukire pa milomo yanga,
pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
172Lilime langa liyimbe mawu anu,
popeza malamulo anu onse ndi olungama.
173Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza
pakuti ndasankha malangizo anu.
174Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova,
ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
175Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni,
ndipo malamulo anu andichirikize.
176Ndasochera ngati nkhosa yotayika,
funafunani mtumiki wanu,
pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Salmo 119119 O salmo 119 é um poema organizado em ordem alfabética, no hebraico.
Álef
1Como são felizes os que andam em caminhos irrepreensíveis,
que vivem conforme a lei do Senhor!
2Como são felizes os que obedecem aos seus estatutos
e de todo o coração o buscam!
3Não praticam o mal
e andam nos caminhos do Senhor.
4Tu mesmo ordenaste os teus preceitos
para que sejam fielmente obedecidos.
5Quem dera fossem firmados os meus caminhos
na obediência aos teus decretos.
6Então não ficaria decepcionado
ao considerar todos os teus mandamentos.
7Eu te louvarei de coração sincero
quando aprender as tuas justas ordenanças.
8Obedecerei aos teus decretos;
nunca me abandones.
Bêt
9Como pode o jovem manter pura a sua conduta?
Vivendo de acordo com a tua palavra.
10Eu te busco de todo o coração;
não permitas que eu me desvie dos teus mandamentos.
11Guardei no coração a tua palavra
para não pecar contra ti.
12Bendito sejas, Senhor!
Ensina-me os teus decretos.
13Com os lábios repito
todas as leis que promulgaste.
14Regozijo-me em seguir os teus testemunhos
como o que se regozija com grandes riquezas.
15Meditarei nos teus preceitos
e darei atenção às tuas veredas.
16Tenho prazer nos teus decretos;
não me esqueço da tua palavra.
Guímel
17Trata com bondade o teu servo
para que eu viva e obedeça à tua palavra.
18Abre os meus olhos
para que eu veja as maravilhas da tua lei.
19Sou peregrino na terra;
não escondas de mim os teus mandamentos.
20A minha alma consome-se
de perene desejo das tuas ordenanças.
21Tu repreendes os arrogantes;
malditos os que se desviam dos teus mandamentos!
22Tira de mim a afronta e o desprezo,
pois obedeço aos teus estatutos.
23Mesmo que os poderosos se reúnam para conspirar contra mim,
ainda assim o teu servo meditará nos teus decretos.
24Sim, os teus testemunhos são o meu prazer;
eles são os meus conselheiros.
Dálet
25Agora estou prostrado no pó;
preserva a minha vida conforme a tua promessa.
26A ti relatei os meus caminhos e tu me respondeste;
ensina-me os teus decretos.
27Faze-me discernir o propósito dos teus preceitos;
então meditarei nas tuas maravilhas.
28A minha alma se consome de tristeza;
fortalece-me conforme a tua promessa.
29Desvia-me dos caminhos enganosos;
por tua graça, ensina-me a tua lei.
30Escolhi o caminho da fidelidade;
decidi seguir as tuas ordenanças.
31Apego-me aos teus testemunhos, ó Senhor;
não permitas que eu fique decepcionado.
32Corro pelo caminho que os teus mandamentos apontam,
pois me deste maior entendimento.
He
33Ensina-me, Senhor, o caminho dos teus decretos,
e a eles obedecerei até o fim.
34Dá-me entendimento, para que eu guarde a tua lei
e a ela obedeça de todo o coração.
35Dirige-me pelo caminho dos teus mandamentos,
pois nele encontro satisfação.
36Inclina o meu coração para os teus estatutos,
e não para a ganância.
37Desvia os meus olhos das coisas inúteis;
faze-me viver nos caminhos que traçaste.119.37 Dois manuscritos do Texto Massorético e os manuscritos do mar Morto dizem preserva a minha vida pela tua palavra.
38Cumpre a tua promessa para com o teu servo,
para que sejas temido.
39Livra-me da afronta que me apavora,
pois as tuas ordenanças são boas.
40Como anseio pelos teus preceitos!
Preserva a minha vida por tua justiça!
Vav
41Que o teu amor alcance-me, Senhor,
e a tua salvação, segundo a tua promessa;
42então responderei aos que me afrontam,
pois confio na tua palavra.
43Jamais tires da minha boca a palavra da verdade,
pois nas tuas ordenanças depositei a minha esperança.
44Obedecerei constantemente à tua lei,
para todo o sempre.
45Andarei em verdadeira liberdade,
pois tenho buscado os teus preceitos.
46Falarei dos teus testemunhos diante de reis,
sem ficar envergonhado.
47Tenho prazer nos teus mandamentos;
eu os amo.
48A ti119.48 Ou Aos teus mandamentos levanto minhas mãos
e medito nos teus decretos.
Zain
49Lembra-te da tua palavra ao teu servo,
pela qual me deste esperança.
50Este é o meu consolo no meu sofrimento:
A tua promessa dá-me vida.
51Os arrogantes zombam de mim o tempo todo,
mas eu não me desvio da tua lei.
52Lembro-me, Senhor, das tuas ordenanças do passado
e nelas acho consolo.
53Fui tomado de ira tremenda por causa dos ímpios
que rejeitaram a tua lei.
54Os teus decretos são o tema
da minha canção em minha peregrinação.
55De noite lembro-me do teu nome, Senhor!
Vou obedecer à tua lei.
56Esta tem sido a minha prática:
Obedecer aos teus preceitos.
Hêt
57Tu és a minha herança, Senhor;
prometi obedecer às tuas palavras.
58De todo o coração suplico a tua graça;
tem misericórdia de mim, conforme a tua promessa.
59Refleti em meus caminhos e voltei os meus passos
para os teus testemunhos.
60Eu me apressarei e não hesitarei
em obedecer aos teus mandamentos.
61Embora as cordas dos ímpios queiram prender-me,
eu não me esqueço da tua lei.
62À meia-noite me levanto para dar-te graças
pelas tuas justas ordenanças.
63Sou amigo de todos os que te temem
e obedecem aos teus preceitos.
64A terra está cheia do teu amor, Senhor;
ensina-me os teus decretos.
Tét
65Trata com bondade o teu servo, Senhor,
conforme a tua promessa.
66Ensina-me o bom senso e o conhecimento,
pois confio em teus mandamentos.
67Antes de ser castigado, eu andava desviado,
mas agora obedeço à tua palavra.
68Tu és bom, e o que fazes é bom;
ensina-me os teus decretos.
69Os arrogantes mancharam o meu nome com mentiras,
mas eu obedeço aos teus preceitos de todo o coração.
70O coração deles é insensível;
eu, porém, tenho prazer na tua lei.
71Foi bom para mim ter sido castigado,
para que aprendesse os teus decretos.
72Para mim vale mais a lei que decretaste
do que milhares de peças de prata e ouro.
Iode
73As tuas mãos me fizeram e me formaram;
dá-me entendimento para aprender os teus mandamentos.
74Quando os que têm temor de ti me virem, se alegrarão,
pois na tua palavra depositei a minha esperança.
75Sei, Senhor, que as tuas ordenanças são justas,
e que por tua fidelidade me castigaste.
76Seja o teu amor o meu consolo,
conforme a tua promessa ao teu servo.
77Alcance-me a tua misericórdia para que eu tenha vida,
porque a tua lei é o meu prazer.
78Sejam humilhados os arrogantes, pois me prejudicaram sem motivo;
mas eu meditarei nos teus preceitos.
79Venham apoiar-me aqueles que te temem,
aqueles que entendem os teus estatutos.
80Seja o meu coração íntegro para com os teus decretos,
para que eu não seja humilhado.
Caf
81Estou quase desfalecido, aguardando a tua salvação,
mas na tua palavra depositei a minha esperança.
82Os meus olhos fraquejam de tanto esperar pela tua promessa,
e pergunto: “Quando me consolarás?”
83Embora eu seja como uma vasilha inútil119.83 Hebraico: um odre na fumaça.,
não me esqueço dos teus decretos.
84Até quando o teu servo deverá esperar
para que castigues os meus perseguidores?
85Cavaram uma armadilha contra mim os arrogantes,
os que não seguem a tua lei.
86Todos os teus mandamentos merecem confiança;
ajuda-me, pois sou perseguido com mentiras.
87Quase acabaram com a minha vida na terra,
mas não abandonei os teus preceitos.
88Preserva a minha vida pelo teu amor,
e obedecerei aos estatutos que decretaste.
Lâmed
89A tua palavra, Senhor,
para sempre está firmada nos céus.
90A tua fidelidade é constante por todas as gerações;
estabeleceste a terra, que firme subsiste.
91Conforme as tuas ordens, tudo permanece até hoje119.91 Ou as tuas leis permanecem até hoje,
pois tudo está a teu serviço.
92Se a tua lei não fosse o meu prazer,
o sofrimento já me teria destruído.
93Jamais me esquecerei dos teus preceitos,
pois é por meio deles que preservas a minha vida.
94Salva-me, pois a ti pertenço
e busco os teus preceitos!
95Os ímpios estão à espera para destruir-me,
mas eu considero os teus testemunhos.
96Tenho constatado que toda perfeição tem limite;
mas não há limite para o teu mandamento.
Mem
97Como eu amo a tua lei!
Medito nela o dia inteiro.
98Os teus mandamentos me tornam mais sábio que os meus inimigos,
porquanto estão sempre comigo.
99Tenho mais discernimento que todos os meus mestres,
pois medito nos teus testemunhos.
100Tenho mais entendimento que os anciãos,
pois obedeço aos teus preceitos.
101Afasto os pés de todo caminho mau
para obedecer à tua palavra.
102Não me afasto das tuas ordenanças,
pois tu mesmo me ensinas.
103Como são doces para o meu paladar as tuas palavras!
Mais que o mel para a minha boca!
104Ganho entendimento por meio dos teus preceitos;
por isso odeio todo caminho de falsidade.
Nun
105A tua palavra é lâmpada que ilumina os meus passos
e luz que clareia o meu caminho.
106Prometi sob juramento e o cumprirei:
vou obedecer às tuas justas ordenanças.
107Passei por muito sofrimento;
preserva, Senhor, a minha vida, conforme a tua promessa.
108Aceita, Senhor, a oferta de louvor dos meus lábios,
e ensina-me as tuas ordenanças.
109A minha vida está sempre em perigo119.109 Hebraico: em minhas mãos.,
mas não me esqueço da tua lei.
110Os ímpios prepararam uma armadilha contra mim,
mas não me desviei dos teus preceitos.
111Os teus testemunhos são a minha herança permanente;
são a alegria do meu coração.
112Dispus o meu coração para cumprir
os teus decretos até o fim.
Sâmeq
113Odeio os que são inconstantes,
mas amo a tua lei.
114Tu és o meu abrigo e o meu escudo;
e na tua palavra depositei a minha esperança.
115Afastem-se de mim os que praticam o mal!
Quero obedecer aos mandamentos do meu Deus!
116Sustenta-me, segundo a tua promessa, e eu viverei;
não permitas que se frustrem as minhas esperanças.
117Ampara-me, e estarei seguro;
sempre estarei atento aos teus decretos.
118Tu rejeitas todos os que se desviam dos teus decretos,
pois os seus planos enganosos são inúteis.
119Tu destróis119.119 Alguns manuscritos do Texto Massorético, a Septuaginta e outras versões gregas dizem consideras. como refugo todos os ímpios da terra;
por isso amo os teus testemunhos.
120O meu corpo estremece diante de ti;
as tuas ordenanças enchem-me de temor.
Áin
121Tenho vivido com justiça e retidão;
não me abandones nas mãos dos meus opressores.
122Garante o bem-estar do teu servo;
não permitas que os arrogantes me oprimam.
123Os meus olhos fraquejam, aguardando a tua salvação
e o cumprimento da tua justiça.
124Trata o teu servo conforme o teu amor leal
e ensina-me os teus decretos.
125Sou teu servo; dá-me discernimento
para compreender os teus testemunhos.
126Já é tempo de agires, Senhor,
pois a tua lei está sendo desrespeitada.
127Eu amo os teus mandamentos mais do que o ouro,
mais do que o ouro puro.
128Por isso considero justos os teus preceitos
e odeio todo caminho de falsidade.
Pê
129Os teus testemunhos são maravilhosos;
por isso lhes obedeço.
130A explicação das tuas palavras ilumina
e dá discernimento aos inexperientes.
131Abro a boca e suspiro,
ansiando por teus mandamentos.
132Volta-te para mim e tem misericórdia de mim,
como sempre fazes aos que amam o teu nome.
133Dirige os meus passos, conforme a tua palavra;
não permitas que nenhum pecado me domine.
134Resgata-me da opressão dos homens,
para que eu obedeça aos teus preceitos.
135Faze o teu rosto resplandecer sobre119.135 Isto é, mostra a tua bondade para com. o teu servo
e ensina-me os teus decretos.
136Rios de lágrimas correm dos meus olhos,
porque a tua lei não é obedecida.
Tsade
137Justo és, Senhor,
e retas são as tuas ordenanças.
138Ordenaste os teus testemunhos com justiça;
dignos são de inteira confiança!
139O meu zelo me consome,
pois os meus adversários se esquecem das tuas palavras.
140A tua promessa119.140 Ou palavra foi plenamente comprovada,
e, por isso, o teu servo a ama.
141Sou pequeno e desprezado,
mas não esqueço os teus preceitos.
142A tua justiça é eterna,
e a tua lei é a verdade.
143Tribulação e angústia me atingiram,
mas os teus mandamentos são o meu prazer.
144Os teus testemunhos são eternamente justos,
dá-me discernimento para que eu tenha vida.
Cof
145Eu clamo de todo o coração;
responde-me, Senhor, e obedecerei aos teus testemunhos!
146Clamo a ti; salva-me,
e obedecerei aos teus estatutos!
147Antes do amanhecer me levanto e suplico o teu socorro;
na tua palavra depositei a minha esperança.
148Fico acordado nas vigílias da noite,
para meditar nas tuas promessas.
149Ouve a minha voz pelo teu amor leal;
faze-me viver, Senhor, conforme as tuas ordenanças.
150Os meus perseguidores aproximam-se com más intenções,119.150 Conforme alguns manuscritos do Texto Massorético, a Septuaginta e algumas versões gregas. O Texto Massorético diz Os que tramam o mal estão por perto.
mas estão distantes da tua lei.
151Tu, porém, Senhor, estás perto,
e todos os teus mandamentos são verdadeiros.
152Há muito aprendi dos teus testemunhos
que tu os estabeleceste para sempre.
Rêsh
153Olha para o meu sofrimento e livra-me,
pois não me esqueço da tua lei.
154Defende a minha causa e resgata-me;
preserva a minha vida conforme a tua promessa.
155A salvação está longe dos ímpios,
pois eles não buscam os teus decretos.
156Grande é a tua compaixão, Senhor;
preserva a minha vida conforme as tuas leis.
157Muitos são os meus adversários e os meus perseguidores,
mas eu não me desvio dos teus estatutos.
158Com grande desgosto vejo os infiéis,
que não obedecem à tua palavra.
159Vê como amo os teus preceitos!
Dá-me vida, Senhor, conforme o teu amor leal.
160A verdade é a essência da tua palavra,
e todas as tuas justas ordenanças são eternas.
Shin e Sin
161Os poderosos perseguem-me sem motivo,
mas é diante da tua palavra que o meu coração treme.
162Eu me regozijo na tua promessa como alguém
que encontra grandes despojos.
163Odeio e detesto a falsidade,
mas amo a tua lei.
164Sete vezes por dia eu te louvo
por causa das tuas justas ordenanças.
165Os que amam a tua lei desfrutam paz,
e nada há que os faça tropeçar.
166Aguardo a tua salvação, Senhor,
e pratico os teus mandamentos.
167Obedeço aos teus testemunhos;
amo-os infinitamente!
168Obedeço a todos os teus preceitos e testemunhos,
pois conheces todos os meus caminhos.
Tau
169Chegue à tua presença o meu clamor, Senhor!
Dá-me entendimento conforme a tua palavra.
170Chegue a ti a minha súplica.
Livra-me, conforme a tua promessa.
171Meus lábios transbordarão de louvor,
pois me ensinas os teus decretos.
172A minha língua cantará a tua palavra,
pois todos os teus mandamentos são justos.
173Com tua mão vem ajudar-me,
pois escolhi os teus preceitos.
174Anseio pela tua salvação, Senhor,
e a tua lei é o meu prazer.
175Permite-me viver para que eu te louve;
e que as tuas ordenanças me sustentem.
176Andei vagando como ovelha perdida;
vem em busca do teu servo,
pois não me esqueci dos teus mandamentos.