Salimo 119
Alefu
1Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa,
amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
2Odala ndi amene amasunga malamulo ake,
amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
3Sachita cholakwa chilichonse;
amayenda mʼnjira zake.
4Inu mwapereka malangizo
ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
5Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika
pa kumvera zophunzitsa zanu!
6Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi,
poganizira malamulo anu onse.
7Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama,
pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
8Ndidzamvera zophunzitsa zanu;
musanditaye kwathunthu.
Beti
9Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake?
Akawasamala potsata mawu anu.
10Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse;
musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
11Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga
kuti ndisakuchimwireni.
12Mutamandike Inu Yehova;
phunzitseni malamulo anu.
13Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse
amene amachokera pakamwa panu.
14Ndimakondwera potsatira malamulo anu
monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
15Ndimalingalira malangizo anu
ndipo ndimaganizira njira zanu.
16Ndimakondwera ndi malamulo anu;
sindidzayiwala konse mawu anu.
Gimeli
17Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo;
kuti tsono ndisunge mawu anu.
18Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona
zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
19Ine ndine mlendo pa dziko lapansi;
musandibisire malamulo anu.
20Moyo wanga wafowoka polakalaka
malamulo anu nthawi zonse.
21Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa,
amene achoka pa malamulo anu.
22Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo
pakuti ndimasunga malamulo anu.
23Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza,
mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
24Malamulo anu amandikondweretsa;
ndiwo amene amandilangiza.
Daleti
25Moyo wanga wakangamira fumbi;
tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
26Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha;
phunzitseni malamulo anu.
27Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu;
pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
28Moyo wanga wafowoka ndi chisoni;
limbikitseni monga mwa mawu anu.
29Mundichotse mʼnjira zachinyengo;
mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
30Ndasankha njira ya choonadi;
ndayika malamulo anu pa mtima panga.
31Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova;
musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
32Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu,
pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
He
33Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu;
ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
34Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu
ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
35Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu,
pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
36Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu,
osati chuma.
37Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe;
sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
38Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu,
kuti Inu muopedwe.
39Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa,
pakuti malamulo anu ndi abwino.
40Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu!
Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
Wawi
41Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova,
chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
42ndipo ndidzayankha amene amandinyoza,
popeza ndimadalira mawu anu.
43Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga,
pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
44Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse,
ku nthawi za nthawi.
45Ndidzayendayenda mwaufulu,
chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
46Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu
ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
47popeza ndimakondwera ndi malamulo anu
chifukwa ndimawakonda.
48Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda,
ndipo ndimalingalira malangizo anu.
Zayini
49Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu,
popeza mwandipatsa chiyembekezo.
50Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi:
lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
51Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa,
koma sindichoka pa malamulo anu.
52Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale,
ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
53Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa
amene ataya malamulo anu.
54Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga
kulikonse kumene ndigonako.
55Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova,
ndipo ndidzasunga malamulo anu.
56Ichi ndicho ndakhala ndikuchita:
ndimasunga malangizo anu.
Heti
57Yehova, Inu ndiye gawo langa;
ndalonjeza kumvera mawu anu.
58Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse;
mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
59Ndinalingalira za njira zanga
ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
60Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza
kumvera malamulo anu.
61Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe,
sindidzayiwala lamulo lanu.
62Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu
chifukwa cha malamulo anu olungama.
63Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani,
kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
64Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika,
phunzitseni malamulo anu.
Teti
65Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu
molingana ndi mawu anu.
66Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino,
pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
67Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera,
koma tsopano ndimamvera mawu anu.
68Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino;
phunzitseni malamulo anu.
69Ngakhale odzikuza andipaka mabodza,
ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
70Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa,
koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
71Ndi bwino kuti ndinasautsidwa
kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
72Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri
kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
Yodi
73Manja anu anandilenga ndi kundiwumba;
patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
74Iwo amene amakuopani akondwere akandiona,
chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
75Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama
ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
76Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa,
molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
77Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo,
popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
78Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa;
koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
79Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine,
iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
80Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu
kuti ndisachititsidwe manyazi.
Kafu
81Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu,
koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
82Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu;
Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
83Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi
sindiyiwala zophunzitsa zanu.
84Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti?
Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
85Anthu osalabadira za Mulungu,
odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
86Malamulo anu onse ndi odalirika;
thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
87Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi
koma sindinataye malangizo anu.
88Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika,
ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Lamedi
89Mawu anu Yehova ndi amuyaya;
akhazikika kumwambako.
90Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse;
Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
91Malamulo anu alipobe mpaka lero lino,
pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
92Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa,
ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
93Ine sindidzayiwala konse malangizo anu,
pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
94Ndine wanu, ndipulumutseni;
pakuti ndasamala malangizo anu.
95Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge,
koma ndidzalingalira umboni wanu.
96Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire,
koma malamulo anu alibe malire konse.
Memu
97Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu!
Ndimalingaliramo tsiku lonse.
98Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga,
popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
99Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse
popeza ndimalingalira umboni wanu.
100Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba,
popeza ndimamvera malangizo anu.
101Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa
kuti ndithe kumvera mawu anu.
102Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu,
pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
103Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa,
otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
104Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu;
kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Nuni
105Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga
ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
106Ndalumbira ndipo ndatsimikiza,
kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
107Ndazunzika kwambiri;
Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
108Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga,
ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
109Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi,
sindidzayiwala malamulo anu.
110Anthu oyipa anditchera msampha,
koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
111Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya;
Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
112Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu
mpaka kumapeto kwenikweni.
Samekhi
113Ndimadana ndi anthu apawiripawiri,
koma ndimakonda malamulo anu.
114Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa;
chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
115Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa,
kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
116Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo;
musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
117Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa;
nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
118Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu,
pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
119Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala;
nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
120Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu;
ndimachita mantha ndi malamulo anu.
Ayini
121Ndachita zolungama ndi zabwino;
musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
122Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino,
musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
123Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu,
kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
124Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika,
ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
125Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa,
kuti ndimvetsetse umboni wanu.
126Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu;
malamulo anu akuswedwa.
127Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu
kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
128ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka,
ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Pe
129Maumboni anu ndi odabwitsa
nʼchifukwa chake ndimawamvera.
130Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika;
ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
131Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu,
kufunafuna malamulo anu.
132Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo,
monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
133Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu;
musalole kuti tchimo lizindilamulira.
134Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza,
kuti ndithe kumvera malangizo anu.
135Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu
ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
136Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga,
chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Tsade
137Yehova ndinu wolungama,
ndipo malamulo anu ndi abwino.
138Maumboni amene munatipatsa ndi olungama;
ndi odalirika ndithu.
139Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga
chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
140Mawu anu ndi woyera kwambiri
nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
141Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka,
sindiyiwala malangizo anu.
142Chilungamo chanu nʼchamuyaya,
ndipo malamulo anu nʼchoona.
143Mavuto ndi masautso zandigwera,
koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
144Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse;
patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
Kofu
145Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova,
ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
146Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni
ndipo ndidzasunga umboni wanu.
147Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo;
chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
148Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku,
kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
149Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika;
Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
150Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira,
koma ali kutali ndi malamulo anu.
151Koma Inu Yehova muli pafupi,
malamulo anu onse ndi woona.
152Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu
kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
Reshi
153Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse,
pakuti sindinayiwale malamulo anu.
154Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola;
sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
155Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa,
pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
156Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu;
sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
157Adani amene akundizunza ndi ambiri,
koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
158Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro,
popeza samvera mawu anu.
159Onani momwe ndimakondera malangizo anu;
sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
160Mawu anu onse ndi owona;
malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
Sini ndi Shini
161Olamulira amandizunza popanda chifukwa,
koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
162Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu,
ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
163Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho,
koma ndimakonda malamulo anu.
164Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku
pakuti malamulo anu ndi olungama.
165Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu,
ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
166Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova,
ndipo ndimatsatira malamulo anu.
167Ndimamvera umboni wanu
pakuti ndimawukonda kwambiri.
168Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu,
pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
Tawu
169Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova;
patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
170Kupempha kwanga kufike pamaso panu;
pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
171Matamando asefukire pa milomo yanga,
pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
172Lilime langa liyimbe mawu anu,
popeza malamulo anu onse ndi olungama.
173Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza
pakuti ndasankha malangizo anu.
174Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova,
ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
175Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni,
ndipo malamulo anu andichirikize.
176Ndasochera ngati nkhosa yotayika,
funafunani mtumiki wanu,
pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Gottes gute Ordnungen sind nicht zu überbieten!119 Der Psalm besteht im Grundtext aus 22 Strophen zu je 8 Zeilen. Die Strophen folgen den 22 Buchstaben des hebräischen Alphabets. Innerhalb jeder Strophe beginnt jede Zeile mit demselben Buchstaben.
1.
1Glücklich sind die Menschen,
denen man nichts Böses nachsagen kann,
die sich stets nach dem Gesetz des Herrn richten.
2Glücklich sind alle, die sich an seine Weisungen halten
und von ganzem Herzen nach ihm fragen.
3Solche Menschen tun kein Unrecht,
sie leben so, wie es Gott gefällt.
4Was du, Herr, angeordnet hast,
das soll jeder genau beachten.
5Nichts soll mich davon abbringen können,
deine Ordnungen treu zu befolgen.
6Deine Gebote verliere ich nicht aus den Augen.
Darum brauche ich mich nicht zu schämen,
7sondern kann dich mit aufrichtigem Herzen loben.
Deine guten Gesetze lerne ich immer besser kennen.
8Ich will mich an deine Ordnungen halten –
hilf mir dabei und lass mich nicht im Stich!
2.
9Herr, wie kann ein junger Mensch leben,
ohne sich dabei schuldig zu machen?
Indem er sich nach deinem Wort richtet.
10Auch ich frage von ganzem Herzen nach dir;
lass mich doch nicht von dem Weg abkommen,
den deine Gebote mir weisen!
11Tief präge ich mir dein Wort ein,
damit ich nicht vor dir schuldig werde.
12Herr, dich will ich loben und preisen!
Lehre mich, deine Ordnungen zu verstehen!
13Alle Anweisungen, die du gegeben hast,
sage ich mir immer wieder auf.
14Ein Leben nach deinen Geboten zu führen
erfreut mich mehr als jeder Reichtum.
15Ich denke über deine Vorschriften nach
und halte mir deinen Willen vor Augen.
16Deine Gesetze machen mich glücklich;
nie werde ich dein Wort vergessen.
3.
17Herr, ich bin dein Diener! Erweise mir deine Güte,
denn nur so kann ich leben und dein Wort befolgen.
18Öffne mir die Augen, damit ich erkenne,
welche Wunder dein Gesetz enthält!
19Diese Welt wird nicht für immer meine Heimat sein.
Umso mehr brauche ich deine Gebote –
verheimliche sie nicht vor mir!
20Ich wünsche mir nichts sehnlicher,
als deine Weisungen stets vor Augen zu haben.
21Du strafst die Selbstgerechten und verfluchst alle,
die sich über deine Gebote hinwegsetzen.
22Lass sie nicht länger über mich spotten –
ich halte mich doch an das, was du sagst!
23Mögen sich auch mächtige Leute verbünden
und gemeine Pläne gegen mich schmieden,
bleibe ich trotz allem dein Diener
und denke über deine Ordnungen nach.
24Über deine Gesetze freue ich mich,
denn sie sind hervorragende Ratgeber.
4.
25Herr, ich bin am Boden zerstört.
Schenke mir neue Kraft, wie du es versprochen hast!
26Schon oft habe ich meine Not vor dich gebracht,
und du hast mir immer geholfen.
Zeige mir auch jetzt, was ich tun soll!
27Hilf mir, deine Weisungen zu verstehen,
damit ich über deine Wunder nachdenken kann.
28Vor Kummer gehe ich fast zugrunde.
Richte mich wieder auf – du hast es doch zugesagt!
29Bewahre mich davor, unehrlich zu sein,
und gewähre mir das Vorrecht, dein Gesetz zu kennen!
30Ich habe mich entschlossen, dir treu zu bleiben.
Darum will ich mir immer vor Augen halten,
was du als göttliches Recht festgelegt hast.
31Herr, unbeirrbar halte ich an deinen Anordnungen fest.
Lass nicht zu, dass ich deswegen Schimpf und Schande ernte!
32Zielstrebig will ich den Weg gehen, den deine Gebote mir weisen,
denn du machst mein Herz verständig und bereit119,32 Wörtlich: denn du machst mir das Herz weit..
5.
33Herr, zeige mir, was deine Ordnungen bedeuten!
Ich will sie beachten, solange ich lebe.
34Gib mir Einsicht, damit ich dein Gesetz befolgen kann
und mich von ganzem Herzen danach richte!
35Hilf mir, deine Gebote zu erfüllen,
denn das bereitet mir große Freude.
36Gib mir Liebe zu deinem Wort
und lass mich nicht in Habgier verfallen!
37Ich will mich nicht mit sinnlosen Dingen abgeben;
schenk du mir die Kraft, den richtigen Weg zu gehen!
38Herr, löse doch deine Zusagen ein,
die du allen gegeben hast, die dir mit Ehrfurcht begegnen.
39Ich habe Angst, dass man mich verlacht und beschimpft,
doch ich weiß: Deine Rechtsentscheidungen sind gut.
40Ich sehne mich danach, deinen Befehlen zu gehorchen.
Weil du für Gerechtigkeit sorgst, lebe ich wieder auf.
6.
41Herr, zeige mir doch, wie sehr du mich liebst,
und hilf mir, wie du es versprochen hast!
42Dann kann ich denen die passende Antwort geben,
die jetzt noch verächtlich über mich reden.
Denn ich vertraue auf das, was dein Wort mir sagt.
43Auf deine Weisungen habe ich meine Hoffnung gesetzt.
Lass mich nun nicht als Lügner dastehen,
wenn ich von deiner Treue berichte!
44Niemals will ich aufhören,
dein Gesetz zu befolgen.
45Ich führe mein Leben in Freiheit und Glück,
weil ich deine Ordnungen erforsche.
46Sogar vor Königen will ich ohne Scheu bezeugen,
dass dein Gesetz unumstößlich gilt.
47Ich befolge deine Gebote mit Freude,
ja, so sehr liebe ich sie!
48Ich sehne mich nach deinen Worten,
denn sie sind wertvoll für mich;
über alles, was du angeordnet hast, denke ich gründlich nach.
7.
49Herr, mach dein Versprechen wahr,
das mich, deinen Diener, wieder hoffen ließ.
50Denn immer, wenn ich in Not geriet,
hat deine Zusage mich getröstet und belebt.
51Selbstgefällige Leute ziehen ständig über mich her;
trotzdem weiche ich kein Stück von deinem Gesetz ab.
52Ich verliere nicht den Mut, denn ich erinnere mich daran,
wie du schon früher für Recht gesorgt hast.
53Mich packt der Zorn, wenn ich an die Menschen denke,
die sich von dir und deinem Gesetz losgesagt haben.
54Ich aber werde deine Ordnungen besingen,
solange ich ein Gast auf dieser Erde bin.
55Herr, sogar in der Nacht denke ich an dich,
und deine Gebote will ich gern befolgen.
56Ja, es ist mir zur Gewohnheit geworden,
unbeirrt nach deinen Leitlinien zu leben.
8.
57Du, Herr, bist alles, was ich brauche!
Deshalb werde ich tun, was du sagst.
58Von ganzem Herzen flehe ich dich an:
Sei mir gnädig, wie du es versprochen hast!
59Ich gebe mir Rechenschaft über mein Leben
und richte mich wieder neu nach deinen Geboten aus.
60Ich zögere nicht und will keine Zeit verlieren,
das zu tun, was du befohlen hast.
61Die Leute, die sich dir widersetzen, wollen mich zu Fall bringen,
doch ich vergesse dein Gesetz nicht.
62Mitten in der Nacht stehe ich auf, um dir zu danken,
weil deine Urteile gerecht sind.
63Wer Ehrfurcht vor dir hat und nach deinen Maßstäben lebt,
der ist mein Freund.
64Herr, die ganze Erde ist erfüllt von deiner Güte.
Lehre mich, deine Ordnungen zu verstehen!
9.
65Herr, du bist gut zu mir, deinem Diener,
ganz so, wie du es versprochen hast.
66Schenke mir Urteilskraft und Verständnis,
denn auf deine Gebote verlasse ich mich.
67Ich bin viele Irrwege gegangen, bis ich in Bedrängnis geriet
und schließlich umkehren musste.
Daher will ich mich jetzt nach deinem Willen richten.
68Gott, du bist gut – dir verdanke ich so viel!
Lass mich deine Ordnungen verstehen!
69Unverfrorene Lügner ziehen meinen Namen in den Schmutz,
aber ich befolge unbeirrbar deine Weisungen.
70Ihr Gewissen ist abgestumpft; an ihnen prallt alles ab, was du sagst.
Ich aber freue mich über dein Gesetz.
71Für mich war es gut, dass ich in Bedrängnis geriet
und schließlich umkehren musste.
Denn da erst lernte ich, wie hilfreich deine Gebote sind.
72Ja, dein Gesetz ist wertvoller für mich
als Berge von Silber und Gold!
10.
73Herr, mein Schöpfer! Du hast mir das Leben gegeben.
Schenke mir nun auch die Einsicht, die ich brauche,
um nach deinen Geboten zu leben!
74Alle, die Ehrfurcht vor dir haben, werden sich über mich freuen,
denn ich verlasse mich auf dein Wort.
75Herr, ich weiß, dass deine Entscheidungen richtig sind.
Selbst als du mich leiden ließest, meintest du es gut mit mir.119,75 Wörtlich: In Treue hast du mich gebeugt.
76Lass mich deine Gnade erfahren
und tröste mich, wie du es versprochen hast!
77Dein Gesetz befolge ich gerne.
Erbarme dich über mich und hilf mir, denn nur so kann ich leben.
78Bring die unverschämten Lügner zu Fall;
sie haben mich grundlos ins Elend gestürzt.
Ich aber denke über deine Ordnungen nach.
79Ich wünsche mir, dass alle zu mir halten,
die dich ehren und deine Anweisungen befolgen.
80Entschlossen will ich mich nach deinen Geboten richten,
damit ich mich nicht zu schämen brauche.
11.
81Voller Sehnsucht warte ich auf deine Hilfe,
ich setze alle meine Hoffnung auf dein Wort.
82Ich vergehe fast vor Ungeduld, bis du deine Zusage erfüllst.
Wann endlich tröstest du mich?
83Ich fühle mich nutzlos, alt und verbraucht;119,83 Wörtlich: Ich bin wie ein Weinschlauch im Rauch.
trotzdem werde ich nicht müde, deine Ordnungen zu befolgen.
84Wie lange muss ich noch warten? Ich bin doch dein Diener!
Wann gehst du endlich mit denen ins Gericht,
die es auf mich abgesehen haben?
85In ihrem Stolz haben sie mir eine Grube gegraben;
dein Gesetz ist ihnen völlig gleichgültig.
86Hilf mir, denn sie verfolgen mich ohne Grund!
Doch auf deine Gebote kann ich mich verlassen.
87Ich weigere mich, gegen deine Anordnungen zu verstoßen,
obwohl die Feinde mich fast umgebracht hätten.
88Sei mir gnädig und bewahre mein Leben!
Dann kann ich mich weiterhin an das halten, was dein Wort bezeugt!
12.
89Herr, dein Wort bleibt für immer und ewig –
so unverrückbar wie der Himmel hat es Bestand.
90Deine Treue zu uns gilt ohne Ende –
so unerschütterlich wie die Erde, die du erschufst.
91Himmel und Erde bestehen bis heute,
weil du es so willst, denn dir muss alles dienen.
92Hätte ich nicht Freude an deinem Gesetz gehabt,
dann wäre ich in meinem Elend umgekommen.
93Nie will ich deine Befehle vergessen,
denn durch sie hast du mich neu belebt.
94Herr, ich gehöre zu dir. So hilf mir doch,
denn ich habe immer nach deinen Geboten gefragt!
95Gewissenlose Menschen liegen auf der Lauer, um mich zu beseitigen.
Doch ich achte umso mehr auf das, was du mir sagst.
96Ich sah, dass alles ein Ende findet,
auch wenn es noch so vollkommen ist.
Nur dein Wort kennt keine Grenzen.
13.
97Herr, wie sehr liebe ich dein Gesetz;
den ganzen Tag denke ich darüber nach!
98Gerade weil es mir immer gegenwärtig ist,
bin ich meinen Feinden an Klugheit überlegen.
99Ich habe mehr begriffen als alle meine Lehrer,
denn ich mache mir ständig Gedanken über deine Ordnungen.
100Ich besitze mehr Einsicht als alte Menschen mit ihrer Erfahrung,
denn ich habe mein Leben nach deinen Geboten ausgerichtet.
101Von krummen Wegen hielt ich mich stets fern,
damit ich nicht gegen dein Wort verstoße.
102Ich habe deine Belehrungen gerne angenommen,
denn einen besseren Lehrer als dich gibt es nicht.
103Dein Wort ist meine Lieblingsspeise,
es ist süßer als der beste Honig.
104Dein Gesetz macht mich einsichtig und klug,
deshalb ist mir jede Art von Falschheit verhasst.
14.
105Dein Wort ist wie ein Licht in der Nacht,
das meinen Weg erleuchtet.
106Was du in deinem Wort festgelegt hast,
das will ich tun, gerechter Gott!
Ich habe einen Eid darauf geleistet, und dazu stehe ich.
107Doch jetzt bin ich völlig am Ende!
Herr, schenke mir neue Kraft, wie du es versprochen hast!
108Ja, Herr, nimm meinen Dank als ein Opfer an
und lehre mich, deine Ordnungen zu verstehen!
109Mein Leben ist ständig in Gefahr,119,109 Wörtlich: Mein Leben halte ich ständig in der Hand.
trotzdem vergesse ich dein Gesetz nicht.
110Die Gottlosen wollen mich in ihre Fallen locken,
doch ich lasse mich nicht von deinen Geboten abbringen.
111Was uns als dein Wille überliefert wurde,
ist für alle Zeit mein kostbarer Besitz
und erfüllt mein Herz mit tiefer Freude.
112Ich bin entschlossen, mich an deine Weisungen zu halten –
jeden Tag meines Lebens, bis an mein Ende119,112 Oder: – für ewig ist mein Lohn!!
15.
113Herr, ich kann solche Menschen nicht leiden,
die einmal »Ja« und einmal »Nein« zu dir sagen;
aber dein Gesetz liebe ich mit ungeteiltem Herzen.
114Bei dir bin ich geborgen wie unter einem schützenden Schild,
auf deine Zusagen setze ich meine Hoffnung.
115Verschwindet, ihr Unheilstifter, hindert mich nicht –
denn ich will den Geboten meines Gottes gehorchen!
116Herr, gib mir festen Halt, wie du es versprochen hast,
dann lebe ich wieder auf!
Lass nicht zu, dass ich vergeblich hoffe.
117Richte mich auf, Herr, dann ist mir geholfen!
Immer will ich deine Ordnungen beachten.
118Wer deine Befehle in den Wind schlägt, den lehnst auch du ab;
solche Menschen schaden sich mit ihren Lügen nur selbst119,118 Wörtlich: denn umsonst ist ihr Trug..
119Wie Müll beseitigst du alle, die dich verachten.
Deshalb liebe ich, was du befiehlst.
120Aus Furcht vor dir läuft es mir kalt den Rücken herunter,
ich habe Angst, dass du mich verurteilen könntest.
16.
121Herr, ich habe getan, was richtig und gut ist,
darum überlass mich nicht der Willkür meiner Feinde!
122Versprich mir, dass alles wieder gut wird, und lass nicht zu,
dass mich diese selbstherrlichen Menschen unterdrücken!
123Gerechter Gott, ich sehne mich danach, dass du mich befreist
und das Versprechen erfüllst, das du mir gegeben hast.
124Herr, du bist gnädig, darum hilf mir doch!
Lehre mich, deine Ordnungen zu verstehen!
125Dir will ich dienen; nun schenke mir auch die nötige Einsicht,
damit ich erkenne, was dein Wort befiehlt!
126Es ist höchste Zeit, dass du eingreifst, Herr,
denn die Menschen missachten dein Gesetz.
127Ich aber liebe deine Gebote –
sie bedeuten mir mehr als reines Gold.
128Jede Art von Falschheit ist mir verhasst.
Nur deine Gebote garantieren einen geraden Weg,
darum will ich mich genau an sie halten.
17.
129Herr, deine Gebote sind wunderbar,
deshalb befolge ich sie gern.
130Im Leben eines Menschen wird es hell,
wenn er anfängt, dein Wort zu verstehen.
Wer bisher gedankenlos durchs Leben ging, der wird jetzt klug.
131Mein Verlangen nach deinen Geboten
ist wie der Durst eines Menschen,
der in der Hitze nach Wasser lechzt.
132Herr, wende dich mir zu und sei mir gnädig,
so wie du es gegenüber allen bist, die dich lieben.
133Lenke meine Schritte durch dein Wort
und lass nicht zu, dass das Böse über mich Macht gewinnt!
134Erlöse mich aus der Gewalt der Menschen, die mich unterdrücken;
dann kann ich nach deinen Vorschriften leben!
135Blicke mich freundlich an, ich gehöre doch zu dir!
Lehre mich, deine Ordnungen zu verstehen!
136Ich weine hemmungslos, wenn ich sehe,
wie andere dein Gesetz missachten.
18.
137Du, Herr, bist ein gerechter Gott,
und was du beschließt, ist richtig und gut.
138Auf deine Weisungen kann man sich verlassen,
sie alle bezeugen deine große Treue.
139Ich bin außer mir vor Zorn, weil ich sehe,
wie meine Feinde deine Worte übergehen.
140Was du sagst, ist vollkommen zuverlässig,119,140 Wörtlich: Dein Wort ist ganz durchläutert.
darum liebe ich es und will dir dienen.
141Obwohl ich klein und verachtet bin,
vergesse ich deine Ordnungen nicht.
142Deine Gerechtigkeit bleibt für immer bestehen;
dein Gesetz ist die reine Wahrheit.
143Selbst wenn ich vor Angst keinen Ausweg mehr weiß,
freue ich mich noch über deine Gebote;
144sie sind gerecht, und daran wird sich nie etwas ändern.
Hilf mir, sie zu verstehen, denn nur so kann ich leben!
19.
145Herr, ich flehe dich an: Erhöre mich!
An deine Ordnungen will ich mich halten.
146Ich rufe laut: Rette mich doch;
wie gern möchte ich deine Gebote befolgen!
147Schon vor Tagesanbruch schreie ich zu dir um Hilfe,
ich setze alle meine Hoffnung auf dein Wort.
148Voller Erwartung bleibe ich die ganze Nacht wach
und denke über das nach, was du mir sagst.
149Höre mich, Herr, in deiner großen Liebe;
erhalte mein Leben durch dein gerechtes Urteil.
150Böse Menschen machen sich an mich heran, um mir zu schaden;
wie weit haben sie sich von deinem Gesetz entfernt!
151Aber du, Herr, du bist mir nahe!
Auf alle deine Gebote kann ich mich verlassen.
152Schon lange weiß ich, dass du dein Gesetz erlassen hast,
damit es für alle Zeiten gilt!
20.
153Herr, sieh doch, wie niedergeschlagen ich bin!
Hilf mir, denn ich habe dein Gesetz nie aus den Augen verloren.
154Nimm dich meiner Sache an und sorge für Recht,
ja, erhalte mein Leben, so wie du es versprochen hast!
155Wer sich dir widersetzt,
kann nicht damit rechnen, dass du ihn rettest,
denn deine Ordnungen sind ihm gleichgültig.
156Herr, schon oft hast du dein Erbarmen gezeigt;
richte mich auch jetzt wieder auf durch dein gerechtes Urteil!
157Viele Feinde verfolgen und bedrängen mich,
trotzdem weiche ich kein Stück von deinen Geboten ab.
158Ich empfinde Abscheu und Ekel, wenn ich mir die Menschen ansehe,
die dir untreu sind und sich über dein Wort hinwegsetzen.
159Herr, sieh doch, wie sehr ich deine Befehle liebe!
Du bist gnädig, darum schenke mir wieder neue Kraft!
160Jedes Wort, das du sagst, ist wahr.
Was du, gerechter Gott, entschieden hast, gilt für immer und ewig.
21.
161Herr, die Mächtigen verfolgen mich ohne Grund,
doch mich beeindruckt allein das, was du mir sagst.
162Ich freue mich über dein Wort wie jemand,
der einen wertvollen Schatz findet.
163Ich verabscheue gemeine Lügen,
dein Gesetz aber liebe ich.
164Siebenmal am Tag lobe ich dich, Herr,
denn deine Entscheidungen sind gut und gerecht.
165Wer dein Gesetz lieb hat, lebt in Frieden und Glück –
ein solcher Mensch wird niemals scheitern.
166Herr, ich hoffe darauf, dass du mich rettest,
denn ich habe mich nach deinen Geboten gerichtet.
167Deine Weisungen sind der Maßstab für mein Handeln;
ich habe sie fest ins Herz geschlossen.
168Ja, deine Befehle und Mahnungen befolge ich,
denn du siehst alles, was ich tue.
22.
169Herr, ich flehe dich an: Erhöre mich!
Gib mir die Einsicht, die dein Wort verspricht!
170Höre auf mein Schreien und rette mich,
so wie du es zugesagt hast!
171Ich will dich von Herzen loben,
denn du lässt mich deine Ordnungen verstehen.
172Fröhlich besinge ich dein Wort,
denn alles, was du befiehlst, ist richtig und gut.
173Greif ein und komm mir zu Hilfe!
Ich habe meine Wahl getroffen:
Nur deine Gebote sollen der Maßstab für mein Leben sein.
174Sehnsüchtig warte ich auf deine Hilfe;
Herr, dein Gesetz ist meine größte Freude.
175Ich möchte leben, um dich zu preisen;
deine Ordnungen mögen mich dabei leiten!
176Heimatlos irre ich umher wie ein Schaf, das seine Herde verloren hat.
Suche doch nach mir, denn ich gehöre zu dir!
Ich habe nicht vergessen, was du befohlen hast.