Masalimo 116 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 116:1-19

Salimo 116

1Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga;

Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.

2Pakuti ananditchera khutu,

ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.

3Zingwe za imfa zinandizinga,

zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera;

ndinapeza mavuto ndi chisoni.

4Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova:

“Inu Yehova, pulumutseni!”

5Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama

Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.

6Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima;

pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.

7Pumula iwe moyo wanga,

pakuti Yehova wakuchitira zokoma.

8Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa,

maso anga ku misozi,

mapazi anga kuti angapunthwe,

9kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova

mʼdziko la anthu amoyo.

10Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati,

“Ndasautsidwa kwambiri.”

11Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati,

“Anthu onse ndi abodza.”

12Ndingamubwezere chiyani Yehova,

chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?

13Ndidzakweza chikho cha chipulumutso

ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.

14Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova

pamaso pa anthu ake onse.

15Imfa ya anthu oyera mtima

ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.

16Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu:

ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu;

Inu mwamasula maunyolo anga.

17Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu

ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.

18Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova

pamaso pa anthu ake onse,

19mʼmabwalo a nyumba ya Yehova,

mʼkati mwako iwe Yerusalemu.

Tamandani Yehova.

Nueva Versión Internacional

Salmo 116:1-19

Salmo 116

1Yo amo al Señor

porque él escucha116:1 Yo amo … él escucha. Lit. Yo amo porque el Señor escucha. mi voz de súplica.

2Por cuanto él inclina a mí su oído,

lo invocaré toda mi vida.

3Los lazos de la muerte me enredaron;

me sorprendió la angustia del sepulcro116:3 sepulcro. Lit. Seol.

y caí en la ansiedad y la aflicción.

4Entonces clamé al Señor:

«¡Te ruego, Señor, que me salves la vida!».

5El Señor es misericordioso y justo;

nuestro Dios es compasivo.

6El Señor protege a la gente sencilla;

estaba yo muy débil, y él me salvó.

7¡Ya puedes, alma mía, estar tranquila,

porque el Señor ha sido bueno contigo!

8Tú, Señor, me has librado de la muerte,

has enjugado mis lágrimas,

no me has dejado tropezar.

9Por eso andaré siempre delante del Señor

en esta tierra de los vivientes.

10Yo creí, aunque dije:

«Estoy muy afligido».

11En mi angustia llegué a decir:

«Todos son unos mentirosos».

12¿Cómo puedo pagarle al Señor

por tanta bondad que me ha mostrado?

13¡Tan solo brindando con la copa de salvación

e invocando el nombre del Señor!

14¡Tan solo cumpliendo mis promesas al Señor

en presencia de todo su pueblo!

15Mucho valor tiene a los ojos del Señor

la muerte de sus fieles.

16Yo, Señor, soy tu siervo;

soy siervo tuyo, hijo de tu sierva;

¡tú has roto mis cadenas!

17Te ofreceré un sacrificio de gratitud

e invocaré, Señor, tu nombre.

18Cumpliré mis promesas al Señor

en presencia de todo su pueblo,

19en los atrios de la casa del Señor,

en medio de ti, oh Jerusalén.

¡Aleluya!