Masalimo 115 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 115:1-18

Salimo 115

1Kwa ife ayi Yehova, kwa ife ayi

koma ulemerero ukhale pa dzina lanu,

chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika ndiponso chifukwa cha kukhulupirika kwanu.

2Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akunena kuti,

“Mulungu wawo ali kuti?”

3Mulungu wathu ali kumwamba;

Iye amachita chilichonse chimene chimamukondweretsa.

4Koma mafano awo ndi siliva ndi golide,

opangidwa ndi manja a anthu.

5Pakamwa ali napo koma sayankhula,

maso ali nawo koma sapenya;

6makutu ali nawo koma samva,

mphuno ali nazo koma sanunkhiza;

7manja ali nawo koma akakhudza samva kanthu;

mapazi ali nawo koma sayenda;

kapena pakhosi pawo kutulutsa mawu.

8Anthu amene amapanga mafanowo adzafanana nawo,

chimodzimodzinso onse amene amadalira mafanowo.

9Inu Aisraeli, dalirani Yehova;

Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.

10Iwe nyumba ya Aaroni, dalira Yehova;

Iye ndiye thandizo lako ndi chishango chako.

11Inu amene mumaopa Iye, dalirani Yehova;

Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.

12Yehova watikumbukira ndipo adzatidalitsa:

adzadalitsa nyumba ya Israeli,

adzadalitsa nyumba ya Aaroni,

13adzadalitsa iwo amene amaopa Yehova;

aangʼono ndi aakulu omwe.

14Yehova akuwonjezereni madalitso;

inuyo pamodzi ndi ana anu.

15Mudalitsidwe ndi Yehova,

Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

16Kumwamba ndi kwa Yehova,

koma dziko lapansi Iye walipereka kwa anthu.

17Si anthu akufa amene amatamanda Yehova,

amene amatsikira kuli chete;

18ndi ife amene timatamanda Yehova,

kuyambira tsopano mpaka muyaya.

Tamandani Yehova.

New Serbian Translation

Псалми 115:1-18

Псалам 115

1Немој нама, о, Господе, немој нама,

већ имену своме славу подај,

због милости своје и истине своје!

2Зашто народи да говоре:

„Тај Бог њихов, где је?“

3А Бог наш је на небесима

и он чини све што му се прохте!

4Сребро су и злато њихови идоли,

људских руку дело.

5Са устима – а неми,

са очима – а слепи;

6са ушима – а глуви

и са носем који не мирише;

7са рукама које не пипају,

са ногама које се не крећу

и са грлом што ни глас да пусти.

8Такви ће да буду ти што су их начинили,

сви који се у њих поуздају!

9Израиљу, у Господа се уздај!

Он им је помоћник, он им је штит!

10Доме Аронов, у Господа се уздај!

Он им је помоћник, он им је заштитник!

11Ви што стрепите од Господа,

у Господа се уздајте!

Он им је помоћник, он им је заштитник!

12Сетио се и нас Господ!

Нек нас благослови,

нека благослови дом Израиљев;

нека благослови дом Аронов!

13Благословиће оне што стрепе од Господа,

како мале тако и велике.

14Умножио вас Господ,

и вас и децу вашу!

15Благословио вас Господ,

Саздатељ небеса и земље!

16Небеса су Господња небеса,

а земљу је дао потомцима људи.

17Преминули не славе Господа,

ни сви што у покој иду;

18а ми Господа славимо

сада и довека!

Славите Господа!