Masalimo 115 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 115:1-18

Salimo 115

1Kwa ife ayi Yehova, kwa ife ayi

koma ulemerero ukhale pa dzina lanu,

chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika ndiponso chifukwa cha kukhulupirika kwanu.

2Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akunena kuti,

“Mulungu wawo ali kuti?”

3Mulungu wathu ali kumwamba;

Iye amachita chilichonse chimene chimamukondweretsa.

4Koma mafano awo ndi siliva ndi golide,

opangidwa ndi manja a anthu.

5Pakamwa ali napo koma sayankhula,

maso ali nawo koma sapenya;

6makutu ali nawo koma samva,

mphuno ali nazo koma sanunkhiza;

7manja ali nawo koma akakhudza samva kanthu;

mapazi ali nawo koma sayenda;

kapena pakhosi pawo kutulutsa mawu.

8Anthu amene amapanga mafanowo adzafanana nawo,

chimodzimodzinso onse amene amadalira mafanowo.

9Inu Aisraeli, dalirani Yehova;

Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.

10Iwe nyumba ya Aaroni, dalira Yehova;

Iye ndiye thandizo lako ndi chishango chako.

11Inu amene mumaopa Iye, dalirani Yehova;

Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.

12Yehova watikumbukira ndipo adzatidalitsa:

adzadalitsa nyumba ya Israeli,

adzadalitsa nyumba ya Aaroni,

13adzadalitsa iwo amene amaopa Yehova;

aangʼono ndi aakulu omwe.

14Yehova akuwonjezereni madalitso;

inuyo pamodzi ndi ana anu.

15Mudalitsidwe ndi Yehova,

Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

16Kumwamba ndi kwa Yehova,

koma dziko lapansi Iye walipereka kwa anthu.

17Si anthu akufa amene amatamanda Yehova,

amene amatsikira kuli chete;

18ndi ife amene timatamanda Yehova,

kuyambira tsopano mpaka muyaya.

Tamandani Yehova.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 115:1-18

第 115 篇

上帝是獨一真神

(平行經文:詩篇135·15-20

1耶和華啊,

不要將榮耀歸於我們,

不要歸於我們。

願榮耀歸於你的名,

因為你慈愛、信實!

2為何讓列國說

「他們的上帝在哪裡」?

3我們的上帝高居在天,

按自己的旨意行事。

4他們的神像不過是人用金銀造的。

5它們有口不能言,有眼不能看,

6有耳不能聽,有鼻不能聞,

7有手不能摸,有腳不能走,

有喉嚨也不能發聲。

8那些製造它們、信靠它們的人也會和它們一樣。

9以色列人啊,要信靠耶和華!

祂是你們的幫助,

是你們的盾牌。

10亞倫家啊,要信靠耶和華!

祂是你們的幫助,

是你們的盾牌。

11敬畏耶和華的人啊,要信靠祂!

祂是你們的幫助,

是你們的盾牌。115·4-11 平行經文:詩篇135·15-20

12耶和華眷顧我們,賜福給我們。

祂要賜福給以色列人,

賜福給亞倫家。

13耶和華要賜福給一切敬畏祂的人,

不分尊貴卑賤。

14願耶和華使你們和你們的後代人丁興旺!

15願創造天地的耶和華賜福給你們!

16高天屬於耶和華,

但祂把大地賜給了世人。

17死人不能歌頌耶和華,

下到墳墓的人不能讚美祂。

18但我們要讚美耶和華,

從現在直到永遠。

你們要讚美耶和華!