Masalimo 113 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 113:1-9

Salimo 113

1Tamandani Yehova.

Mutamandeni, inu atumiki a Yehova,

tamandani dzina la Yehova.

2Yehova atamandidwe,

kuyambira tsopano mpaka muyaya.

3Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake,

dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.

4Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse,

ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.

5Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu,

Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?

6amene amawerama pansi kuyangʼana

miyamba ndi dziko lapansi?

7Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi

ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;

8amawakhazika pamodzi ndi mafumu,

pamodzi ndi mafumu a anthu ake.

9Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake

monga mayi wa ana wosangalala.

Tamandani Yehova.

New International Reader’s Version

Psalm 113:1-9

Psalm 113

1Praise the Lord.

Praise him, you who serve the Lord.

Praise the name of the Lord.

2Let us praise the name of the Lord,

both now and forever.

3From the sunrise in the east to the sunset in the west,

may the name of the Lord be praised.

4The Lord is honored over all the nations.

His glory reaches to the highest heavens.

5Who is like the Lord our God?

He sits on his throne in heaven.

6He bends down to look

at the heavens and the earth.

7He raises poor people up from the trash pile.

He lifts needy people out of the ashes.

8He causes them to sit with princes.

He causes them to sit with the princes of his people.

9He gives children to the woman who doesn’t have any children.

He makes her a happy mother in her own home.

Praise the Lord.