Masalimo 112 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 112:1-10

Salimo 112

1Tamandani Yehova.

Wodala munthu amene amaopa Yehova,

amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.

2Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko;

mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.

3Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake,

ndipo chilungamo chake ndi chosatha.

4Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima;

wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.

5Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu,

amene amachita ntchito yake mwachilungamo.

6Ndithu sadzagwedezeka;

munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.

7Saopa akamva zoyipa zimene zachitika;

mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.

8Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha;

potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.

9Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka,

chilungamo chake chimanka mpaka muyaya;

nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.

10Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima;

adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka.

Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.

Nueva Versión Internacional

Salmo 112:1-10

Salmo 112Sal 112 Este salmo es un poema acróstico, que sigue el orden del alfabeto hebreo.

1¡Aleluya!

Álef

Dichoso el que teme al Señor,

Bet

el que halla gran deleite en sus mandamientos.

Guímel

2Su descendencia será poderosa en la tierra;

Dálet

la generación de los justos será bendecida.

He

3En su casa habrá abundantes riquezas

Vav

y para siempre permanecerá su justicia.

Zayin

4Para los justos la luz brilla en las tinieblas;

Jet

para los que son misericordiosos, compasivos y justos.

Tet

5Bien le va al que presta con generosidad,

Yod

y maneja sus negocios con justicia.

Lámed

6El justo jamás caerá;

Caf

su recuerdo permanecerá para siempre.

Mem

7No temerá recibir malas noticias;

Nun

su corazón estará firme, confiado en el Señor.

Sámej

8Su corazón estará seguro, sin temor alguno,

Ayin

y al final verá derrotados a sus adversarios.

Pe

9Reparte sus bienes entre los pobres;

Tsade

su justicia permanece para siempre;

Qof

su poder112:9 poder. Lit. cuerno. será gloriosamente exaltado.

Resh

10El malvado verá esto y se irritará;

Shin

rechinará los dientes y se irá consumiendo.

Tav

¡Los deseos de los malvados se frustrarán!