Masalimo 112 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 112:1-10

Salimo 112

1Tamandani Yehova.

Wodala munthu amene amaopa Yehova,

amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.

2Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko;

mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.

3Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake,

ndipo chilungamo chake ndi chosatha.

4Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima;

wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.

5Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu,

amene amachita ntchito yake mwachilungamo.

6Ndithu sadzagwedezeka;

munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.

7Saopa akamva zoyipa zimene zachitika;

mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.

8Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha;

potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.

9Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka,

chilungamo chake chimanka mpaka muyaya;

nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.

10Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima;

adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka.

Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.

New Russian Translation

Псалтирь 112:1-9

Псалом 112

1Аллилуйя!

Воздайте хвалу Господу, слуги Господни,

воздайте хвалу имени Господа!

2Да будет прославлено имя Господне

отныне и вовеки!

3От востока и до запада112:3 Букв.: «От восхода солнца и до заката».

да будет прославлено имя Господне!

4Господь превознесен над всеми народами,

и слава Его выше небес.

5Кто подобен Господу, нашему Богу,

восседающему на троне в вышине?

6Он склоняется, чтобы взирать

на происходящее на небе и на земле.

7Он поднимает бедного из праха

и возвышает нищего из грязи,

8чтобы посадить их с вождями,

с вождями их народа.

9Бесплодную женщину вселяет в дом

счастливой матерью.

Аллилуйя!