Masalimo 112 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 112:1-10

Salimo 112

1Tamandani Yehova.

Wodala munthu amene amaopa Yehova,

amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.

2Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko;

mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.

3Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake,

ndipo chilungamo chake ndi chosatha.

4Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima;

wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.

5Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu,

amene amachita ntchito yake mwachilungamo.

6Ndithu sadzagwedezeka;

munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.

7Saopa akamva zoyipa zimene zachitika;

mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.

8Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha;

potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.

9Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka,

chilungamo chake chimanka mpaka muyaya;

nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.

10Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima;

adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka.

Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 112:1-10

第 112 篇

敬畏上帝者必蒙福

1你們要讚美耶和華!

敬畏耶和華、樂於遵行祂命令的人有福了!

2他的子孫在世上必興盛,

正直人的後代必蒙福。

3他的家財豐厚,

他的公義永存。

4黑暗中必有光照亮正直人,

照亮有恩慈、好憐憫、行公義的人。

5慷慨借貸,

行事公正的人必亨通。

6他必永不動搖,

義人必永遠蒙眷顧。

7他不怕惡訊,

他堅定地信靠耶和華。

8他心裡鎮定自若,毫不害怕,

他終必戰勝仇敵。

9他慷慨施捨,賙濟窮人;

他的仁義永遠長存,

他必充滿力量,得享尊榮。

10惡人見狀,必然惱怒,

咬牙切齒,氣絕身亡。

惡人的盼望必破滅。