Masalimo 111 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 111:1-10

Salimo 111

1Tamandani Yehova.

Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse

mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.

2Ntchito za Yehova nʼzazikulu;

onse amene amakondwera nazo amazilingalira.

3Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu,

ndipo chilungamo chake ndi chosatha.

4Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike;

Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.

5Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye;

amakumbukira pangano lake kwamuyaya.

6Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake,

kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.

7Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama;

malangizo ake onse ndi odalirika.

8Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi,

ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.

9Iyeyo amawombola anthu ake;

anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya

dzina lake ndi loyera ndi loopsa.

10Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru;

onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu.

Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.

New Russian Translation

Псалтирь 111:1-10

Псалом 111111 Псалом 111 В оригинале этот псалом написан в форме акростиха, т. е. каждая строка начинается с очередной буквы еврейского алфавита.

1Аллилуйя!

Блажен человек, боящийся Господа,

получающий большое наслаждение от Его повелений.

2Могущественным будет на земле его потомство;

поколение праведных благословится.

3Изобилие и богатство будут в его доме,

и его праведность будет пребывать вечно.

4Для честных восходит свет во тьме,

он милостив, милосерден и праведен111:4 Или: « … во тьме, потому что Бог … ».

5Благо человеку, который великодушен и щедро дает взаймы,

тому, кто ведет свои дела справедливо.

6Он никогда не поколеблется;

праведник будет в вечной памяти.

7Не побоится плохих известий;

сердце его твердо, уповая на Господа.

8Сердце его крепко – он не испугается;

он увидит падение своих врагов.

9Он щедро раздал свое имущество бедным,

и его праведность пребывает вовек,

рог111:9 Рог был символом могущества, власти и силы. его вознесется в славе.

10Нечестивый увидит и разозлится,

заскрипит зубами и исчезнет.

Желание нечестивых не сбудется.