Salimo 111
1Tamandani Yehova.
Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse
mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
2Ntchito za Yehova nʼzazikulu;
onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
3Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu,
ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
4Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike;
Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
5Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye;
amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
6Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake,
kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
7Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama;
malangizo ake onse ndi odalirika.
8Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi,
ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
9Iyeyo amawombola anthu ake;
anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya
dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
10Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru;
onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu.
Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.
第 111 篇
赞美上帝
1你们要赞美耶和华!
在正直人的大会中,
我要全心全意地称谢耶和华。
2耶和华的作为伟大,
所有喜欢的人都必思想。
3祂的作为荣耀威严,
祂的公义永远长存。
4祂的奇妙作为令人无法忘怀。
耶和华充满怜悯和恩惠。
5祂赐下粮食给那些敬畏祂的人,
祂永不忘记自己的约。
6祂向自己的子民彰显大能,
把列国的土地赐给他们。
7祂凭信实和公正行事,
祂的法则可靠,
8是凭信实和正直赐下的,
存到永永远远。
9祂救赎了自己的子民,
立了永远的约,
祂的名神圣可畏。
10智慧始于敬畏耶和华,
遵行祂命令者皆明睿。
祂永远当受赞美。