Masalimo 111 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 111:1-10

Salimo 111

1Tamandani Yehova.

Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse

mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.

2Ntchito za Yehova nʼzazikulu;

onse amene amakondwera nazo amazilingalira.

3Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu,

ndipo chilungamo chake ndi chosatha.

4Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike;

Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.

5Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye;

amakumbukira pangano lake kwamuyaya.

6Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake,

kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.

7Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama;

malangizo ake onse ndi odalirika.

8Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi,

ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.

9Iyeyo amawombola anthu ake;

anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya

dzina lake ndi loyera ndi loopsa.

10Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru;

onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu.

Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 111:1-10

第 111 篇

赞美上帝

1你们要赞美耶和华!

在正直人的大会中,

我要全心全意地称谢耶和华。

2耶和华的作为伟大,

所有喜欢的人都必思想。

3祂的作为荣耀威严,

祂的公义永远长存。

4祂的奇妙作为令人无法忘怀。

耶和华充满怜悯和恩惠。

5祂赐下粮食给那些敬畏祂的人,

祂永不忘记自己的约。

6祂向自己的子民彰显大能,

把列国的土地赐给他们。

7祂凭信实和公正行事,

祂的法则可靠,

8是凭信实和正直赐下的,

存到永永远远。

9祂救赎了自己的子民,

立了永远的约,

祂的名神圣可畏。

10智慧始于敬畏耶和华,

遵行祂命令者皆明睿。

祂永远当受赞美。