Masalimo 11 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 11:1-7

Salimo 11

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Mwa Yehova ine ndimathawiramo.

Nanga mungathe bwanji kunena kwa ine kuti,

“Thawira ku phiri lako ngati mbalame.

2Pakuti taona oyipa akunga mauta awo;

ayika bwino mivi yawo pa zingwe za uta,

pobisala pawo kuti alase

olungama mtima.

3Tsono ngati maziko awonongeka,

olungama angachite chiyani?”

4Yehova ali mʼNyumba yake yoyera;

Yehova ali pa mpando wake waufumu kumwamba.

Iye amayangʼanitsitsa ana a anthu;

maso ake amawayesa.

5Yehova amayesa olungama,

koma moyo wake umadana ndi oyipa,

amene amakonda zachiwawa.

6Iye adzakhuthulira pa oyipa

makala amoto ndi sulufule woyaka;

mphepo yotentha idzakhala yowayenera.

7Pakuti Yehova ndi wolungama,

Iye amakonda chilungamo;

ndipo anthu olungama adzaona nkhope yake.

New Russian Translation

Псалтирь 11:1-9

Псалом 11

1Дирижеру хора, под восьмиструнный инструмент. Псалом Давида.

2Господи, помоги, потому что не стало святого,

исчезли верные среди людей!

3Они обманывают друг друга;

от лживого сердца говорит их льстивый язык.

4Пусть погубит Господь всякий льстивый язык

и все хвастливые уста,

5что говорят: «Мы одержим победу устами.

Язык наш с нами – кто нам хозяин?»

6«Так как слабых теснят

и бедные стонут,

Я ныне восстану, – говорит Господь. –

Я дам им желанное спасение».

7Слова Господа – слова чистые,

как серебро, что очищено в горне,

переплавлено семь раз.

8Господи, Ты сохранишь нас,

сбережешь нас от этого рода вовек.

9Повсюду расхаживают нечестивые,

когда у людей низость в почете.