Masalimo 11 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 11:1-7

Salimo 11

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Mwa Yehova ine ndimathawiramo.

Nanga mungathe bwanji kunena kwa ine kuti,

“Thawira ku phiri lako ngati mbalame.

2Pakuti taona oyipa akunga mauta awo;

ayika bwino mivi yawo pa zingwe za uta,

pobisala pawo kuti alase

olungama mtima.

3Tsono ngati maziko awonongeka,

olungama angachite chiyani?”

4Yehova ali mʼNyumba yake yoyera;

Yehova ali pa mpando wake waufumu kumwamba.

Iye amayangʼanitsitsa ana a anthu;

maso ake amawayesa.

5Yehova amayesa olungama,

koma moyo wake umadana ndi oyipa,

amene amakonda zachiwawa.

6Iye adzakhuthulira pa oyipa

makala amoto ndi sulufule woyaka;

mphepo yotentha idzakhala yowayenera.

7Pakuti Yehova ndi wolungama,

Iye amakonda chilungamo;

ndipo anthu olungama adzaona nkhope yake.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Salmo 11:1-7

Salmo 11

Al director musical. Salmo de David.

1En el Señor hallo refugio.

¿Cómo, pues, os atrevéis a decirme:

«Huye al monte, como las aves»?

2Ved cómo tensan sus arcos los malvados:

preparan las flechas sobre la cuerda

para disparar desde las sombras

contra los rectos de corazón.

3Cuando los fundamentos son destruidos,

¿qué le queda al justo?

4El Señor está en su santo templo,

en los cielos tiene el Señor su trono,

y atentamente observa al ser humano;

con sus propios ojos lo examina.

5El Señor examina a justos y a malvados,

y aborrece a los que aman la violencia.

6Hará llover sobre los malvados

ardientes brasas y candente azufre;

¡un viento abrasador será su suerte!

7Justo es el Señor, y ama la justicia;

por eso los íntegros contemplarán su rostro.