Masalimo 109 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 109:1-31

Salimo 109

Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Salimo la Davide.

1Mulungu amene ndimakutamandani,

musakhale chete,

2pakuti anthu oyipa ndi achinyengo

atsekula pakamwa pawo kutsutsana nane;

iwo ayankhula motsutsana nane ndi malilime abodza.

3Andizungulira ndi mawu audani,

amandinena popanda chifukwa.

4Mʼmalo mwa chikondi changa amandineneza,

koma ine ndine munthu wapemphero.

5Iwo amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino,

ndi udani mʼmalo mwa chikondi changa.

6Sankhani munthu woyipa kuti amutsutse iye;

lolani wotsutsa ayime ku dzanja lake lamanja.

7Pamene aweruzidwa, apezeke kuti ndi wolakwa,

ndipo mapemphero ake amutsutse.

8Masiku ake akhale owerengeka;

munthu wina atenge malo ake a utsogoleri.

9Ana ake akhale amasiye

ndipo mkazi wake akhale wopanda mwamuna.

10Ana ake akhale oyendayenda ndi opemphapempha;

apirikitsidwe kuchoka pa mabwinja a nyumba zawo.

11Wokongoza alande zonse zimene ali nazo;

alendo afunkhe ntchito za manja ake.

12Pasapezeke ndi mmodzi yemwe womukomera mtima

kapena kumvera chisoni ana ake amasiye.

13Zidzukulu zake zithe nʼkufa,

mayina awo afafanizidwe mu mʼbado wotsatirawo.

14Mphulupulu za makolo ake zikumbukiridwe pamaso pa Yehova;

tchimo la amayi ake lisadzafafanizidwe.

15Machimo awo akhale pamaso pa Yehova nthawi zonse,

kuti Iye achotse chikumbutso chawo pa dziko lapansi.

16Pakuti iye sanaganizirepo zochita chifundo,

koma anazunza mpaka kuwapha anthu osauka

ndi osweka mtima.

17Anakonda kutemberera,

matembererowo abwerere kwa iye;

sanakondwe nʼkudalitsa anthu ena,

choncho madalitso akhale kutali naye.

18Anavala kutemberera ngati chovala;

kutemberera kunalowa mʼthupi lake ngati madzi,

kulowa mʼmafupa ake ngati mafuta.

19Matemberero akhale ngati chofunda chodzikutira nacho,

ngati lamba wovala tsiku ndi tsiku.

20Awa akhale malipiro ochokera kwa Yehova pa onditsutsa anga,

kwa iwo amene amayankhula zoyipa za ine.

21Koma Inu Ambuye Wamphamvuzonse,

muchite nane molingana ndi dzina lanu,

chifukwa cha ubwino wa chikondi chanu, pulumutseni.

22Pakuti ndine wosauka ndi wosowa,

ndipo mtima wanga ukuwawa mʼkati mwanga.

23Ndikuzimirira ngati mthunzi wa kumadzulo,

ndapirikitsidwa ngati dzombe.

24Mawondo anga afowoka chifukwa cha kusala zakudya,

thupi langa lawonda ndi mutu wanga womwe.

25Ndine chinthu chotonzedwa kwa otsutsana nane;

akandiona, amapukusa mitu yawo.

26Thandizeni Inu Yehova Mulungu wanga;

pulumutseni molingana ndi chikondi chanu.

27Adaniwo adziwe kuti limeneli ndi dzanja lanu,

kuti Inu Yehova mwachita zimenezi.

28Angathe kutemberera, koma Inu mudzadalitsa;

pamene iwo andiputa adzachititsidwa manyazi,

koma mtumiki wanu adzasangalala.

29Onditsutsa adzavekedwa mnyozo,

ndipo adzadzifunditsa manyazi ngati chovala.

30Ndi pakamwa panga ndidzathokoza Yehova kwambiri;

ndidzamutamanda mʼgulu lalikulu la anthu.

31Popeza Iye amayima ku dzanja lamanja la munthu wosowayo,

kupulumutsa moyo wake kwa iwo amene agamula molakwa.

La Bible du Semeur

Psaumes 109:1-31

Sors de ton silence, ô Dieu !

1Au chef de chœur. Psaume de David.

Dieu, toi que je loue, ╵ne reste pas silencieux,

2car des gens méchants ╵ouvrent contre moi ╵leur bouche empreinte de tromperie,

et ils tiennent contre moi ╵des propos menteurs.

3Ils m’entourent de paroles ╵que la haine inspire.

Sans cause, ils me font la guerre.

4Pour prix de mon amitié, ╵ils m’ont accusé,

tandis que moi, je suis en prière.

5Ils me font du mal ╵pour le bien que je leur fais,

et mon amitié ╵est payée de haine.

6Soumets-le à un méchant109.6 Dans les v. 6-19, le psalmiste lance des imprécations contre ses adversaires qui sont motivées par le souci que la justice soit rétablie pour la gloire de Dieu, ainsi que par le désir légitime d’être délivré de ses ennemis. D’autres comprennent ces versets comme une citation des propos tenus par les « gens méchants » contre le psalmiste. !

Qu’un accusateur ╵se tienne à sa droite !

7Que, lors de son jugement, ╵il soit déclaré coupable,

que sa prière serve ╵à le condamner !

8Que ses jours soient abrégés,

qu’un autre prenne sa charge109.8 Cité en Ac 1.20. !

9Que ses fils soient orphelins,

que sa femme reste veuve,

10que ses enfants soient errants, ╵qu’ils mendient leur pain109.10 Texte hébreu traditionnel. L’ancienne version grecque a : qu’ils soient expulsés.,

et qu’ils soient réduits à quémander ╵loin de leur demeure en ruine !

11Que le créancier ╵prenne tout son bien !

Que des étrangers ravissent ╵le produit de son labeur !

12Qu’il n’y ait personne ╵qui lui manifeste ╵de la bienveillance

et qui ait pitié ╵de ses orphelins !

13Que ses descendants ╵soient exterminés

et qu’à la génération suivante, ╵leur nom disparaisse.

14Que le péché de ses pères ╵soit pris en compte par l’Eternel,

que les fautes de sa mère ╵ne soient jamais effacées !

15Que l’Eternel constamment, ╵les ait en ligne de mire !

Que leur souvenir ╵soit extirpé de la terre !

16Car cet homme ╵ne s’est jamais appliqué ╵à agir avec bonté,

et il a persécuté ╵le pauvre, le démuni,

l’homme au cœur brisé, ╵jusqu’à le faire mourir.

17Il aimait maudire : ╵que la malédiction vienne ╵le frapper !

Il refusait de bénir : ╵que la bénédiction fuie ╵loin de lui !

18Puisqu’il endossait ╵la malédiction ╵comme un vêtement,

qu’elle le pénètre ╵comme ferait l’eau,

et qu’elle entre en lui ╵jusque dans ses os ╵comme ferait l’huile109.18 Nb 5.17-28. !

19Qu’elle l’enveloppe ╵comme un vêtement,

comme une ceinture ╵sans cesse attachée ╵autour de ses reins !

20Que ce soit ainsi, ╵que l’Eternel paie ╵mes accusateurs

et ceux qui me calomnient.

21Et toi, Eternel, Seigneur,

interviens en ma faveur ╵en vue de ta renommée !

Toi dont l’amour est si bon, ╵viens me délivrer !

22Je suis affligé et pauvre

et mon cœur est déchiré ╵au-dedans de moi.

23Comme l’ombre qui s’étire, ╵je m’évanouis ;

et l’on me secoue ╵comme on le ferait ╵d’une sauterelle.

24Mes genoux flageolent ╵par l’effet du jeûne

et mon corps est amaigri.

25Je suis, pour ces gens, ╵un sujet de raillerie.

Dès qu’ils m’aperçoivent, ╵ils hochent la tête.

26A l’aide, Eternel, mon Dieu !

Sauve-moi dans ton amour !

27Que mes ennemis ╵puissent reconnaître

que c’est toi seul, Eternel, ╵toi seul qui as fait cela.

28Ils peuvent maudire, ╵toi, tu béniras !

Ils se dressent contre moi… ╵Ils seront couverts de honte !

Et ton serviteur ╵sera dans la joie.

29Que ceux qui m’accusent ╵soient couverts de déshonneur !

Qu’ils soient revêtus de honte ╵comme d’un manteau !

30Je célébrerai ╵l’Eternel à pleine voix,

et je le glorifierai ╵parmi les foules nombreuses,

31car il se tient aux côtés du pauvre

pour le délivrer ╵de ceux qui l’assignent ╵en justice.