Masalimo 108 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 108:1-13

Salimo 108

Nyimbo. Salimo la Davide.

1Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu;

ndidzayimba nyimbo, inde ndidzayimba nyimbo zotamanda ndi moyo wanga wonse.

2Dzukani, zeze ndi pangwe!

Ine ndidzadzutsa mʼbandakucha.

3Ndidzakutamandani Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina;

ndidzayimba za Inu pakati pa anthu a mitundu ina.

4Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kutalika kwake kuposa kumwamba;

kukhulupirika kwanu kumafika mlengalenga.

5Kwezekani Inu Mulungu, kuposa mayiko akumwamba,

ndipo ulemerero wanu uphimbe dziko lonse lapansi.

6Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja

kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.

7Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika:

“Mwachipambano Ine ndidzagawa Sekemu

ndipo ndidzayesa chigwa cha Sukoti.

8Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso;

Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera,

Yuda ndi ndodo yanga yaufumu.

9Mowabu ndi mbale yanga yosambiramo

ndidzaponya nsapato zanga pa Edomu;

ndidzafuwula mopambana pa Filisitiya.”

10Ndani adzandifikitsa ku mzinda wotetezedwa?

Ndani adzanditsogolera ku Edomu?

11Kodi sindinu Mulungu, Inu amene mwatikana

ndipo simuperekezanso magulu athu ankhondo?

12Tithandizeni ife kulimbana ndi mdani,

pakuti thandizo la munthu ndi lopanda pake.

13Chifukwa cha Mulungu wathu, ife tidzapeza chipambano,

ndipo adzapondereza pansi adani athu.

New International Version – UK

Psalms 108:1-13

Psalm 108In Hebrew texts 108:1-13 is numbered 108:2-14.

A song. A psalm of David.

1My heart, O God, is steadfast;

I will sing and make music with all my soul.

2Awake, harp and lyre!

I will awaken the dawn.

3I will praise you, Lord, among the nations;

I will sing of you among the peoples.

4For great is your love, higher than the heavens;

your faithfulness reaches to the skies.

5Be exalted, O God, above the heavens;

let your glory be over all the earth.

6Save us and help us with your right hand,

that those you love may be delivered.

7God has spoken from his sanctuary:

‘In triumph I will parcel out Shechem

and measure off the Valley of Sukkoth.

8Gilead is mine, Manasseh is mine;

Ephraim is my helmet,

Judah is my sceptre.

9Moab is my washbasin,

on Edom I toss my sandal;

over Philistia I shout in triumph.’

10Who will bring me to the fortified city?

Who will lead me to Edom?

11Is it not you, God, you who have rejected us

and no longer go out with our armies?

12Give us aid against the enemy,

for human help is worthless.

13With God we shall gain the victory,

and he will trample down our enemies.