Masalimo 108 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 108:1-13

Salimo 108

Nyimbo. Salimo la Davide.

1Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu;

ndidzayimba nyimbo, inde ndidzayimba nyimbo zotamanda ndi moyo wanga wonse.

2Dzukani, zeze ndi pangwe!

Ine ndidzadzutsa mʼbandakucha.

3Ndidzakutamandani Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina;

ndidzayimba za Inu pakati pa anthu a mitundu ina.

4Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kutalika kwake kuposa kumwamba;

kukhulupirika kwanu kumafika mlengalenga.

5Kwezekani Inu Mulungu, kuposa mayiko akumwamba,

ndipo ulemerero wanu uphimbe dziko lonse lapansi.

6Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja

kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.

7Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika:

“Mwachipambano Ine ndidzagawa Sekemu

ndipo ndidzayesa chigwa cha Sukoti.

8Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso;

Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera,

Yuda ndi ndodo yanga yaufumu.

9Mowabu ndi mbale yanga yosambiramo

ndidzaponya nsapato zanga pa Edomu;

ndidzafuwula mopambana pa Filisitiya.”

10Ndani adzandifikitsa ku mzinda wotetezedwa?

Ndani adzanditsogolera ku Edomu?

11Kodi sindinu Mulungu, Inu amene mwatikana

ndipo simuperekezanso magulu athu ankhondo?

12Tithandizeni ife kulimbana ndi mdani,

pakuti thandizo la munthu ndi lopanda pake.

13Chifukwa cha Mulungu wathu, ife tidzapeza chipambano,

ndipo adzapondereza pansi adani athu.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 108:1-13

第 108 篇

祈求上帝的帮助

大卫的诗歌。

1上帝啊!我的心坚定不移,

我要用心灵歌颂你。

2琴瑟啊,弹奏吧,

我要唤醒黎明。

3耶和华啊,我要在列邦称谢你,

在列国歌颂你。

4因为你的慈爱广及诸天,

你的信实高达穹苍。

5上帝啊,

愿你得到的尊崇超过诸天,

愿你的荣耀覆盖大地。

6求你应允我们的祷告,

伸出右手帮助我们,

使你所爱的人获救。

7上帝在祂的圣所说:

“我要欢然划分示剑,丈量疏割谷。

8基列是我的,玛拿西也是我的,

以法莲是我的头盔,

犹大是我的权杖。

9摩押是我的洗脚盆,

我要把鞋扔给以东

我要在非利士高唱凯歌。”

10谁能带我进入坚固的城池?

谁能领我到以东

11上帝啊,你抛弃了我们吗?

上帝啊,你不再和我们的军队一同出战了吗?

12求你帮助我们攻打仇敌,

因为人的帮助徒然无益。

13我们依靠上帝才能取胜,

祂必把我们的敌人踩在脚下。