BUKU LACHISANU
Masalimo 107–150
Salimo 107
1Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino;
pakuti chikondi chake ndi chosatha.
2Owomboledwa a Yehova anene zimenezi
amene Iyeyo anawawombola mʼdzanja la mdani,
3iwo amene anawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko,
kuchokera kumadzulo ndi kummawa, kuchokera kumpoto ndi kummwera.
4Ena anayendayenda mʼchipululu mopanda kanthu,
osapeza njira yopitira ku mzinda kumene akanakakhazikikako.
5Iwo anamva njala ndi ludzu,
ndipo miyoyo yawo inafowokeratu.
6Pamenepo analirira Yehova mʼmavuto awo
ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.
7Iye anawatsogolera mʼnjira yowongoka
kupita ku mzinda umene anakakhazikikako.
8Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha
ndi chifukwa cha machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,
9pakuti Iye wapha ludzu la munthu womva ludzu
ndipo wakhutitsa wanjala ndi zinthu zabwino.
10Ena anakhala mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu,
amʼndende ovutika mʼmaunyolo achitsulo,
11pakuti iwowo anawukira mawu a Mulungu
ndi kunyoza uphungu wa Wammwambamwamba.
12Kotero Iye anawapereka kuti agwire ntchito yakalavulagaga;
anagwa pansi ndipo panalibe woti awathandize.
13Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo
ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.
14Yehova anawatulutsa mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu
ndipo anadula maunyolo awo.
15Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha
ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,
16pakuti Iye amathyola zipata zamkuwa
ndi kudula pakati mipiringidzo yachitsulo.
17Ena anakhala zitsiru chifukwa cha njira zawo zowukira,
ndipo anamva zowawa chifukwa cha mphulupulu zawo.
18Iwo ananyansidwa ndi chakudya chilichonse
ndipo anafika pafupi ndi zipata za imfa.
19Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo
ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awowo.
20Iye anatumiza mawu ake ndi kuwachiritsa;
anawalanditsa ku manda.
21Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha
ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu.
22Apereke nsembe yachiyamiko
ndi kufotokoza za ntchito zake ndi nyimbo zachimwemwe.
23Ena anayenda pa nyanja mʼsitima zapamadzi;
Iwo anali anthu amalonda pa nyanja yayikulu.
24Anaona ntchito za Yehova,
machitidwe ake odabwitsa mʼnyanja yakuya.
25Pakuti Iye anayankhula ndi kuwutsa mphepo yamkuntho
imene inabweretsa mafunde ataliatali.
26Sitima za pamadzizo zinatukulidwa mmwamba ndi kutsikira pansi pakuya;
pamene amawonongeka, kulimba mtima kwawo kunasungunuka.
27Anachita chizungulire ndi kudzandira ngati anthu oledzera;
anali pa mapeto a moyo wawo.
28Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo
ndipo Iyeyo anawapulumutsa ku masautso awo.
29Yehova analetsa namondwe,
mafunde a mʼnyanja anatontholetsedwa.
30Anali osangalala pamene kunakhala bata,
ndipo Iye anawatsogolera ku dooko limene amalifuna.
31Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha
ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu.
32Akuze Iye mu msonkhano wa anthu
ndi kumutamanda pabwalo la akuluakulu.
33Iye anasandutsa mitsinje kukhala chipululu,
akasupe otuluka madzi kukhala nthaka yowuma,
34ndiponso nthaka yachonde kukhala nthaka yamchere,
chifukwa cha kuyipa kwa amene amakhala kumeneko.
35Anasandutsa chipululu kukhala mayiwe a madzi
ndi nthaka yowuma kukhala akasupe a madzi oyenda;
36kumeneko Iye anabweretsa anthu anjala kuti azikhalako,
ndipo iwo anamanga mzinda woti akhazikikeko.
37Anafesa mbewu mʼminda ndi kudzala mipesa
ndipo anakolola zipatso zochuluka;
38Yehova anawadalitsa, ndipo chiwerengero chawo chinachuluka kwambiri,
ndipo Iye sanalole kuti ziweto zawo zithe.
39Kenaka chiwerengero chawo chinachepa ndipo iwo anatsitsidwa
chifukwa cha mazunzo, mavuto ndi chisoni;
40Iye amene amakhuthulira mʼnyozo pa olemekezeka
anawachititsa kuyendayenda mʼmalo owumawo wopanda njira.
41Koma Iyeyo anakweza anthu osowa kuchoka ku masautso awo
ngati magulu a nkhosa.
42Anthu olungama mtima amaona ndi kusangalala,
koma anthu onse oyipa amatseka pakamwa pawo.
43Aliyense wanzeru asamalitse zinthu zimenezi
ndi kuganizira za chikondi chachikulu cha Yehova.
Quinto Livro
(Salmos 107–150)
Salmo 107
1Deem graças ao Senhor porque ele é bom,
porque o seu amor é eterno!
2Que aqueles a quem o Senhor salvou
contem como Deus os salvou dos seus inimigos!
3Como tornou trazê-los dos quatro cantos da Terra,
do oriente e do ocidente, do norte e das zonas do mar.
4Andaram desgarrados pelo deserto, isolados,
sem um lar onde pudessem descansar.
5Andaram famintos, sedentos, desfalecendo.
6Mas clamaram ao Senhor, na sua tribulação,
e ele os livrou das suas angústias.
7Levou-os, por fim, com segurança,
a um lugar seguro onde habitaram.
8Louvem o Senhor pela sua bondade
e pelas suas maravilhas para com os homens!
9Porque satisfez plenamente a alma que tinha sede,
encheu de bens a alma que tinha fome.
10Quem são esses que estão sentados nas trevas,
nas sombras da morte, prisioneiros da miséria,
pela opressão e pela escravidão?
11Pois rebelaram-se contra as palavras de Deus
e desprezaram os decretos do Altíssimo.
12Foi por isso que ele os abateu com dificuldades;
caíram e ninguém houve que pudesse ajudá-los
a erguerem-se de novo.
13Mas clamaram ao Senhor, na sua tribulação,
e ele os livrou das suas angústias.
14Tirou-os daquelas trevas em que estavam,
daquelas sombras da morte,
e quebrou as cadeias que os amarravam.
15Louvem o Senhor pela sua bondade
e pelas suas maravilhas para com os homens!
16Derrubou os pesados portões de bronze
e despedaçou as barras de ferro das suas prisões;
fez em pedaços as correntes que os amarravam.
17Outros houve que foram afligidos
por causa das suas muitas transgressões,
da loucura que os levou por caminhos de maldade.
18À força de tanto sofrerem, chegaram a definhar;
nem sequer a comida lhes apetecia,
ficando às portas da morte.
19Então clamaram ao Senhor, na sua tribulação,
e ele os livrou das suas angústias.
20Lembrou-lhes a sua palavra,
e as suas fraquezas foram saradas;
livrou-os da destruição.
21Louvem o Senhor pela sua bondade,
e pelas suas maravilhas para com os homens!
22Ofereçam alegres sacrifícios de ação de graças,
e anunciem a toda a gente as suas maravilhosas obras.
23E há ainda os navegantes, os marinheiros,
que atravessam de lés a lés todos esses mares,
cruzando as rotas do mundo;
24Também esses, lá no mar alto,
podem ver obras maravilhosas que o Senhor fez.
25À sua ordem, podem levantar-se ventos tempestuosos
que fazem erguer vagas imensas.
26Pesados navios elevam-se nas suas cristas
e são mergulhados novamente no profundo abismo.
27A própria gente do mar encolhe-se de terror,
cambaleando, vacilando como bêbedos,
perdendo mesmo o controlo de si mesmos.
28Mas clamaram ao Senhor na sua tribulação,
e ele livrou-os das suas angústias.
29Ele faz acabar a tormenta, acalma as vagas.
30A alegria volta de novo com essa bonança;
Deus leva-os até ao porto desejado.
31Louvem o Senhor pela sua bondade
e pelas suas maravilhas para com os homens!
32Como deveriam dar toda a honra a Deus,
publicamente, e perante os anciãos conselheiros!
33Deus seca os rios e transforma-os em desertos.
34Transforma a boa terra num deserto de sal,
por causa da maldade dos que nela habitam.
35Por outro lado, converte os desertos
em terra fértil, cheia de água.
36Ele traz gente faminta para ali habitar
e construir as suas cidades.
37Semeiam os campos e plantam vinhas;
comem de tudo o que a terra produzir.
38É assim que Deus os abençoa
e os ajuda a constituírem grandes famílias,
fazendo multiplicar o seu gado.
39Vemos também que há outros que ficam pobres;
em vez de progredirem, definham,
abatidos pela opressão, aflição e tristeza.
40Deus lança desprezo sobre os orgulhosos;
faz com que governantes acabem por vaguear
entre as ruínas daquilo que possuíram.
41Contudo, aos desfavorecidos Deus os salva da opressão;
no seu abrigo seguro, faz as famílias a multiplicarem-se.
42Estas coisas alegram as pessoas que são retas,
enquanto os maus ficam mudos, sem palavras.
43A sabedoria consiste em prestar atenção a estas coisas,
em refletir sobre a grande bondade do Senhor!