Masalimo 107 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 107:1-43

BUKU LACHISANU

Masalimo 107–150

Salimo 107

1Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino;

pakuti chikondi chake ndi chosatha.

2Owomboledwa a Yehova anene zimenezi

amene Iyeyo anawawombola mʼdzanja la mdani,

3iwo amene anawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko,

kuchokera kumadzulo ndi kummawa, kuchokera kumpoto ndi kummwera.

4Ena anayendayenda mʼchipululu mopanda kanthu,

osapeza njira yopitira ku mzinda kumene akanakakhazikikako.

5Iwo anamva njala ndi ludzu,

ndipo miyoyo yawo inafowokeratu.

6Pamenepo analirira Yehova mʼmavuto awo

ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.

7Iye anawatsogolera mʼnjira yowongoka

kupita ku mzinda umene anakakhazikikako.

8Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha

ndi chifukwa cha machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,

9pakuti Iye wapha ludzu la munthu womva ludzu

ndipo wakhutitsa wanjala ndi zinthu zabwino.

10Ena anakhala mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu,

amʼndende ovutika mʼmaunyolo achitsulo,

11pakuti iwowo anawukira mawu a Mulungu

ndi kunyoza uphungu wa Wammwambamwamba.

12Kotero Iye anawapereka kuti agwire ntchito yakalavulagaga;

anagwa pansi ndipo panalibe woti awathandize.

13Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo

ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.

14Yehova anawatulutsa mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu

ndipo anadula maunyolo awo.

15Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha

ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,

16pakuti Iye amathyola zipata zamkuwa

ndi kudula pakati mipiringidzo yachitsulo.

17Ena anakhala zitsiru chifukwa cha njira zawo zowukira,

ndipo anamva zowawa chifukwa cha mphulupulu zawo.

18Iwo ananyansidwa ndi chakudya chilichonse

ndipo anafika pafupi ndi zipata za imfa.

19Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo

ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awowo.

20Iye anatumiza mawu ake ndi kuwachiritsa;

anawalanditsa ku manda.

21Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha

ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu.

22Apereke nsembe yachiyamiko

ndi kufotokoza za ntchito zake ndi nyimbo zachimwemwe.

23Ena anayenda pa nyanja mʼsitima zapamadzi;

Iwo anali anthu amalonda pa nyanja yayikulu.

24Anaona ntchito za Yehova,

machitidwe ake odabwitsa mʼnyanja yakuya.

25Pakuti Iye anayankhula ndi kuwutsa mphepo yamkuntho

imene inabweretsa mafunde ataliatali.

26Sitima za pamadzizo zinatukulidwa mmwamba ndi kutsikira pansi pakuya;

pamene amawonongeka, kulimba mtima kwawo kunasungunuka.

27Anachita chizungulire ndi kudzandira ngati anthu oledzera;

anali pa mapeto a moyo wawo.

28Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo

ndipo Iyeyo anawapulumutsa ku masautso awo.

29Yehova analetsa namondwe,

mafunde a mʼnyanja anatontholetsedwa.

30Anali osangalala pamene kunakhala bata,

ndipo Iye anawatsogolera ku dooko limene amalifuna.

31Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha

ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu.

32Akuze Iye mu msonkhano wa anthu

ndi kumutamanda pabwalo la akuluakulu.

33Iye anasandutsa mitsinje kukhala chipululu,

akasupe otuluka madzi kukhala nthaka yowuma,

34ndiponso nthaka yachonde kukhala nthaka yamchere,

chifukwa cha kuyipa kwa amene amakhala kumeneko.

35Anasandutsa chipululu kukhala mayiwe a madzi

ndi nthaka yowuma kukhala akasupe a madzi oyenda;

36kumeneko Iye anabweretsa anthu anjala kuti azikhalako,

ndipo iwo anamanga mzinda woti akhazikikeko.

37Anafesa mbewu mʼminda ndi kudzala mipesa

ndipo anakolola zipatso zochuluka;

38Yehova anawadalitsa, ndipo chiwerengero chawo chinachuluka kwambiri,

ndipo Iye sanalole kuti ziweto zawo zithe.

39Kenaka chiwerengero chawo chinachepa ndipo iwo anatsitsidwa

chifukwa cha mazunzo, mavuto ndi chisoni;

40Iye amene amakhuthulira mʼnyozo pa olemekezeka

anawachititsa kuyendayenda mʼmalo owumawo wopanda njira.

41Koma Iyeyo anakweza anthu osowa kuchoka ku masautso awo

ngati magulu a nkhosa.

42Anthu olungama mtima amaona ndi kusangalala,

koma anthu onse oyipa amatseka pakamwa pawo.

43Aliyense wanzeru asamalitse zinthu zimenezi

ndi kuganizira za chikondi chachikulu cha Yehova.

Hoffnung für Alle

Psalm 107:1-43

Fünftes Buch

(Psalm 107–150)

Herr, du hast uns gerettet!

1Dankt dem Herrn, denn er ist gut,

und seine Gnade hört niemals auf!

2Dies sollen alle bekennen, die der Herr erlöst hat.

Ja, er hat sie aus der Gewalt ihrer Unterdrücker befreit

3und aus fernen Ländern wieder zurückgebracht –

aus Ost und West, aus Nord und Süd.

4Manche irrten in der trostlosen Wüste umher

und konnten keinen bewohnten Ort finden.

5Hunger und Durst raubten ihnen alle Kraft,

sie waren der Verzweiflung nahe.

6In auswegloser Lage schrien sie zum Herrn,

und er rettete sie aus ihrer Not.

7Er half ihnen, den richtigen Weg zu finden,

und führte sie zu einer bewohnten Stadt.

8Sie sollen den Herrn preisen für seine Gnade

und für seine Wunder, die er uns Menschen erleben lässt!

9Denn er hat den Verdurstenden zu trinken gegeben,

die Hungernden versorgte er mit reichlich Nahrung.

10Andere lagen in der Finsternis gefangen

und litten unter ihren schweren Fesseln.

11Sie hatten missachtet, was Gott ihnen sagte,

und die Weisungen des Höchsten in den Wind geschlagen.

12Darum zerbrach er ihren Stolz durch Mühsal und Leid;

sie lagen am Boden, und keiner half ihnen auf.

13In auswegloser Lage schrien sie zum Herrn,

und er rettete sie aus ihrer Not.

14Er holte sie aus den finsteren Kerkern heraus

und riss ihre Fesseln entzwei.

15Sie sollen den Herrn preisen für seine Gnade

und für seine Wunder, die er uns Menschen erleben lässt!

16Denn er hat die gepanzerten Türen zerschmettert

und die eisernen Riegel aufgebrochen.

17Andere hatten leichtfertig gesündigt;

wegen ihrer Verfehlungen siechten sie nun dahin.

18Zuletzt ekelten sie sich vor jeder Speise

und standen schon an der Schwelle des Todes.

19In auswegloser Lage schrien sie zum Herrn,

und er rettete sie aus ihrer Not.

20Er sprach nur ein Wort, und sie wurden gesund.

So bewahrte er sie vor dem sicheren Tod.

21Sie sollen den Herrn preisen für seine Gnade

und für seine Wunder, die er uns Menschen erleben lässt!

22Aus Dank sollen sie ihm Opfergaben bringen

und voll Freude von seinen Taten erzählen!

23Wieder andere segelten aufs Meer hinaus,

um mit ihren Schiffen Handel zu treiben.

24Dort erlebten sie die Macht des Herrn,

auf hoher See wurden sie Zeugen seiner Wunder.

25Nur ein Wort von ihm – und ein Sturm peitschte das Meer.

Wogen türmten sich auf,

26warfen die Schiffe hoch in die Luft

und stießen sie sogleich wieder in die Tiefe.

Da verloren die Seeleute jede Hoffnung.

27Sie wankten und taumelten wie Betrunkene,

mit ihrer Weisheit waren sie am Ende.

28In auswegloser Lage schrien sie zum Herrn,

und er rettete sie aus ihrer Not.

29Er bannte die tödliche Gefahr:

Der Sturm legte sich, und die Wellen wurden ruhig.

30Da jubelten sie, dass endlich Stille herrschte!

Gott brachte sie in den sicheren Hafen, an das ersehnte Ziel.

31Sie sollen den Herrn preisen für seine Gnade

und für seine Wunder, die er uns Menschen erleben lässt!

32Vor der ganzen Gemeinde sollen sie ihn rühmen

und ihn loben vor dem Rat der führenden Männer.

33Gott verwandelt wasserreiches Land in dürre Wüste,

und wo vorher Quellen sprudelten, entstehen trostlose Steppen.

34Fruchtbare Gebiete lässt er zur Salzwüste veröden,

wenn die Bosheit der Bewohner dort überhandnimmt.

35Doch er verwandelt auch dürres Land in eine Oase

und lässt mitten in der Steppe Quellen aufbrechen.

36Hungernde Menschen siedeln sich dort an

und gründen Städte, um darin zu wohnen.

37Sie bestellen die Felder, legen Weinberge an

und bringen Jahr für Jahr eine reiche Ernte ein.

38Gott segnet sie mit vielen Kindern

und vergrößert ihre Viehherden immer mehr.

39Doch wenn sie immer weniger werden,

wenn sie gebeugt sind von Unglück und Leid,

40dann macht Gott ihre Unterdrücker zum Gespött

und lässt sie in der Wüste umherirren.

41Die Hilflosen aber rettet er aus ihrem Elend

und lässt ihre Familien wachsen wie große Herden.

42Die aufrichtigen Menschen sehen es voll Freude,

und alle niederträchtigen müssen verstummen.

43Wer verständig ist, der soll immer wieder daran denken

und erkennen, auf welch vielfache Weise der Herr seine Gnade zeigt!