Masalimo 107 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 107:1-43

BUKU LACHISANU

Masalimo 107–150

Salimo 107

1Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino;

pakuti chikondi chake ndi chosatha.

2Owomboledwa a Yehova anene zimenezi

amene Iyeyo anawawombola mʼdzanja la mdani,

3iwo amene anawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko,

kuchokera kumadzulo ndi kummawa, kuchokera kumpoto ndi kummwera.

4Ena anayendayenda mʼchipululu mopanda kanthu,

osapeza njira yopitira ku mzinda kumene akanakakhazikikako.

5Iwo anamva njala ndi ludzu,

ndipo miyoyo yawo inafowokeratu.

6Pamenepo analirira Yehova mʼmavuto awo

ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.

7Iye anawatsogolera mʼnjira yowongoka

kupita ku mzinda umene anakakhazikikako.

8Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha

ndi chifukwa cha machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,

9pakuti Iye wapha ludzu la munthu womva ludzu

ndipo wakhutitsa wanjala ndi zinthu zabwino.

10Ena anakhala mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu,

amʼndende ovutika mʼmaunyolo achitsulo,

11pakuti iwowo anawukira mawu a Mulungu

ndi kunyoza uphungu wa Wammwambamwamba.

12Kotero Iye anawapereka kuti agwire ntchito yakalavulagaga;

anagwa pansi ndipo panalibe woti awathandize.

13Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo

ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.

14Yehova anawatulutsa mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu

ndipo anadula maunyolo awo.

15Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha

ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,

16pakuti Iye amathyola zipata zamkuwa

ndi kudula pakati mipiringidzo yachitsulo.

17Ena anakhala zitsiru chifukwa cha njira zawo zowukira,

ndipo anamva zowawa chifukwa cha mphulupulu zawo.

18Iwo ananyansidwa ndi chakudya chilichonse

ndipo anafika pafupi ndi zipata za imfa.

19Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo

ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awowo.

20Iye anatumiza mawu ake ndi kuwachiritsa;

anawalanditsa ku manda.

21Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha

ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu.

22Apereke nsembe yachiyamiko

ndi kufotokoza za ntchito zake ndi nyimbo zachimwemwe.

23Ena anayenda pa nyanja mʼsitima zapamadzi;

Iwo anali anthu amalonda pa nyanja yayikulu.

24Anaona ntchito za Yehova,

machitidwe ake odabwitsa mʼnyanja yakuya.

25Pakuti Iye anayankhula ndi kuwutsa mphepo yamkuntho

imene inabweretsa mafunde ataliatali.

26Sitima za pamadzizo zinatukulidwa mmwamba ndi kutsikira pansi pakuya;

pamene amawonongeka, kulimba mtima kwawo kunasungunuka.

27Anachita chizungulire ndi kudzandira ngati anthu oledzera;

anali pa mapeto a moyo wawo.

28Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo

ndipo Iyeyo anawapulumutsa ku masautso awo.

29Yehova analetsa namondwe,

mafunde a mʼnyanja anatontholetsedwa.

30Anali osangalala pamene kunakhala bata,

ndipo Iye anawatsogolera ku dooko limene amalifuna.

31Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha

ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu.

32Akuze Iye mu msonkhano wa anthu

ndi kumutamanda pabwalo la akuluakulu.

33Iye anasandutsa mitsinje kukhala chipululu,

akasupe otuluka madzi kukhala nthaka yowuma,

34ndiponso nthaka yachonde kukhala nthaka yamchere,

chifukwa cha kuyipa kwa amene amakhala kumeneko.

35Anasandutsa chipululu kukhala mayiwe a madzi

ndi nthaka yowuma kukhala akasupe a madzi oyenda;

36kumeneko Iye anabweretsa anthu anjala kuti azikhalako,

ndipo iwo anamanga mzinda woti akhazikikeko.

37Anafesa mbewu mʼminda ndi kudzala mipesa

ndipo anakolola zipatso zochuluka;

38Yehova anawadalitsa, ndipo chiwerengero chawo chinachuluka kwambiri,

ndipo Iye sanalole kuti ziweto zawo zithe.

39Kenaka chiwerengero chawo chinachepa ndipo iwo anatsitsidwa

chifukwa cha mazunzo, mavuto ndi chisoni;

40Iye amene amakhuthulira mʼnyozo pa olemekezeka

anawachititsa kuyendayenda mʼmalo owumawo wopanda njira.

41Koma Iyeyo anakweza anthu osowa kuchoka ku masautso awo

ngati magulu a nkhosa.

42Anthu olungama mtima amaona ndi kusangalala,

koma anthu onse oyipa amatseka pakamwa pawo.

43Aliyense wanzeru asamalitse zinthu zimenezi

ndi kuganizira za chikondi chachikulu cha Yehova.

La Bible du Semeur

Psaumes 107:1-43

Cinquième livre

Cantique des rachetés

1Célébrez l’Eternel, car il est bon,

car son amour ╵dure à toujours107.1 Voir 100.5 ; 106.1 ; 118.1, 29 ; 136 ; 1 Ch 16.34 ; 2 Ch 5.13 ; 7.3 ; Esd 3.11 ; Jr 33.11..

2Qu’ils le proclament, ╵tous ceux que l’Eternel a délivrés,

qu’il a sauvés des mains de l’oppresseur,

3et qu’il a rassemblés de tous pays :

de l’est, de l’ouest, du nord et du midi107.3 D’après la version syriaque. Texte hébreu traditionnel : la mer..

4Les uns erraient dans le désert ╵où il n’y a personne,

sans trouver le chemin ╵d’une ville habitée.

5Ils étaient affamés, ils avaient soif,

et ils étaient tout près de défaillir.

6Dans leur détresse, ╵ils crièrent à l’Eternel,

et il les délivra de leurs angoisses.

7Il les mena par un chemin tout droit

et les dirigea vers une ville habitable.

8Qu’ils louent donc l’Eternel ╵pour son amour,

pour ses merveilles ╵en faveur des humains !

9Il a désaltéré les assoiffés,

il a comblé de biens les affamés.

10D’autres se trouvaient dans des lieux, ╵où régnaient d’épaisses ténèbres ╵et l’obscurité la plus noire,

enchaînés dans la misère et les fers

11pour avoir bravé les commandements de Dieu

et méprisé les desseins du Très-Haut.

12Il les humilia ╵en les astreignant à un dur labeur :

ils succombaient, privés de tout secours.

13Dans leur détresse, ╵ils crièrent à l’Eternel,

et il les délivra de leurs angoisses.

14Il les fit sortir des lieux sombres ╵et ténébreux,

il rompit les liens qui les retenaient.

15Qu’ils louent donc l’Eternel pour son amour,

pour ses merveilles ╵en faveur des humains !

16Car il a brisé les portes de bronze

et il a rompu les verrous de fer.

17Des insensés, vivant dans le péché,

s’étaient rendus malheureux par leurs fautes.

18Tout aliment répugnait à leur bouche,

ils approchaient des portes de la mort.

19Dans leur détresse, ╵ils crièrent à l’Eternel,

et il les délivra de leurs angoisses.

20Il dit un mot et les guérit,

et il les fit échapper à la tombe.

21Qu’ils louent donc l’Eternel pour son amour,

pour ses merveilles ╵en faveur des humains !

22Et qu’ils lui offrent ╵des sacrifices de reconnaissance ;

qu’avec des cris de joie, ╵ils racontent ses œuvres.

23D’autres s’étaient embarqués sur la mer, ╵dans des bateaux

et ils vaquaient à leurs occupations ╵sur de profondes eaux.

24Ceux-là ont vu les œuvres ╵de l’Eternel,

et ses prodiges sur la haute mer.

25A sa parole, ╵il fit lever un vent impétueux

qui souleva les flots.

26Tantôt ils étaient portés jusqu’au ciel,

tantôt ils retombaient dans les abîmes,

et ainsi mis à mal, ils défaillaient.

27Pris de vertige, ils titubaient comme ivres,

et tout leur savoir-faire ╵s’était évanoui.

28Dans leur détresse, ╵ils crièrent à l’Eternel,

et il les délivra de leurs angoisses.

29Il calma la tempête,

et fit taire les flots ╵qui s’étaient soulevés contre eux.

30Ce calme fut pour eux cause de joie

et Dieu les guida au port désiré.

31Qu’ils louent donc l’Eternel pour son amour,

pour ses merveilles ╵en faveur des humains !

32Qu’ils disent sa grandeur ╵dans l’assemblée du peuple,

et qu’ils le louent ╵au conseil des autorités107.32 L’assemblée du peuple pour le culte et le conseil des responsables réunis aux portes de la ville où se traitaient les affaires publiques étaient les lieux où celui qui avait été délivré pouvait rendre témoignage à Dieu..

33Il peut faire tarir les fleuves ╵et les transformer en désert,

ou changer les sources d’eau en lieux secs ;

34d’un sol fertile, il fait une saline107.34 Le sel rend le sol stérile (Gn 13.10 ; 14.3 ; 19.24-26 ; Dt 29.22).

quand ses habitants pratiquent le mal.

35Mais il change aussi le désert en lac

et la terre aride en sources d’eau vive,

36et il y établit ╵ceux qui ont faim,

pour qu’ils y fondent ╵une ville habitable,

37qu’ils ensemencent des champs et plantent des vignes

qui porteront des fruits en abondance.

38Il les bénit en sorte qu’ils se multiplient,

et il ne laisse pas ╵décroître leur bétail.

39D’autres sont réduits à un petit nombre, ╵écrasés sous le poids

de l’oppression, ╵du malheur et de la souffrance.

40Dieu répand le mépris sur les puissants,

les fait errer dans un désert sans route.

41Mais il délivre le pauvre de la détresse

et rend les familles fécondes ╵comme le petit bétail.

42Les hommes droits le voient et ils s’en réjouissent,

mais toute méchanceté a la bouche close.

43Que celui qui est sage ╵prête attention à tout cela,

et qu’il médite sur l’amour ╵de l’Eternel.