Masalimo 106 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 106:1-48

Salimo 106

1Tamandani Yehova.

Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino;

pakuti chikondi chake ndi chosatha.

2Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova

kapena kumutamanda mokwanira?

3Odala ndi amene amasunga chilungamo,

amene amachita zolungama nthawi zonse.

4Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu,

bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo,

5kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika,

kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu

ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani.

6Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu;

tachita zolakwa ndipo tachita moyipa.

7Pamene makolo athu anali mu Igupto,

sanalingalire za zozizwitsa zanu;

iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka,

ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira.

8Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake,

kuti aonetse mphamvu zake zazikulu.

9Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma;

anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu.

10Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo;

anawawombola mʼdzanja la mdani.

11Madzi anamiza adani awo,

palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.

12Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake

ndi kuyimba nyimbo zamatamando.

13Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita,

ndipo sanayembekezere uphungu wake.

14Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo;

mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu.

15Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha,

koma anatumiza nthenda yowondetsa.

16Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni,

amene Yehova anadzipatulira.

17Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani;

inakwirira gulu la Abiramu.

18Moto unayaka pakati pa otsatira awo;

lawi lamoto linapsereza anthu oyipa.

19Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu

ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo.

20Anasinthanitsa ulemerero wawo

ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu.

21Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa,

amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto,

22zozizwitsa mʼdziko la Hamu

ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira.

23Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga,

pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa,

kuyima pamaso pake,

ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge.

24Motero iwo ananyoza dziko lokoma;

sanakhulupirire malonjezo ake.

25Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo

ndipo sanamvere Yehova.

26Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake,

kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu,

27kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina

ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse.

28Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori

ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo;

29anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa,

ndipo mliri unabuka pakati pawo.

30Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo,

ndipo mliri unaleka.

31Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake,

kwa mibado yosatha imene ikubwera.

32Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova

ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo,

33pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu,

ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera.

34Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu

monga momwe Yehova anawalamulira.

35Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo

ndi kuphunzira miyambo yawo.

36Ndipo anapembedza mafano awo,

amene anakhala msampha kwa iwowo.

37Anapereka nsembe ana awo aamuna

ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.

38Anakhetsa magazi a anthu osalakwa,

magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi,

amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani,

ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo.

39Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita;

ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo.

40Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake

ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.

41Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina,

ndipo adani awo anawalamulira.

42Adani awo anawazunza

ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.

43Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri,

koma iwo ankatsimikiza za kuwukira

ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.

44Koma Iye anaona kuzunzika kwawo

pamene anamva kulira kwawo;

45Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake

ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.

46Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo

awamvere chisoni.

47Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu,

ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina

kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera

ndi kunyadira mʼmatamando anu.

48Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli,

Kuyambira muyaya mpaka muyaya.

Anthu onse anene kuti, “Ameni!”

Tamandani Yehova.

Nueva Versión Internacional

Salmo 106:1-48

Salmo 106

106:1,47-481Cr 16:34-36

1¡Aleluya!

Den gracias al Señor porque él es bueno;

su gran amor perdura para siempre.

2¿Quién puede proclamar las proezas del Señor

o expresar toda su alabanza?

3Dichosos los que practican la justicia

y hacen siempre lo que es justo.

4Acuérdate de mí, Señor, cuando muestres tu bondad a tu pueblo;

ven en mi ayuda el día de tu salvación,

5para que yo pueda disfrutar del bienestar de tus escogidos,

participar de la alegría de tu pueblo

y expresar mis alabanzas con tu heredad.

6Hemos pecado, lo mismo que nuestros antepasados;

hemos hecho lo malo y actuado con iniquidad.

7Cuando nuestros antepasados estaban en Egipto,

no tomaron en cuenta tus maravillas,

no recordaron la inmensidad de tu gran amor

y se rebelaron junto al mar, el mar Rojo.106:7 Lit. mar de las Cañas. Término con el que se designa en la Biblia al mar Rojo en su parte septentrional; también en vv. 9 y 22.

8Pero Dios los salvó, haciendo honor a su nombre,

para mostrar su gran poder.

9Reprendió al mar Rojo y este quedó seco;

los condujo por las profundidades del mar como si cruzaran el desierto.

10Los salvó del poder de quienes los odiaban;

los rescató del poder de sus enemigos.

11Las aguas envolvieron a sus adversarios

y ninguno de estos quedó con vida.

12Entonces ellos creyeron en sus promesas

y le entonaron alabanzas.

13Pero muy pronto olvidaron sus acciones

y no esperaron a conocer sus planes.

14En el desierto cedieron a sus propios deseos;

en los páramos pusieron a prueba a Dios.

15Y él les dio lo que pidieron,

pero les envió una enfermedad devastadora.

16En el campamento tuvieron envidia de Moisés

y de Aarón, el que estaba consagrado al Señor.

17Se abrió la tierra y se tragó a Datán;

sepultó a los seguidores de Abirán.

18Un fuego devoró a ese grupo;

las llamas consumieron a los malvados.

19En Horeb hicieron un becerro;

se postraron ante un ídolo de fundición.

20Cambiaron a quien era su gloria

por la imagen de un toro que come hierba.

21Se olvidaron del Dios que los salvó

y que había hecho grandes cosas en Egipto:

22milagros en la tierra de Cam

y maravillas asombrosas junto al mar Rojo.

23Dios amenazó con destruirlos,

pero no lo hizo por Moisés, su escogido,

quien se puso ante él en la brecha

e impidió que su ira los destruyera.

24Despreciaron una tierra apetecible;

no creyeron en la promesa de Dios.

25Murmuraron en sus tiendas de campaña

y no obedecieron al Señor.

26Por tanto, él juró solemnemente con su mano en alto contra ellos

para hacerlos caer en el desierto,

27para hacer caer a sus descendientes entre las naciones

y dispersarlos entre los países.

28Se sometieron al yugo de Baal Peor

y comieron sacrificios a los muertos.

29Provocaron la ira del Señor con sus malvadas acciones

y les sobrevino una plaga.

30Pero Finés se levantó e intervino,

y la plaga se detuvo.

31Esto se le acreditó como un acto de justicia

para siempre, por todas las generaciones.

32Junto a las aguas de Meribá hicieron enojar al Señor.

Y a Moisés le fue mal por culpa de ellos,

33porque se rebelaron contra el Espíritu de Dios106:33 contra … de Dios. Alt. contra su espíritu.

y Moisés habló sin pensar lo que decía.

34No destruyeron a los pueblos

que el Señor les había señalado,

35sino que se mezclaron con los paganos

y adoptaron sus costumbres.

36Rindieron culto a sus ídolos

que fueron una trampa para ellos.

37Ofrecieron a sus hijos y a sus hijas

como sacrificio a esos demonios.

38Derramaron sangre inocente,

la sangre de sus hijos y sus hijas.

Al ofrecerlos en sacrificio a los ídolos de Canaán,

su sangre derramada contaminó la tierra.

39Se hicieron impuros por esos hechos;

se prostituyeron con sus acciones.

40La ira del Señor se encendió contra su pueblo;

su heredad le resultó aborrecible.

41Por eso los entregó a los paganos

y fueron dominados por quienes los odiaban.

42Sus enemigos los oprimieron,

los sometieron a su poder.

43Muchas veces Dios los libró;

pero ellos se obstinaron en su rebeldía

y se hundieron en su iniquidad.

44Al verlos angustiados

y escuchar su clamor,

45Dios se acordó del pacto que había hecho con ellos

y por su gran amor les tuvo compasión.

46Hizo que todos sus opresores

también se apiadaran de ellos.

47¡Sálvanos, Señor, Dios nuestro!

Vuelve a reunirnos de entre las naciones,

para que demos gracias a tu santo nombre

y alabarte sea nuestra gloria.

48¡Bendito sea el Señor, el Dios de Israel,

eternamente y para siempre!

Que todo el pueblo diga: «¡Amén!».

¡Aleluya!