Masalimo 105 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 105:1-45

Salimo 105

1Yamikani Yehova, itanani dzina lake;

lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.

2Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo;

fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.

3Munyadire dzina lake loyera;

mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.

4Dalirani Yehova ndi mphamvu zake;

funafunani nkhope yake nthawi yonse.

5Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita,

zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,

6inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake,

inu ana a Yakobo, osankhika ake.

7Iye ndiye Yehova Mulungu wathu;

maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.

8Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya,

mawu amene analamula kwa mibado yonse,

9pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu,

lumbiro limene analumbira kwa Isake.

10Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa,

kwa Israeli monga pangano lamuyaya:

11“Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani

ngati gawo la cholowa chako.”

12Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero,

ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,

13ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina,

kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.

14Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza;

anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:

15“Musakhudze odzozedwa anga;

musachitire choyipa aneneri anga.”

16Iye anabweretsa njala pa dziko

ndipo anawononga chakudya chonse;

17Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo,

Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.

18Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza,

khosi lake analiyika mʼzitsulo,

19mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa,

mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.

20Mfumu inatuma munthu kukamumasula,

wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.

21Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake,

wolamulira zonse zimene iye anali nazo,

22kulangiza ana a mfumu monga ankafunira

ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.

23Tsono Israeli analowa mu Igupto;

Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.

24Yehova anachulukitsa anthu ake;

ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;

25amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake,

kukonzera chiwembu atumiki ake.

26Yehova anatuma Mose mtumiki wake,

ndi Aaroni amene Iye anamusankha.

27Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo,

zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.

28Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima.

Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.

29Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi,

kuchititsa kuti nsomba zawo zife.

30Dziko lawo linadzaza ndi achule

amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.

31Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka

ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.

32Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala,

ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;

33Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu,

nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.

34Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera,

ziwala zosawerengeka;

35zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo,

zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.

36Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo,

zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.

37Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri,

ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.

38Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka,

pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.

39Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo,

ndi moto owawunikira usiku.

40Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri

ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.

41Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka;

ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.

42Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene

linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.

43Iye anatulutsa anthu ake akukondwera,

osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;

44Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina

ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,

45kuti iwo asunge malangizo ake

ndi kutsatira malamulo ake.

Tamandani Yehova.

Nueva Versión Internacional

Salmo 105:1-45

Salmo 105

105:1-151Cr 16:8-22

1Den gracias al Señor; proclamen su nombre.

¡Den a conocer sus obras entre las naciones!

2¡Cántenle, entónenle salmos!

¡Hablen de todas sus maravillas!

3¡Gloríense en su santo nombre!

¡Alégrese el corazón de los que buscan al Señor!

4¡Busquen al Señor y su fuerza;

anhelen siempre su rostro!

5¡Recuerden las maravillas que ha hecho,

las señales y las leyes que ha emitido!

6¡Ustedes, descendientes de Abraham, su siervo!

¡Ustedes, hijos de Jacob, elegidos suyos!

7Él es el Señor nuestro Dios;

en toda la tierra están sus leyes.

8Se acordó siempre de su pacto,

la palabra que ordenó para mil generaciones;

9del pacto que hizo con Abraham

y del juramento que hizo a Isaac.

10Se lo confirmó a Jacob como un estatuto,

a Israel como un pacto eterno,

11cuando dijo: «Te daré la tierra de Canaán

como la herencia que te corresponde».

12Aun cuando eran pocos en número,

unos cuantos extranjeros en la tierra,

13que andaban siempre de nación en nación

y de reino en reino,

14a nadie permitió que los oprimiera,

sino que por causa de ellos reprendió a los reyes:

15«¡No toquen a mis ungidos!

¡No maltraten a mis profetas!».

16Dios provocó hambre en la tierra

al hacer escasear el alimento.105:16 escasear el alimento. Lit. todo bastón de pan.

17Pero envió delante de ellos a un hombre:

a José, vendido como esclavo.

18Le sujetaron los pies con grilletes,

entre hierros aprisionaron su cuello,

19hasta que se cumplió lo que él predijo

y la palabra del Señor probó que él era veraz.

20El rey ordenó ponerlo en libertad;

el gobernante de los pueblos lo dejó libre.

21Lo nombró señor sobre su casa

y administrador de todas sus posesiones,

22con pleno poder para instruir105:22 instruir (LXX, Siríaca y Vulgata); atar (TM). a sus príncipes

e impartir sabiduría a sus jefes.

23Entonces Israel vino a Egipto;

Jacob fue extranjero en el país de Cam.

24El Señor hizo que su pueblo se multiplicara;

lo hizo más poderoso que sus adversarios,

25a quienes les cambió su sentir para que odiaran a su pueblo

y se confabularan contra sus siervos.

26Envió a su siervo Moisés,

y a Aarón, a quien había escogido,

27y estos hicieron señales milagrosas entre ellos,

maravillas en el país de Cam.

28Envió tinieblas y la tierra se oscureció,

pero ellos se rebelaron105:28 se rebelaron (LXX y Siríaca); no se rebelaron (TM). contra sus palabras.

29Convirtió en sangre sus aguas

y causó la muerte de sus peces.

30Todo Egipto105:30 Todo Egipto. Lit. La tierra de ellos. se infestó de ranas,

hasta las habitaciones de sus reyes.

31Habló Dios e invadieron todo el país

enjambres de tábanos y mosquitos.

32Convirtió la lluvia en granizo

y lanzó rayos sobre su tierra;

33derribó sus vides y sus higueras,

y destrozó los árboles de su territorio.

34Dio una orden y llegaron las langostas

y una infinidad de saltamontes.

35Arrasaron con toda la vegetación del país,

devoraron los frutos de sus campos.

36Hirió de muerte a todos los primogénitos del país,

las primicias de su virilidad.

37Sacó a los israelitas cargados de plata y oro

y no hubo entre sus tribus nadie que tropezara.

38Los egipcios se alegraron de su partida,

pues el miedo a los israelitas los dominaba.

39Él los cubrió con una nube

y con fuego los alumbró de noche.

40Pidió el pueblo comida y les envió codornices;

los sació con pan del cielo.

41Abrió la roca y brotó agua

que corrió por el desierto como un río.

42Se acordó Dios de su santa promesa,

la que hizo a su siervo Abraham.

43Sacó a su pueblo, a sus escogidos,

en medio de gran alegría y de gritos jubilosos.

44Les entregó las tierras que poseían las naciones;

heredaron el fruto del trabajo de otros pueblos

45para que ellos observaran sus estatutos

y pusieran en práctica sus leyes.

¡Aleluya!