Masalimo 105 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 105:1-45

Salimo 105

1Yamikani Yehova, itanani dzina lake;

lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.

2Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo;

fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.

3Munyadire dzina lake loyera;

mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.

4Dalirani Yehova ndi mphamvu zake;

funafunani nkhope yake nthawi yonse.

5Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita,

zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,

6inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake,

inu ana a Yakobo, osankhika ake.

7Iye ndiye Yehova Mulungu wathu;

maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.

8Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya,

mawu amene analamula kwa mibado yonse,

9pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu,

lumbiro limene analumbira kwa Isake.

10Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa,

kwa Israeli monga pangano lamuyaya:

11“Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani

ngati gawo la cholowa chako.”

12Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero,

ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,

13ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina,

kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.

14Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza;

anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:

15“Musakhudze odzozedwa anga;

musachitire choyipa aneneri anga.”

16Iye anabweretsa njala pa dziko

ndipo anawononga chakudya chonse;

17Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo,

Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.

18Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza,

khosi lake analiyika mʼzitsulo,

19mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa,

mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.

20Mfumu inatuma munthu kukamumasula,

wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.

21Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake,

wolamulira zonse zimene iye anali nazo,

22kulangiza ana a mfumu monga ankafunira

ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.

23Tsono Israeli analowa mu Igupto;

Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.

24Yehova anachulukitsa anthu ake;

ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;

25amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake,

kukonzera chiwembu atumiki ake.

26Yehova anatuma Mose mtumiki wake,

ndi Aaroni amene Iye anamusankha.

27Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo,

zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.

28Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima.

Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.

29Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi,

kuchititsa kuti nsomba zawo zife.

30Dziko lawo linadzaza ndi achule

amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.

31Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka

ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.

32Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala,

ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;

33Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu,

nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.

34Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera,

ziwala zosawerengeka;

35zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo,

zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.

36Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo,

zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.

37Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri,

ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.

38Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka,

pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.

39Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo,

ndi moto owawunikira usiku.

40Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri

ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.

41Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka;

ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.

42Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene

linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.

43Iye anatulutsa anthu ake akukondwera,

osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;

44Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina

ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,

45kuti iwo asunge malangizo ake

ndi kutsatira malamulo ake.

Tamandani Yehova.

New Russian Translation

Псалтирь 105:1-48

Псалом 105

1Аллилуйя!

Славьте Господа,

потому что Он благ и милость Его навеки!

2Кто выразит могущество Господа

и возвестит всю Его славу?

3Блаженны те, кто хранит правосудие

и вершит праведные дела во все времена!

4Вспомни меня, Господи, во время благоволения к Своему народу,

помоги и мне, когда будешь спасать их,

5чтобы я увидел благополучие Твоих избранных,

возвеселился вместе с Твоим народом

и хвалился – с Твоим наследием.

6Мы согрешили, как и наши предки,

совершили беззаконие, поступили нечестиво.

7Отцы наши не поняли Твоих чудес в Египте,

забыли обилие Твоей милости

и возмутились у моря, у Красного моря.

8Он все же спас их ради Своего имени,

чтобы показать Свое могущество.

9Он приказал Красному морю, и оно высохло,

и провел Он их через его глубины, как по пустыне.

10Спас их от рук ненавидящего их,

избавил их от руки врага105:10 См. Исх. 14:30..

11Воды покрыли противников их,

не осталось ни одного.

12Тогда поверили они Его словам

и воспели Ему хвалу.

13Но вскоре забыли Его дела,

не ждали Его совета.

14Возгорелись страстным желанием в пустыне

и испытывали Бога в необитаемой местности.

15Он дал им желаемое,

но наслал на них истощение.

16Они позавидовали Моисею в лагере

и Аарону, святому Господню.

17Земля разверзлась и поглотила Датана

и все скопище Авирама105:17 См. Чис. 16 глава..

18Возгорелся огонь посреди них,

и пламя сожгло нечестивых.

19Они сделали изваяние тельца в Хориве

и поклонились истукану105:19 См. Исх. 32 глава.,

20променяли свою Славу

на изображение быка, питающегося травой.

21Забыли Бога, своего Спасителя,

сотворившего великие дела в Египте,

22чудеса в земле Хама

и устрашающие дела у Красного моря.

23Поэтому Он сказал, что погубил бы их,

если бы Моисей, избранный Его,

не встал перед Ним в расселине,

чтобы отвратить Его ярость,

чтобы Он не погубил их105:23 См. Исх. 32:11-14..

24И пренебрегли они землей желанной105:24 То есть землей Ханаана, которую Бог сделал наследием Израиля. См. Чис. 13 и 14 главы.,

не поверили Его обещанию,

25роптали в своих шатрах

и не слушались голоса Господа.

26Поэтому Он поклялся с поднятой рукой,

что поразит их в пустыне,

27а также их потомков среди народов,

и рассеет их по землям.

28Они присоединились к Баал-Пеору105:28 Баал-Пеор – божество средиземноморских народов.

и ели жертвы, принесенные бездушным.

29Раздражали Его своими делами,

и разразился среди них мор.

30Но поднялся Пинехас, произвел суд,

и мор прекратился105:30 См. Чис. 25.,

31Это вменилось в праведность ему

из поколения в поколение, навсегда.

32Еще они прогневали Его у вод Меривы105:32 На языке оригинала это слово означает «ссора». См. Исх. 17:1-7 и Чис. 20:2-13,

и Моисей был наказан из-за них,

33потому что они возмутили его дух,

и он погрешил своими устами105:33 См. Чис. 20:2-13..

34Не уничтожили они народы,

о которых сказал им Господь,

35а смешались с язычниками

и научились их делам;

36служили их идолам,

которые стали для них сетью105:36 См. Суд. 1:19–2:23..

37Приносили демонам в жертву

своих сыновей и дочерей;

38проливали невинную кровь,

кровь своих сыновей и дочерей,

которых жертвовали ханаанским идолам,

и земля осквернилась кровью.

39Они оскверняли себя своими делами,

прелюбодействовали своими поступками105:34-39 См. Втор. 7:1-6; 18:9-13; Суд. 1:19–2:5..

40Поэтому возгорелся гнев Господень на Его народ,

и возгнушался Он Своим наследием.

41Он отдал их в руки чужеземцев,

и ненавидящие Израиль властвовали над ними.

42Враги притесняли их,

и они смирились под их рукой.

43Много раз Он избавлял их,

но они гневили Его своим упрямством

и были унижены в своем беззаконии.

44Все же Он обращал внимание на их скорбь,

когда слышал их вопль,

45вспоминал о Своем завете с ними

и смягчался по Своей великой милости.

46Он вызывал к ним сострадание

со стороны всех, кто пленял их.

47Спаси нас, Господи, наш Боже,

и собери нас из среды народов,

чтобы мы воздали благодарность Твоему святому имени

и хвалились Твоей славой.

48Прославлен будь, Господь, Бог Израиля,

от века и до века!

И весь народ сказал: «Аминь!»105:48 Аминь – еврейское слово, которое переводится как «да, верно, воистину так» или «да будет так».

Аллилуйя!