Salimo 105
1Yamikani Yehova, itanani dzina lake;
lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
2Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo;
fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
3Munyadire dzina lake loyera;
mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
4Dalirani Yehova ndi mphamvu zake;
funafunani nkhope yake nthawi yonse.
5Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita,
zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
6inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake,
inu ana a Yakobo, osankhika ake.
7Iye ndiye Yehova Mulungu wathu;
maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
8Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya,
mawu amene analamula kwa mibado yonse,
9pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu,
lumbiro limene analumbira kwa Isake.
10Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa,
kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
11“Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani
ngati gawo la cholowa chako.”
12Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero,
ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
13ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina,
kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
14Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza;
anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
15“Musakhudze odzozedwa anga;
musachitire choyipa aneneri anga.”
16Iye anabweretsa njala pa dziko
ndipo anawononga chakudya chonse;
17Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo,
Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
18Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza,
khosi lake analiyika mʼzitsulo,
19mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa,
mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
20Mfumu inatuma munthu kukamumasula,
wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
21Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake,
wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
22kulangiza ana a mfumu monga ankafunira
ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
23Tsono Israeli analowa mu Igupto;
Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
24Yehova anachulukitsa anthu ake;
ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
25amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake,
kukonzera chiwembu atumiki ake.
26Yehova anatuma Mose mtumiki wake,
ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
27Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo,
zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
28Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima.
Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
29Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi,
kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
30Dziko lawo linadzaza ndi achule
amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
31Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka
ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
32Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala,
ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
33Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu,
nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
34Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera,
ziwala zosawerengeka;
35zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo,
zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
36Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo,
zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
37Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri,
ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
38Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka,
pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
39Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo,
ndi moto owawunikira usiku.
40Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri
ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
41Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka;
ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
42Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene
linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
43Iye anatulutsa anthu ake akukondwera,
osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
44Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina
ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
45kuti iwo asunge malangizo ake
ndi kutsatira malamulo ake.
Tamandani Yehova.
하나님과 그의 백성
1너희는
여호와께 감사하고
그의 이름을 선포하며
그가 행하신 일을
온 세상에 알게 하라.
2그에게 노래하고 그를 찬양하며
그의 신기한 일을 말하라.
3그의 거룩한 이름을 자랑하라.
여호와를 찾는 자에게는
즐거움이 있으리라.
4너희는 여호와를 찾고
그의 능력을 구하며
항상 그를 바라보아라.
5여호와의 종 아브라함의 후손들아,
6하나님이 택하신
이스라엘 자손들아,
너희는 그가 행하신
놀랍고 신기한 일과
그가 내린 심판을 기억하라.
7그는 여호와 우리 하나님이시다.
그가 온 세상을 심판하신다.
8그는 영원한 자기 계약,
곧 천 대에까지 약속하신
그의 말씀을 기억하셨으니
9이것은 그가 아브라함과
맺은 계약이며
이삭에게 하신 맹세요
10야곱에게 하신 약속이며
이스라엘과 맺은
영원한 계약이다.
11이것이 바로
“내가 가나안 땅을 너에게 주어
네 소유가 되게 하겠다” 고
하신 말씀이다.
12이스라엘 백성의 수가 매우 적고
가나안 땅에서
그들이 나그네가 되어
13이 민족 저 민족,
이 나라 저 나라로
방황할 때에도
14하나님은 아무도 그들을
괴롭히지 못하게 하시고
그들을 위해
모든 왕들에게 경고하셨다.
15“나의 택한 종들에게 손대지 말고
나의 예언자들을 해하지 말라.”
16그가 그 땅에 기근을 보내
양식이 다 떨어지게 하셨으나
17한 사람을 앞서 보내셨으니
종으로 팔린 요셉이었다.
18족쇄에 그 발이 상하고
그 몸이 쇠사슬에 묶였으니
19여호와의 말씀이
이루어질 때까지라.
그 말씀이
105:19 또는 ‘저를 단련하였도다’그가 진실함을 입증하였다.
20왕이 사람을 보내
그를 석방하였으니
여러 민족을 통치하는 자가
그를 자유롭게 하였다.
21그가 나라 살림을 그에게 맡겨
그의 모든 소유를 관리하게 하고
22왕의 신하들을
마음대로 다스리게 하며
그의 고문관들을 교훈하게 하였다.
23그때 야곱이 이집트로 들어가
함의 땅에서 살게 되었다.
24여호와께서 자기 백성을
크게 번성하게 하셔서
그들의 대적보다 더 강하게 하시고
25이집트 사람들의 마음을 돌이켜
자기 백성을 미워하게 하고
자기 종들을
교활하게 다루도록 하셨다.
26그가 자기 종 모세와
자기가 택한 아론을 보내시자
27그들이 자기 백성들에게
여호와의 표적을 보이고
함 땅에 기적을 행하였다.
28여호와께서 흑암을 보내
그 땅을 어둡게 하셨으나
이집트 사람들은
그의 명령에 순종하지 않았다.
29그가 강물을 피가 되게 하시고
물고기를 죽이셨다.
30그 땅이 개구리로 뒤덮여
왕의 침실에도 뛰어들었다.
31여호와께서 말씀하시니
파리떼가 나오고
온 땅에 105:31 또는 ‘각다귀’이가 생겼다
32그가 저희 땅에
비 대신 우박과 번개를 보내시고
33포도나무와 무화과나무를 치시며
그 땅의 나무들을 꺾으셨다.
34여호와께서 말씀하시자
수많은 메뚜기떼가 날아와서
35그 땅의 모든 채소와
농작물을 먹어 버렸다.
36여호와께서 이집트 가정의
모든 장남을 죽이시고
37자기 백성을 인도하여
은과 금을 가지고 나오게 하셨으니
그들 가운데
병든 자나 약한 자들이 없었다.
38그들이 떠날 때
이집트 사람들이 기뻐하였으니
그들이 이스라엘 사람들을
두려워하였기 때문이었다.
39여호와께서 구름을 펴셔서
따가운 햇볕을 막는
덮개가 되게 하시고
밤에는 불 기둥으로
그들의 갈 길을 밝혀 주셨으며
40그들이 요구하므로
메추라기를 보내 주시고
하늘의 양식으로
그들을 만족하게 하셨다.
41그가 바위를 가르시자
물이 솟구쳐나와
메마른 땅에 강처럼 흘렀으니
42그의 종 아브라함에게 하신
그의 거룩한 약속을
기억하셨음이라.
43그가 택한 자기 백성을
이끌어내셨으므로
그들이 기뻐서 노래하며 외쳤다.
44그가 이방 나라들의 땅을
그들에게 주시고
다른 민족이 애써 지은 농작물을
그들에게 주셨으니
45자기 백성이 그의 법을 지키고
그의 명령에
순종하도록 하기 위해서였다.
105:45 또는 ‘할렐루야’여호와를 찬양하라!