Masalimo 105 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 105:1-45

Salimo 105

1Yamikani Yehova, itanani dzina lake;

lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.

2Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo;

fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.

3Munyadire dzina lake loyera;

mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.

4Dalirani Yehova ndi mphamvu zake;

funafunani nkhope yake nthawi yonse.

5Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita,

zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,

6inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake,

inu ana a Yakobo, osankhika ake.

7Iye ndiye Yehova Mulungu wathu;

maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.

8Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya,

mawu amene analamula kwa mibado yonse,

9pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu,

lumbiro limene analumbira kwa Isake.

10Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa,

kwa Israeli monga pangano lamuyaya:

11“Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani

ngati gawo la cholowa chako.”

12Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero,

ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,

13ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina,

kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.

14Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza;

anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:

15“Musakhudze odzozedwa anga;

musachitire choyipa aneneri anga.”

16Iye anabweretsa njala pa dziko

ndipo anawononga chakudya chonse;

17Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo,

Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.

18Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza,

khosi lake analiyika mʼzitsulo,

19mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa,

mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.

20Mfumu inatuma munthu kukamumasula,

wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.

21Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake,

wolamulira zonse zimene iye anali nazo,

22kulangiza ana a mfumu monga ankafunira

ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.

23Tsono Israeli analowa mu Igupto;

Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.

24Yehova anachulukitsa anthu ake;

ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;

25amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake,

kukonzera chiwembu atumiki ake.

26Yehova anatuma Mose mtumiki wake,

ndi Aaroni amene Iye anamusankha.

27Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo,

zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.

28Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima.

Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.

29Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi,

kuchititsa kuti nsomba zawo zife.

30Dziko lawo linadzaza ndi achule

amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.

31Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka

ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.

32Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala,

ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;

33Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu,

nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.

34Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera,

ziwala zosawerengeka;

35zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo,

zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.

36Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo,

zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.

37Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri,

ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.

38Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka,

pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.

39Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo,

ndi moto owawunikira usiku.

40Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri

ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.

41Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka;

ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.

42Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene

linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.

43Iye anatulutsa anthu ake akukondwera,

osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;

44Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina

ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,

45kuti iwo asunge malangizo ake

ndi kutsatira malamulo ake.

Tamandani Yehova.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 105:1-45

第 105 篇

上帝和祂的子民

(平行经文:历代志上16:8-22

1你们要称谢耶和华,呼求祂的名,

在列邦传扬祂的作为。

2要歌颂、赞美祂,

述说祂一切奇妙的作为。

3要以祂的圣名为荣,

愿寻求耶和华的人都欢欣。

4要寻求耶和华和祂的能力,

时常来到祂面前。

5-6祂仆人亚伯拉罕的后裔,

祂所拣选的雅各的子孙啊,

要记住祂所行的神迹奇事和祂口中的判词。

7祂是我们的上帝耶和华,

祂在普天下施行审判。

8祂永远记得祂的约,

历经千代也不忘祂的应许,

9就是祂与亚伯拉罕所立的约,

以撒所起的誓。

10祂把这约定为律例赐给雅各

定为永远的约赐给以色列

11祂说:“我必把迦南赐给你,

作为你的产业。”

12那时他们人丁稀少,

在当地寄居。

13他们在异国他乡流离飘零。

14耶和华不容人压迫他们,

还为他们的缘故责备君王,

15说:“不可难为我膏立的人,

也不可伤害我的先知。”

16祂在那里降下饥荒,

断绝一切食物的供应。

17祂派一个人率先前往,

这人就是被卖为奴隶的约瑟

18他被戴上脚镣,套上枷锁,

19直到后来他的预言应验,

耶和华的话试炼了他。

20埃及王下令释放他,

百姓的首领给他自由,

21派他执掌朝政,

管理国中的一切,

22有权柄管束王的大臣,

将智慧传授王的长老。

23以色列来到埃及

寄居在地。

24耶和华使祂的子民生养众多,

比他们的仇敌还要强盛。

25祂使仇敌憎恨他们,

用诡计虐待他们。

26祂派遣祂的仆人摩西和祂拣选的亚伦

27埃及行神迹,

地行奇事。

28祂降下黑暗,使黑暗笼罩那里;

他们没有违背祂的话。

29祂使埃及的水变成血,

鱼都死去;

30又使国中到处是青蛙,

王宫禁院也不能幸免。

31祂一发命令,

苍蝇蜂拥而至,虱子遍满全境。

32祂使雨变成冰雹,

遍地电光闪闪。

33祂击倒他们的葡萄树和无花果树,

摧毁他们境内的树木。

34祂一发声,

就飞来无数蝗虫和蚂蚱,

35吃尽他们土地上的植物,

吃尽他们田间的出产。

36祂又击杀他们境内所有的长子,

就是他们年轻力壮时生的长子。

37祂带领以色列人携金带银地离开埃及

各支派中无人畏缩。

38埃及人惧怕他们,

乐见他们离去。

39祂铺展云彩为他们遮荫,

晚上用火给他们照明。

40他们祈求,

祂就赐下鹌鹑,降下天粮,

叫他们饱足。

41祂使磐石裂开、涌出水来,

在干旱之地奔流成河。

42因为祂没有忘记祂赐给仆人亚伯拉罕的神圣应许。

43祂带领自己的子民欢然离去,

祂所拣选的百姓欢唱着前行。

44祂把列国的土地赐给他们,

使他们获得别人的劳动成果。

45祂这样做是要使他们持守祂的命令,

遵行祂的律法。

你们要赞美耶和华!