Masalimo 105 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 105:1-45

Salimo 105

1Yamikani Yehova, itanani dzina lake;

lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.

2Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo;

fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.

3Munyadire dzina lake loyera;

mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.

4Dalirani Yehova ndi mphamvu zake;

funafunani nkhope yake nthawi yonse.

5Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita,

zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,

6inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake,

inu ana a Yakobo, osankhika ake.

7Iye ndiye Yehova Mulungu wathu;

maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.

8Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya,

mawu amene analamula kwa mibado yonse,

9pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu,

lumbiro limene analumbira kwa Isake.

10Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa,

kwa Israeli monga pangano lamuyaya:

11“Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani

ngati gawo la cholowa chako.”

12Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero,

ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,

13ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina,

kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.

14Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza;

anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:

15“Musakhudze odzozedwa anga;

musachitire choyipa aneneri anga.”

16Iye anabweretsa njala pa dziko

ndipo anawononga chakudya chonse;

17Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo,

Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.

18Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza,

khosi lake analiyika mʼzitsulo,

19mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa,

mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.

20Mfumu inatuma munthu kukamumasula,

wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.

21Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake,

wolamulira zonse zimene iye anali nazo,

22kulangiza ana a mfumu monga ankafunira

ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.

23Tsono Israeli analowa mu Igupto;

Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.

24Yehova anachulukitsa anthu ake;

ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;

25amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake,

kukonzera chiwembu atumiki ake.

26Yehova anatuma Mose mtumiki wake,

ndi Aaroni amene Iye anamusankha.

27Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo,

zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.

28Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima.

Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.

29Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi,

kuchititsa kuti nsomba zawo zife.

30Dziko lawo linadzaza ndi achule

amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.

31Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka

ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.

32Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala,

ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;

33Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu,

nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.

34Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera,

ziwala zosawerengeka;

35zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo,

zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.

36Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo,

zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.

37Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri,

ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.

38Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka,

pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.

39Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo,

ndi moto owawunikira usiku.

40Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri

ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.

41Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka;

ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.

42Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene

linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.

43Iye anatulutsa anthu ake akukondwera,

osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;

44Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina

ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,

45kuti iwo asunge malangizo ake

ndi kutsatira malamulo ake.

Tamandani Yehova.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Забур 105:1-48

Песнь 105

Славьте Вечного!

1Славьте Вечного, потому что Он благ

и милость Его – навеки!

2Кто выразит могущество Вечного

и возвестит всю Его славу?

3Благословенны те, кто хранит правосудие

и вершит праведные дела во все времена.

4Вспомни меня, Вечный, во время благоволения к Своему народу,

помоги и мне, когда будешь спасать их,

5чтобы я увидел благополучие Твоих избранных,

возвеселился вместе с Твоим народом

и хвалился вместе с Твоим наследием.

6Мы согрешили, как и наши предки,

совершили беззаконие, поступили нечестиво.

7Отцы наши не поняли Твоих чудес в Египте,

забыли обилие Твоих щедрот

и возмутились у Тростникового моря105:7 Тростниковое море – буквальный перевод с языка оригинала. Среди современных специалистов существуют различные мнения, о каком водоёме здесь идёт речь. Тростниковым морем могли называть как цепи озёр, расположенных на Суэцком перешейке и, вероятно, соединявшихся тогда проливами с Красным морем, так и Суэцкий и Акабский заливы Красного моря (см. напр., 3 Цар. 9:26). В Инджиле эти же воды названы Красным морем. Также в ст. 9 и 22..

8Он всё же спас их ради Своего имени,

чтобы показать Своё могущество.

9Он приказал Тростниковому морю,

и оно высохло,

и провёл Он их через его глубины,

как по суше.

10Спас их от рук ненавидящих их,

избавил их от руки врага.

11Воды покрыли противников их,

не осталось ни одного.

12Тогда поверили они Его словам

и воспели Ему хвалу105:7-12 См. Исх. 14:10-31..

13Но вскоре забыли Его дела,

не ждали Его совета.

14Страстно возжелали в пустыне мяса

и испытывали Всевышнего в необитаемой местности.

15Он дал им желаемое,

но послал на них страшную болезнь105:13-15 См. Чис. 11..

16Они позавидовали в стане Мусо

и Хоруну, священнослужителю Вечного.

17Земля разверзлась и поглотила Датана

и всё скопище Авирама.

18Возгорелся огонь посреди них,

и пламя сожгло нечестивых105:16-18 См. Чис. 16..

19Они сделали изваяние тельца на Синае105:19 Букв.: «на Хориве». Хорив – другое название горы Синай.

и поклонились истукану;

20променяли Всевышнего, их Славу,

на изображение быка, питающегося травой.

21Забыли Всевышнего, своего Спасителя,

сотворившего великие дела в Египте,

22чудеса в земле Хама105:22 То есть в Египте. Египтяне были потомками Хама (см. Нач. 10:6-10).

и устрашающие дела у Тростникового моря.

23Поэтому Он сказал, что уничтожит их,

и уничтожил бы, если бы не Мусо, избранный Его,

который встал перед Ним в расселине,

чтобы отвратить Его ярость,

чтобы Он не погубил их105:19-23 См. Исх. 32..

24И пренебрегли они землёй желанной,

не поверили Его обещанию,

25роптали в своих шатрах

и не слушались голоса Вечного.

26Поэтому Он поклялся с поднятой рукой,

что поразит их в пустыне,

27а также их потомков среди народов,

и рассеет их по землям105:24-27 См. Чис. 13–14..

28Они присоединились к Баал-Пеору105:28 Баал-Пеор – божество, почитавшееся моавитянами.

и ели жертвы, принесённые мёртвым идолам.

29Раздражали Его своими делами,

и разразился среди них мор.

30Но поднялся Пинхас, произвёл суд,

и мор прекратился.

31Это вменилось в праведность ему,

что навсегда останется в памяти поколений105:28-31 См. Чис. 25..

32Ещё они прогневали Его у вод Меривы,

и Мусо был наказан из-за них,

33потому что они возмутили его дух,

и он погрешил своими устами105:32-33 См. Исх. 17:1-7; Чис. 20:2-13..

34Не уничтожили они народы,

вопреки повелению Вечного,

35а смешались с ними

и научились их делам;

36служили их идолам,

которые стали для них сетью.

37Приносили демонам в жертву

своих сыновей и дочерей;

38проливали невинную кровь,

кровь своих сыновей и дочерей,

которых жертвовали ханонским идолам,

и земля осквернилась кровью.

39Они оскверняли себя своими делами,

распутничали своими поступками105:34-39 См. Втор. 7:1-6; 18:9-13; Суд. 1:19–2:5..

40Поэтому возгорелся гнев Вечного на Его народ,

и возгнушался Он Своим наследием.

41Он отдал их в руки чужеземцев,

и ненавидящие Исроил властвовали над ними.

42Враги притесняли их,

и они смирились под их рукой.

43Много раз Он избавлял их,

но они гневили Его своим упрямством

и были унижены в своём беззаконии105:40-43 См. Суд. 2:10-19..

44Всё же Он обращал внимание на их скорбь,

когда слышал их вопль,

45вспоминал о Своём соглашении с ними

и смягчался по Своей великой милости.

46Он вызывал к ним сострадание

со стороны всех, кто пленял их.

47Спаси нас, Вечный, наш Бог,

и собери нас из среды народов,

чтобы славить нам Твоё святое имя

и Твоей славою хвалиться.

Заключительное благословение четвёртой книги

48Хвала Вечному, Богу Исроила,

от века и до века!

И весь народ пусть скажет: «Аминь!»105:48 Аминь – еврейское слово, которое переводится как «да, верно, воистину так» или «да будет так».

Славьте Вечного!