Masalimo 105 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 105:1-45

Salimo 105

1Yamikani Yehova, itanani dzina lake;

lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.

2Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo;

fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.

3Munyadire dzina lake loyera;

mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.

4Dalirani Yehova ndi mphamvu zake;

funafunani nkhope yake nthawi yonse.

5Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita,

zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,

6inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake,

inu ana a Yakobo, osankhika ake.

7Iye ndiye Yehova Mulungu wathu;

maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.

8Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya,

mawu amene analamula kwa mibado yonse,

9pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu,

lumbiro limene analumbira kwa Isake.

10Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa,

kwa Israeli monga pangano lamuyaya:

11“Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani

ngati gawo la cholowa chako.”

12Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero,

ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,

13ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina,

kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.

14Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza;

anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:

15“Musakhudze odzozedwa anga;

musachitire choyipa aneneri anga.”

16Iye anabweretsa njala pa dziko

ndipo anawononga chakudya chonse;

17Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo,

Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.

18Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza,

khosi lake analiyika mʼzitsulo,

19mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa,

mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.

20Mfumu inatuma munthu kukamumasula,

wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.

21Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake,

wolamulira zonse zimene iye anali nazo,

22kulangiza ana a mfumu monga ankafunira

ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.

23Tsono Israeli analowa mu Igupto;

Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.

24Yehova anachulukitsa anthu ake;

ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;

25amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake,

kukonzera chiwembu atumiki ake.

26Yehova anatuma Mose mtumiki wake,

ndi Aaroni amene Iye anamusankha.

27Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo,

zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.

28Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima.

Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.

29Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi,

kuchititsa kuti nsomba zawo zife.

30Dziko lawo linadzaza ndi achule

amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.

31Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka

ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.

32Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala,

ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;

33Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu,

nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.

34Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera,

ziwala zosawerengeka;

35zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo,

zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.

36Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo,

zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.

37Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri,

ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.

38Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka,

pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.

39Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo,

ndi moto owawunikira usiku.

40Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri

ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.

41Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka;

ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.

42Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene

linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.

43Iye anatulutsa anthu ake akukondwera,

osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;

44Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina

ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,

45kuti iwo asunge malangizo ake

ndi kutsatira malamulo ake.

Tamandani Yehova.

La Bible du Semeur

Psaumes 105:1-45

Dieu est fidèle105 Pour les v. 1-15, voir 1 Ch 16.8-22.

1Louez l’Eternel, ╵et faites appel à lui !

Publiez parmi les peuples ╵ses hauts faits !

2Chantez à sa gloire, ╵et célébrez-le ╵en musique !

Racontez sans cesse ╵toutes ses merveilles !

3Soyez fiers de lui, ╵car il est très saint !

Que le cœur de ceux ╵qui sont attachés à l’Eternel ╵soit rempli de joie !

4Tournez-vous vers l’Eternel ! ╵Faites appel à sa force !

Aspirez à vivre ╵constamment en sa présence !

5Souvenez-vous des merveilles ╵qu’il a accomplies !

Rappelez-vous ses prodiges ╵et les jugements ╵qu’il a prononcés,

6vous, les descendants ╵d’Abraham, son serviteur,

vous, descendants de Jacob, ╵vous qu’il a choisis !

7Notre Dieu, c’est l’Eternel,

sur toute la terre ╵s’exercent ses jugements.

8Il se souvient pour toujours ╵de son alliance,

de ce qu’il a donné sa parole ╵pour mille générations105.8 Voir Dt 7.9. :

9il a conclu un traité ╵avec Abraham,

et l’a confirmé ╵par serment à Isaac105.9 Voir Gn 12.7 ; 17.8 ; 22.16-17 ; 26.3..

10Il l’a confirmé ╵à Jacob ╵en en faisant une loi,

et, pour Israël, ╵une alliance pour toujours.

11Il a déclaré : ╵« Je te donnerai ╵le pays de Canaan,

ce sera la part ╵que vous allez posséder105.11 Pour les v. 10-11, voir Gn 28.13-15.. »

12Ils n’étaient alors ╵qu’un très petit nombre,

une poignée d’immigrants105.12 Voir Gn 34.30 ; Dt 7.7 ; 26.5.,

13allant çà et là, ╵d’une peuplade à une autre,

d’un royaume vers un autre peuple.

14Mais Dieu ne laissa personne ╵les persécuter ;

il réprimanda des rois à leur sujet :

15« Ne maltraitez pas ╵ceux qui me sont consacrés

et ne faites pas de mal ╵à ceux qui sont mes prophètes105.15 Pour les v. 14-15, voir Gn 12.17 ; 20.3-7. ! »

16Il fit venir la famine ╵sur tout le pays,

les privant de pain105.16 Voir Gn 41.53-57..

17Il envoya devant eux un homme :

Joseph, vendu comme esclave105.17 Voir Gn 37.28 ; 45.5..

18On chargea ses pieds de chaînes,

son cou d’un carcan de fer105.18 Voir Gn 39.20.

19jusqu’au jour où s’accomplit ╵ce que Joseph avait annoncé.

Alors la parole ╵prononcée par l’Eternel ╵montra qu’il avait raison105.19 Voir Gn 37.6-10. :

20le roi ordonna ╵de le délier ;

le dominateur des peuples ╵le fit relâcher105.20 Voir Gn 41.14.

21et il l’établit seigneur sur son royaume,

il le nomma gouverneur ╵de tous ses domaines105.21 Voir Gn 41.39-41.

22pour donner ses instructions à ses ministres ╵comme il le jugerait bon,

pour enseigner la sagesse ╵à ses conseillers.

23Puis Israël se rendit ╵en Egypte,

Jacob émigra ╵au pays de Cham105.23 Voir Gn 46.6 ; 47.11..

24Dieu rendit son peuple ╵très fécond,

plus puissant ╵que ses ennemis.

25Il changea les dispositions de ceux-ci, ╵qui se mirent à haïr son peuple,

à préparer le malheur ╵de ses serviteurs105.25 Pour les v. 24-25, voir Ex 1.7-14..

26Alors il leur envoya ╵Moïse, son serviteur,

Aaron qu’il avait choisi105.26 Voir Ex 3.1-4, 17..

27En Egypte, ils accomplirent ╵sur son ordre des miracles

et de grands prodiges ╵au pays de Cham.

28Il envoya les ténèbres ╵qui couvrirent le pays105.28 Voir Ex 10.21-29.,

et les Egyptiens cessèrent ╵de résister à ses ordres105.28 Voir Ex 11.1-2. L’ancienne version grecque et la syriaque portent : avaient résisté à ses ordres..

29Il changea leurs eaux en sang

et fit mourir leurs poissons105.29 Voir Ex 7.14-25..

30Il fit grouiller de grenouilles ╵le pays entier

jusqu’aux chambres de leur roi105.30 Voir Ex 7.26 à 8.11..

31Sur un ordre de sa part, ╵parurent des mouches venimeuses,

les moustiques envahirent ╵le pays entier105.31 Voir Ex 8.12-28..

32Au lieu de la pluie, ╵il leur envoya la grêle

et il fit tomber la foudre ╵sur tout leur pays.

33Il frappa ╵leurs vignes et leurs figuiers

et brisa les arbres ╵de leur territoire105.33 Voir Ex 9.13-35..

34Sur un ordre de sa part, ╵d’innombrables sauterelles

et des criquets arrivèrent

35pour dévorer toute l’herbe ╵à travers tout le pays,

et tous les produits ╵de leur terre105.35 Voir Ex 10.1-20..

36Puis il fit mourir ╵tous les fils aînés dans leur pays,

premiers fruits de leur vigueur virile105.36 Voir Ex 12.29-30.,

37et il fit sortir les siens ╵avec de l’argent, de l’or105.37 Voir Ex 12.35-36.,

sans qu’aucun trébuche ╵parmi ses tribus.

38Les Egyptiens se réjouirent ╵de les voir partir,

car devant ce peuple, ╵ils étaient terrorisés105.38 Voir Ex 12.33 ; 15.16..

39Il étendit la nuée ╵comme un rideau protecteur,

et il fit briller un feu ╵pour les éclairer la nuit105.39 Voir Ex 13.21-22 ; 14.19-20..

40Parce qu’ils le demandèrent, ╵il leur envoya des cailles

et les rassasia ╵du pain qui venait du ciel105.40 Voir Ex 16.13-18..

41Il fendit la roche, ╵et l’eau en jaillit.

A travers la steppe aride, ╵elle coula comme un fleuve105.41 Voir Ex 17.1-7 ; Nb 20.2-13.,

42car il se souvint ╵d’Abraham, son serviteur,

et de la promesse sainte ╵qu’il lui avait faite105.42 Voir Gn 15.13-14 ; Ex 2.24..

43Il fit sortir du pays ╵son peuple dans l’allégresse

et ceux qu’il avait choisis ╵avec des cris de triomphe.

44Il leur a donné les terres ╵occupées par d’autres peuples

et les a fait profiter ╵du travail que ces populations ╵avaient accompli105.44 Voir Jos 11.16-23.,

45pour qu’ils obéissent ╵à ce qu’il avait prescrit

et qu’ils respectent ses lois.

Louez l’Eternel !