Masalimo 103 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 103:1-22

Salimo 103

Salimo la Davide.

1Tamanda Yehova, iwe moyo wanga;

ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.

2Tamanda Yehova, iwe moyo wanga,

ndipo usayiwale zabwino zake zonse.

3Amene amakhululuka machimo ako onse

ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,

4amene awombola moyo wako ku dzenje

ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,

5amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino,

kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.

6Yehova amachita chilungamo

ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.

7Iye anadziwitsa Mose njira zake,

ntchito zake kwa Aisraeli.

8Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima,

wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.

9Iye sadzatsutsa nthawi zonse,

kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;

10satichitira molingana ndi machimo athu,

kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.

11Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi,

koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;

12monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo,

koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.

13Monga bambo amachitira chifundo ana ake,

choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa;

14pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira,

amakumbukira kuti ndife fumbi.

15Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu,

amaphuka ngati duwa la mʼmunda;

16koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso

ndipo malo ake sakumbukirikanso.

17Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya

chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa,

ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo;

18iwo amene amasunga pangano lake

ndi kukumbukira kumvera malangizo ake.

19Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba

ndipo ufumu wake umalamulira onse.

20Tamandani Yehova, inu angelo ake,

amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula,

amene mumamvera mawu ake.

21Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba,

inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake.

22Tamandani Yehova, ntchito yake yonse

kulikonse mu ulamuliro wake.

Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.

Korean Living Bible

시편 103:1-22

여호와의 크신 은혜

(다윗의 시)

1내 영혼아,

여호와를 찬양하라!

내 속에 있는 것들아,

다 그의 거룩한 이름을 찬양하라.

2내 영혼아,

여호와를 찬양하며

그의 모든 은혜를 잊지 말아라.

3그가 너의 모든 죄를 용서하시며

너의 모든 병을 고치시고

4네 생명을 파멸에서 구하시며

너에게 풍성한 사랑과

자비를 베풀고

5103:5 또는 ‘네 소원을’네 삶을 좋은 것으로

만족하게 하셔서

네 젊음을 독수리처럼

새롭게 하신다.

6여호와께서

의로운 일을 행하시며

억압당하는 모든 사람을 위해

정당한 판결을 내리신다.

7그가 자기 뜻을 모세에게 알리시고

이스라엘 백성에게

그의 놀라운 일을 보여 주셨다.

8여호와는 자비롭고 은혜로우시며

쉽게 화를 내지 않으시고

사랑이 풍성하신 분이시니

9항상 책망만 하지 않으시고

화를 영원히 품지 않으시리라.

10그가 우리의 죄에 따라

처벌하지 않으시고

우리의 잘못을

그대로 갚지 않으시니

11하늘이 땅에서 높은 것같이

자기를 두려워하는 자들에 대한

그의 사랑이 크기 때문이다.

12동이 서에서 먼 것같이

그가 우리 죄를 멀리 옮기셨으며

13아버지가

자식을 불쌍히 여기시듯이

여호와께서

자기를 두려워하는 자를

불쌍히 여기시니

14우리가 어떻게

만들어진 것을 아시며

우리가 먼지에 불과한 존재임을

기억하심이라.

15인생은 그 사는 날이 풀과 같고

그 영화가 들의 꽃과 같다.

16바람이 불면 그 꽃은 떨어져

다시 볼 수 없으나

17여호와의 사랑은

18자기를 두려워하는 자에게

영원부터 영원까지 이르고

그의 의는

그의 계약을 지키고

그의 계명을 기억하여

그것을 행하는 자들의

자손 대대에 미친다.

19여호와께서 그 보좌를

하늘에 세우시고

거기서 온 우주를 다스리신다.

20그의 명령을 수행하며

그의 말씀에 순종하는

너희 능력 있는 천사들아,

여호와를 찬양하라.

21여호와를 섬기며 그의 뜻을 행하는

너희 모든 하늘의 군대들아,

여호와를 찬양하라!

22그가 다스리는

너희 모든 피조물들아,

여호와를 찬양하라.

내 영혼아, 여호와를 찬양하라!