Salimo 103
Salimo la Davide.
1Tamanda Yehova, iwe moyo wanga;
ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.
2Tamanda Yehova, iwe moyo wanga,
ndipo usayiwale zabwino zake zonse.
3Amene amakhululuka machimo ako onse
ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,
4amene awombola moyo wako ku dzenje
ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,
5amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino,
kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.
6Yehova amachita chilungamo
ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.
7Iye anadziwitsa Mose njira zake,
ntchito zake kwa Aisraeli.
8Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima,
wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.
9Iye sadzatsutsa nthawi zonse,
kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;
10satichitira molingana ndi machimo athu,
kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.
11Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi,
koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;
12monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo,
koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.
13Monga bambo amachitira chifundo ana ake,
choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa;
14pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira,
amakumbukira kuti ndife fumbi.
15Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu,
amaphuka ngati duwa la mʼmunda;
16koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso
ndipo malo ake sakumbukirikanso.
17Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya
chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa,
ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo;
18iwo amene amasunga pangano lake
ndi kukumbukira kumvera malangizo ake.
19Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba
ndipo ufumu wake umalamulira onse.
20Tamandani Yehova, inu angelo ake,
amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula,
amene mumamvera mawu ake.
21Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba,
inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake.
22Tamandani Yehova, ntchito yake yonse
kulikonse mu ulamuliro wake.
Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
Guds nåde og trofasthed
1En sang af David.
Min sjæl, pris Herren,
alt i mig skal ophøje hans hellige navn.
2Min sjæl, pris Herren,
glem ikke hans velgerninger.
3Han tilgiver alle mine synder
og helbreder alle mine sygdomme.
4Han frier mig fra dødens gab,
velsigner mig med sin nåde og godhed.
5Han mætter mig med gode gaver,
jeg får min livskraft igen som ørnen.
6Han lader retfærdigheden ske fyldest,
så de undertrykte får deres ret.
7Han åbenbarede sine planer for Moses,
Israels folk var vidner til hans undere.
8Herren er barmhjertig og nådig
med tålmodig og trofast kærlighed.
9Han fortsætter ikke med at anklage os,
bliver ikke ved med at være vred.
10Han giver os ikke løn som forskyldt,
straffer os ikke i forhold til vore synder.
11Så højt som himlen er over jorden,
så stor er hans nåde mod dem, der har ærefrygt.
12Så langt som østen er fra vesten,
har han fjernet vore synder fra os.
13Som en far er barmhjertig mod sine børn,
er Herren barmhjertig mod dem, der ærer ham.
14Han forstår, hvor skrøbelige vi er,
han ved, at vi kun er som støv.
15Vores liv på jorden er som græsset,
som markblomster, der hurtigt forsvinder.
16Blæsten gør en ende på blomsten,
man skulle tro, den aldrig havde været der.
17Men Herrens trofasthed er evig,
den omslutter dem, der ærer ham.
Hans godhed bliver alle generationer til del,
18hvis de holder hans pagt og adlyder hans bud.
19Herren sidder på sin trone i Himlen,
alt er underlagt hans herredømme.
20Lovpris Herren, alle hans engle,
I vældige krigere, som adlyder hans ordrer
og udfører alle hans befalinger.
21Ja, pris Herren, I englehære,
som tjener ham og udfører hans vilje.
22Pris Herren, alle hans skabninger,
hvor I end befinder jer i hans rige.
Min sjæl, pris Herren.