Masalimo 102 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 102:1-28

Salimo 102

Pemphero la munthu wosautsidwa, pamene walefuka, nakhuthulira pamaso pa Yehova kulira kwakeko.

1Yehova imvani pemphero langa;

kulira kwanga kopempha thandizo kufike kwa Inu.

2Musandibisire nkhope yanu

pamene ndili pa msautso.

Munditcherere khutu;

pamene ndiyitana ndiyankheni msanga.

3Pakuti masiku anga akupita ngati utsi;

mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka.

4Mtima wanga wakanthidwa ndipo ukufota ngati udzu;

ndipo ndimayiwala kudya chakudya changa.

5Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula

ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha.

6Ndili ngati kadzidzi wa ku chipululu,

monga kadzidzi pakati pa mabwinja.

7Ndimagona osapeza tulo; ndakhala

ngati mbalame yokhala yokha pa denga.

8Tsiku lonse adani anga amandichita chipongwe;

iwo amene amandinyoza, amagwiritsa ntchito dzina langa ngati temberero.

9Pakuti ndimadya phulusa ngati chakudya changa

ndi kusakaniza chakumwa changa ndi misozi

10chifukwa cha ukali wanu waukulu,

popeza Inu mwandinyamula ndi kunditayira kumbali.

11Masiku anga ali ngati mthunzi wa kumadzulo;

Ine ndikufota ngati udzu.

12Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya;

kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.

13Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni

pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo;

nthawi yoyikika yafika.

14Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu;

fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni.

15Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova,

mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu.

16Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni

ndi kuonekera mu ulemerero wake.

17Iye adzayankha pemphero la anthu otayika;

sadzanyoza kupempha kwawo.

18Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo,

kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova:

19“Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba,

kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi,

20kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende,

kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.”

21Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni

ndi matamando ake mu Yerusalemu,

22pamene mitundu ya anthu ndi maufumu

adzasonkhana kuti alambire Yehova.

23Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga;

Iyeyo anafupikitsa masiku anga.

24Choncho Ine ndinati:

“Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga;

zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse.

25Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi

ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu.

26Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo;

zidzatha ngati chovala.

Mudzazisintha ngati chovala

ndipo zidzatayidwa.

27Koma Inu simusintha,

ndipo zaka zanu sizidzatha.

28Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu;

zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”

New International Reader’s Version

Psalm 102:1-28

Psalm 102

A prayer of a suffering person who has become weak. They pour out their problems to the Lord.

1Lord, hear my prayer.

Listen to my cry for help.

2Don’t turn your face away from me

when I’m in trouble.

Pay attention to me.

When I call out for help, answer me quickly.

3My days are disappearing like smoke.

My body burns like glowing coals.

4My strength has dried up like grass.

I even forget to eat my food.

5I groan out loud because of my suffering.

I’m nothing but skin and bones.

6I’m like a desert owl.

I’m like an owl among destroyed buildings.

7I can’t sleep. I’ve become

like a bird alone on a roof.

8All day long my enemies laugh at me.

Those who make fun of me use my name as a curse.

9I eat ashes as my food.

My tears fall into what I’m drinking.

10You were very angry with me.

So you picked me up and threw me away.

11The days of my life are like an evening shadow.

I dry up like grass.

12But Lord, you are seated on your throne forever.

Your fame will continue for all time to come.

13You will rise up and show deep concern for Zion.

The time has come for you to help Zion.

14The stones of your destroyed city are priceless to us.

Even its dust brings deep concern to us.

15The nations will worship the Lord.

All the kings on earth will respect his glorious power.

16The Lord will build Zion again.

He will appear in his glory.

17He will answer the prayer of those who don’t have anything.

He won’t say no to their cry for help.

18Let this be written down for those born after us.

Then people who are not yet born can praise the Lord.

19Here is what should be written.

“The Lord looked down from his temple in heaven.

From heaven he viewed the earth.

20He heard the groans of the prisoners.

He set free those who were sentenced to death.”

21So people will talk about him in Zion.

They will praise him in Jerusalem.

22Nations and kingdoms

will gather there to worship the Lord.

23When I was still young, he took away my strength.

He wasn’t going to let me live much longer.

24So I said, “My God, don’t let me die in the middle of my life.

You will live for all time to come.

25In the beginning you made the earth secure.

You placed it on its foundations.

Your hands created the heavens.

26They will pass away. But you will remain.

They will all wear out like a piece of clothing.

You will make them like clothes

that are taken off and thrown away.

27But you remain the same.

Your years will never end.

28Our children will live with you.

Their sons and daughters will be safe in your care.”