Masalimo 102 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 102:1-28

Salimo 102

Pemphero la munthu wosautsidwa, pamene walefuka, nakhuthulira pamaso pa Yehova kulira kwakeko.

1Yehova imvani pemphero langa;

kulira kwanga kopempha thandizo kufike kwa Inu.

2Musandibisire nkhope yanu

pamene ndili pa msautso.

Munditcherere khutu;

pamene ndiyitana ndiyankheni msanga.

3Pakuti masiku anga akupita ngati utsi;

mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka.

4Mtima wanga wakanthidwa ndipo ukufota ngati udzu;

ndipo ndimayiwala kudya chakudya changa.

5Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula

ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha.

6Ndili ngati kadzidzi wa ku chipululu,

monga kadzidzi pakati pa mabwinja.

7Ndimagona osapeza tulo; ndakhala

ngati mbalame yokhala yokha pa denga.

8Tsiku lonse adani anga amandichita chipongwe;

iwo amene amandinyoza, amagwiritsa ntchito dzina langa ngati temberero.

9Pakuti ndimadya phulusa ngati chakudya changa

ndi kusakaniza chakumwa changa ndi misozi

10chifukwa cha ukali wanu waukulu,

popeza Inu mwandinyamula ndi kunditayira kumbali.

11Masiku anga ali ngati mthunzi wa kumadzulo;

Ine ndikufota ngati udzu.

12Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya;

kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.

13Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni

pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo;

nthawi yoyikika yafika.

14Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu;

fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni.

15Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova,

mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu.

16Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni

ndi kuonekera mu ulemerero wake.

17Iye adzayankha pemphero la anthu otayika;

sadzanyoza kupempha kwawo.

18Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo,

kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova:

19“Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba,

kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi,

20kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende,

kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.”

21Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni

ndi matamando ake mu Yerusalemu,

22pamene mitundu ya anthu ndi maufumu

adzasonkhana kuti alambire Yehova.

23Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga;

Iyeyo anafupikitsa masiku anga.

24Choncho Ine ndinati:

“Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga;

zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse.

25Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi

ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu.

26Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo;

zidzatha ngati chovala.

Mudzazisintha ngati chovala

ndipo zidzatayidwa.

27Koma Inu simusintha,

ndipo zaka zanu sizidzatha.

28Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu;

zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”

Bibelen på hverdagsdansk

Salmernes Bog 102:1-29

Bøn om Herrens indgreb

1Fra en, der lider, men beder om og forventer Herrens hjælp.

2Herre, hør min bøn,

lad mit nødråb nå frem til dig.

3Vend dig ikke bort fra mig,

for jeg lider og er i stor nød.

Hør mig, når jeg kalder på dig,

kom mig hurtigt til hjælp.

4Jeg føler mit liv forsvinde som en røg,

det er, som om jeg blev lagt på et bål.

5Jeg er som afskåret græs, der er ved at visne,

jeg har mistet lysten til at spise.

6Jeg sukker og stønner højlydt,

jeg er snart ikke andet end skind og ben.

7Jeg er mager som en grib i ørkenen,

som en ugle i øde ruiner.

8Om natten ligger jeg vågen og jamrer,

så ulykkelig som en ensom fugl på taget.

9Dagen lang bliver jeg hånet af mine fjender,

de gør nar af mig og forbander mig.

10Den mad, jeg spiser, smager som aske,

min drik er blandet med tårer,

11fordi du udøste din vrede over mig,

du tog mig i kraven og kastede mig bort.

12Mit liv er snart forbi som aftenskyggen,

jeg visner bort som afskåret græs.

13Men du, min Gud, sidder evigt på tronen,

din storhed berømmes fra slægt til slægt.

14Rejs dig og se i nåde til Zion.

Det er tid til at vise din barmhjertighed,

du har jo lovet at komme os til hjælp.

15Selv om Jerusalem ligger i ruiner,

elsker dit folk byens sten og murbrokker.

16Folkeslag skal ære Herrens navn,

og jordens konger skal frygte for hans magt.

17For Herren vil genopbygge Jerusalem,

han vil åbenbare sin magt og herlighed.

18Han vil lytte til de nødstedtes råb,

ikke afvise deres indtrængende bøn.

19Det bliver nedskrevet for efterslægtens skyld,

så kommende generationer må prise Herren.

20Herren ser os fra sin bolig i himlen,

han betragter jorden fra sit himmelske tempel.

21Han hører de tilfangetagne stønne og klage,

han befrier dem, som var dømt til at dø.

22Sådan skal Herrens magt fejres i Zion,

hans frelse skal prises i Jerusalem.

23Da vil nationerne rådslå med hinanden,

og konger skal bøje sig for Herren.

24Herre, du har ramt mig i min bedste alder,

jeg føler, at min livskraft ebber ud.

25Åh, min Gud, du som lever for evigt,

lad mig ikke dø i min bedste alder.

26I begyndelsen grundlagde du jorden,

med egne hænder skabte du himmelrummet.

27Det hele skal forgå, men du vil bestå.

Himmel og jord slides op som en klædning,

du lægger dem væk som et udslidt stykke tøj.

28Men du er altid den samme,

dine leveår får aldrig ende.

29De kommende slægter skal leve i sikkerhed,

de skal få lov at trives i din nærhed.