Masalimo 102 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 102:1-28

Salimo 102

Pemphero la munthu wosautsidwa, pamene walefuka, nakhuthulira pamaso pa Yehova kulira kwakeko.

1Yehova imvani pemphero langa;

kulira kwanga kopempha thandizo kufike kwa Inu.

2Musandibisire nkhope yanu

pamene ndili pa msautso.

Munditcherere khutu;

pamene ndiyitana ndiyankheni msanga.

3Pakuti masiku anga akupita ngati utsi;

mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka.

4Mtima wanga wakanthidwa ndipo ukufota ngati udzu;

ndipo ndimayiwala kudya chakudya changa.

5Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula

ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha.

6Ndili ngati kadzidzi wa ku chipululu,

monga kadzidzi pakati pa mabwinja.

7Ndimagona osapeza tulo; ndakhala

ngati mbalame yokhala yokha pa denga.

8Tsiku lonse adani anga amandichita chipongwe;

iwo amene amandinyoza, amagwiritsa ntchito dzina langa ngati temberero.

9Pakuti ndimadya phulusa ngati chakudya changa

ndi kusakaniza chakumwa changa ndi misozi

10chifukwa cha ukali wanu waukulu,

popeza Inu mwandinyamula ndi kunditayira kumbali.

11Masiku anga ali ngati mthunzi wa kumadzulo;

Ine ndikufota ngati udzu.

12Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya;

kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.

13Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni

pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo;

nthawi yoyikika yafika.

14Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu;

fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni.

15Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova,

mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu.

16Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni

ndi kuonekera mu ulemerero wake.

17Iye adzayankha pemphero la anthu otayika;

sadzanyoza kupempha kwawo.

18Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo,

kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova:

19“Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba,

kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi,

20kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende,

kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.”

21Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni

ndi matamando ake mu Yerusalemu,

22pamene mitundu ya anthu ndi maufumu

adzasonkhana kuti alambire Yehova.

23Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga;

Iyeyo anafupikitsa masiku anga.

24Choncho Ine ndinati:

“Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga;

zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse.

25Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi

ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu.

26Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo;

zidzatha ngati chovala.

Mudzazisintha ngati chovala

ndipo zidzatayidwa.

27Koma Inu simusintha,

ndipo zaka zanu sizidzatha.

28Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu;

zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”

La Bible du Semeur

Psaumes 102:1-29

Prière d’un malheureux

1Prière d’une personne dans l’affliction qui se sent défaillir et qui expose sa plainte devant l’Eternel102.1 Le titre de ce psaume est unique en ce qu’il indique la circonstance de la composition mais non l’auteur du psaume..

2O Eternel, ╵écoute ma prière

et que mon appel au secours ╵parvienne jusqu’à toi !

3Ne te détourne pas de moi ╵en ce jour où je suis dans la détresse,

tends vers moi ton oreille ╵au jour où je t’appelle.

Hâte-toi de répondre !

4Comme une fumée, mes jours passent.

J’ai comme un brasier dans les os.

5Mon cœur est brisé, desséché, ╵comme l’herbe fauchée.

J’en oublie de manger ma nourriture.

6A force de gémir,

je n’ai que la peau sur les os.

7Je suis devenu comparable ╵à la corneille du désert,

je suis pareil au chat-huant ╵qui hante les lieux désolés.

8Je reste privé de sommeil,

je ressemble à un oisillon ╵resté seul sur un toit.

9Mes ennemis ne cessent ╵de m’insulter,

ils se moquent de moi ╵et maudissent les gens ╵en leur souhaitant mon sort.

10Je me nourris de cendre ╵au lieu de pain,

et ma boisson ╵est mêlée de mes larmes102.10 Voir 42.4 ; 80.6..

11Dans ton indignation ╵et ta colère,

tu m’as saisi, ╵et m’as jeté au loin102.11 Comme un tourbillon saisit des feuilles et les jette au loin..

12Tout comme l’ombre102.12 Une ombre qui s’allonge le soir : allusion au soir de la vie. qui s’étire, ╵mes jours déclinent,

et moi, je me dessèche comme l’herbe.

13Mais toi, tu sièges pour toujours, ╵ô Eternel,

et tu interviendras102.13 Ou : ton culte persistera. Litt. souvenir… ╵tout au long des générations.

14Oui, tu te lèveras, ╵et de Sion ╵tu auras compassion !

L’heure est là de lui faire grâce,

le moment est venu :

15tes serviteurs ╵ont ses pierres en affection,

ils restent attachés ╵à cette ville réduite en poussière102.15 Il s’agit des ruines de Jérusalem..

16Alors les autres peuples craindront l’Eternel,

tous les rois de la terre ╵reconnaîtront sa gloire.

17L’Eternel rebâtit Sion

pour y paraître dans sa gloire.

18Il a égard à la prière ╵de ceux qui sont dépossédés,

il ne méprisera pas leur requête.

19Que cela soit mis par écrit ╵pour la génération future,

et le peuple qui sera créé louera Eternel.

20Du haut de sa demeure sainte, ╵l’Eternel s’est penché vers nous.

Du ciel, il regarde la terre,

21et il entend les plaintes des captifs ;

et il rendra la liberté ╵aux condamnés à mort,

22pour que l’on publie en Sion ╵la renommée de l’Eternel,

sa louange à Jérusalem,

23quand se rassembleront les peuples

et les royaumes tous ensemble, ╵afin d’adorer l’Eternel.

24Il a réduit ma force ╵au milieu de ma course,

et abrégé mes jours ;

25c’est pourquoi je m’écrie : ╵« Mon Dieu, ne me fais pas mourir ╵au milieu de mes jours,

toi qui subsistes d’âge en âge !

26Tu as jadis fondé la terre,

le ciel est l’œuvre de tes mains.

27Ils périront, mais tu subsisteras ;

tous s’useront comme un habit ;

comme on remplace un vêtement, ╵tu les remplaceras ╵et ils disparaîtront.

28Mais toi, tu es toujours le même,

tes années ne finiront pas102.28 Les v. 26-28 sont cités en Hé 1.10-12..

29Les enfants de tes serviteurs ╵auront une demeure ;

sous ton regard, leur descendance ╵sera fermement établie. »