Masalimo 101 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 101:1-8

Salimo 101

Salimo la Davide.

1Ndidzayimba za chikondi ndi chiweruzo chanu cholungama;

kwa Inu Yehova ndidzayimba matamando.

2Ndidzatsata njira yolungama;

nanga mudzabwera liti kwa ine?

Ndidzayenda mʼnyumba mwanga

ndi mtima wosalakwa.

3Sindidzayika chinthu chilichonse choyipa

pamaso panga.

Ine ndimadana ndi zochita za anthu opanda chikhulupiriro;

iwo sadzadziphatika kwa ine.

4Anthu a mtima wokhota adzakhala kutali ndi ine;

ine sindidzalola choyipa chilichonse kulowa mwa ine.

5Aliyense wosinjirira mnansi wake mseri

ameneyo ndidzamuletsa;

aliyense amene ali ndi maso amwano ndi mtima wodzikuza,

ameneyo sindidzamulekerera.

6Maso anga adzakhala pa okhulupirika mʼdziko,

kuti akhale pamodzi ndi ine;

iye amene mayendedwe ake ndi wosalakwa

adzanditumikira.

7Aliyense wochita chinyengo

sadzakhala mʼnyumba mwanga.

Aliyense woyankhula mwachinyengo

sadzayima pamaso panga.

8Mmawa uliwonse ndidzatontholetsa anthu

onse oyipa mʼdziko;

ndidzachotsa aliyense wochita zoyipa

mu mzinda wa Yehova.