Masalimo 100 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 100:1-5

Salimo 100

Salimo. Nyimbo yothokoza.

1Fuwulani kwa Yehova mwachimwemwe, inu dziko lonse lapansi.

2Mulambireni Yehova mosangalala;

bwerani pamaso pake ndi nyimbo zachikondwerero.

3Dziwani kuti Yehova ndi Mulungu.

Iye ndiye amene anatipanga ndipo ife ndife ake;

ndife anthu ake, nkhosa za pabusa pake.

4Lowani ku zipata zake ndi chiyamiko

ndi ku mabwalo ake ndi matamando;

muyamikeni ndi kutamanda dzina lake.

5Pakuti Yehova ndi wabwino ndipo chikondi chake ndi chamuyaya;

kukhulupirika kwake nʼkokhazikika pa mibado ndi mibado.

Korean Living Bible

시편 100:1-5

감사와 찬양

(감사의 시)

1온 땅이여, 여호와께

기쁨으로 외쳐라.

2즐거운 마음으로 여호와를 섬기고

노래하며 그 앞에 나아가라.

3여호와가

하나님이라는 사실을 알아라.

그가 우리를 만드셨으니

우리는 그의 백성이요,

그가 기르시는 양이다.

4감사하며 성전에 들어가고

찬송하며 그 뜰에 들어가라.

그에게 감사하고

그의 이름을 찬양하라.

5여호와는 선하시고

그의 사랑은 영원하며

그의 성실하심은 대대에 이른다.