Salimo 100
Salimo. Nyimbo yothokoza.
1Fuwulani kwa Yehova mwachimwemwe, inu dziko lonse lapansi.
2Mulambireni Yehova mosangalala;
bwerani pamaso pake ndi nyimbo zachikondwerero.
3Dziwani kuti Yehova ndi Mulungu.
Iye ndiye amene anatipanga ndipo ife ndife ake;
ndife anthu ake, nkhosa za pabusa pake.
4Lowani ku zipata zake ndi chiyamiko
ndi ku mabwalo ake ndi matamando;
muyamikeni ndi kutamanda dzina lake.
5Pakuti Yehova ndi wabwino ndipo chikondi chake ndi chamuyaya;
kukhulupirika kwake nʼkokhazikika pa mibado ndi mibado.
Ein fröhliches Danklied
1Ein Lied für den Dankgottesdienst.
Jubelt dem Herrn zu, ihr Völker der Erde!
2Dient ihm voll Freude,
kommt zu ihm mit fröhlichen Liedern!
3Erkennt, dass der Herr allein Gott ist!
Er hat uns geschaffen, wir gehören ihm100,3 Oder: wir haben nichts dazu getan.!
Wir sind sein Volk, das er umsorgt wie ein Hirte seine Herde.
4Geht durch die Tempeltore ein mit Dank,
betretet die Vorhöfe mit Lobgesang!
Preist ihn und rühmt seinen Namen!
5Denn der Herr ist gut zu uns, seine Gnade hört niemals auf,
für alle Zeiten hält er uns die Treue.